من خلقني؟ ولماذا؟
Ndani adandilenga? Nanga chifukwa chiyani? Cholengedwa Chili chonse chimasonyeza kupezeka kwa Mlengi. Ndani adalenga kumwamba ndi dziko la pansi ndi zolengedwa zikuluzikulu zomwe zili mkati mwa ziwirizi zomwe sizimadziwika? Kodi ndi ndani adaika ndondomeko yokuya ndi yolongosoka bwino yakayendedwe ka zinthu kumwamba ndi dziko lapansi? Kodi ndani amene adalenga munthu ndikumupatsa makutu, maso, ndi nzeru? ndikumpatsa kuthekera kophunzira ndikudziwa zoona? Kodi mungafotokoze bwanji ndondomeko yodzama ndi yokuya ya momwe Mulungu adaikira ziwalo zapa thupi lako komanso ziwalo za zinthu za moyo?…
Cholengedwa Chili chonse chimasonyeza kupezeka kwa Mlengi.
Ndani adandilenga? Nanga chifukwa chiyani?
Ndani adalenga kumwamba ndi dziko la pansi ndi zolengedwa zikuluzikulu zomwe zili mkati mwa ziwirizi zomwe sizimadziwika?
Kodi ndi ndani adaika ndondomeko yokuya ndi yolongosoka bwino yakayendedwe ka zinthu kumwamba ndi dziko lapansi?
Kodi ndani amene adalenga munthu ndikumupatsa makutu, maso, ndi nzeru? ndikumpatsa kuthekera kophunzira ndikudziwa zoona?
Kodi mungafotokoze bwanji ndondomeko yodzama ndi yokuya ya momwe Mulungu adaikira ziwalo zapa thupi lako komanso ziwalo za zinthu za moyo? ndani adalenga zimenezo?
Kodi dziko lalikululi zimatheka bwanji zinthu kuchitika mwa ndondomeko komanso mokhazikika potengera malamulo okuya omwe akhala akuliteteza dzikoli kwa zaka zochuluka?
Ndi ndani amene adakhazikitsa ndondomeko zomwe zimayendesa dzikoli (moyo ndi imfa, kuberekana kwa zamoyo, usiku ndi usana, kusintha kwa nyengo, ndi zina zotero)?
Kodi dzikoli lidadzilenga lokha? Kapena lidangolengedwa popanda olilenga? Kapena lidangopezeka mwazizi/ mwa ngozi?
Ndi chifukwa chiyani munthu amakhulupilira kuti pali zinthu zimene sangazione? zinthu ngati: (chidziwitso, nzeru, mzimu, malingaliro, ndi chikondi) kodi sichifukwa chakuti amawona zotsatira zake? Nanga munthu angakane bwanji kukhalapo kwa Mlengi wa chilengedwe chachikuluchi pamene akuona zotsatira za zolengedwa zake ndi zotsatira za zochita zake ndi chifundo chake?!
Palibe amene angavomereze kuuzidwa kuti nyumbayi idabwera popanda wina kumanga! Kapena kumuuza kuti nyumbayi ilibe yemwe anaibweretsa! Kodi anthu ena angakhulupirire bwanji anthu amene amanena kuti chilengedwe chonsechi chinabwera popanda Mlengi? Kodi munthu woganiza bwino angavomereze bwanji kuuzidwa kuti dongosolo lolondola lachilengedwechi linangopezeka mwangozi?
Mulungu wapamwamba adanena kuti: (Kapena adalengedwa popanda Mlengi kapena iwo adadzilenga okha? Kapena iwo ndi amene adalenga mitambo ndi nthaka? koma kuti anthu amenewa ndi osakhulupilira). . [32:52].
Mulungu wapamwamba ayeretsedwe.
Pali Mulungu ndi Mlengi m’modzi yekha basi, amene ali ndi maina ndi mbiri zambiri zosonyeza kuti ndi okwanira pa chilichonse. Ena mwa maina ake ndi : Mlengi, Wachisoni chosatha, Opereka zosowa za zolengedwa,Opereka mowolowa, ndipo “Allah,” ndi dzina loziwila bwino mwa maina mlungu olemekezeka,tanthauzo lake,ndi oyenela kupembezedwa ndi iye yekha basi opanda ophatikizana naye.
Mulungu wapamwamba akuyankhula mu Quran yolemekezeka ([1]): (Nena -iwe Mtumiki Muhammad-kwa amene akukufunsa mwachipongwe za mbiri za Mulungu wako kuti: iye ndi Mulungu m'modzi. *Mulungu ndi okhala ndi zonse, odaliridwa ndi zolengedwa zake. * Sadabereke mwana komanso sadaberekedwe. *Ndiponso palibe aliyense ofanana ndi iye. [112: 1-4].
Mulungu wapamwambamwamba adanena kuti: (Palibe Mulungu opembedzedwa mwa choonadi koma iye, wamoyo wamuyaya,odaliridwa ndi zolengedwa zonse,samasinza kapena kumupeza tulo,zolengedwa zonse zili ku mwamba ndi dziko lapansi zili m'manja mwake,palibe amene angakhale ndi mphamvu zomuthandiza wina pamaso pa Mulungu kupatula Mulungu ataloleza kuti zitero,amadziwa za zolengedwa zonse zomwe zinalipo kalekale,zomwe zili pano ndi zomwe zidzalengedwe m'tsogolo,amadziwa za m'tsogolo zomwe zidzachitikire zolengedwa zake komanso zomwe zinachitika kale,palibe cholengedwa chimadziwa zobisika zake kupatula zomwe iye Mulungu wachidziwitsa cholengedwacho,mpando wa ufumu wake malo ake ndi akulu monga m'mene kulili kumwamba ndi dziko lapansi, ndipo sizimamulemera kuzisunga ndikuteteza kumwamba ndi dziko lapansi, iye Mulungu ndi wapamwamba komanso wamkulu). [2:255].
MBIRI ZA MULUNGU WAPAMWAMBA OYERETSEDWA:
Mulungu ndi amene adalenga nthaka ndikuipanga yokhazikika, ndikupanga kukhala yoyenera kuzofuna za zolengedwa zake. Mulungu ndi amene adalenga kumwamba ndi zolengedwa zazikulu zomwe zili m'menemo,ndipo adaika ndondomeko zakuya zakagwiridwe ka ntchito ka dzuwa,mwezi ,usana ndi usiku zomwe zikusonyeza ukulu wa Mulungu.
Mulungu ndi amene adatifewetsera potipatsa mpweya omwe popanda m'pweyawo ife sitingakhale ndi moyo,ndipo iye Mulungu ndi amene amatigwetsera mvula ndipo adatifewesera nyanja ndi mitsinje kudzera mu maulendo apa madzi komanso zakudya zochokera pa nyanja ndi mitsinje ngati nsomba.Ndipo iye ndi amene amatipatsa zakudya pomwe tinali makanda tili m'mimba mwa azimai athu pa nthawi yomwe tinalibe mphamvu zosaka zakudya tokha.Komanso iye ndi amene adawapanga magazi kuti adziyenda m'misempha mwathu.Ndipo adaipanganga mitima yathu kumagunda mosalekeza kuyambira tsiku limene tinabadwa mpaka tsiku lomwe tidzamwalire.
Mulungu adanena kuti: (Ndipo Mulungu adakutulutsani m'mimba mwa azimayi anu pomwe inu simudali kudziwa chilichonse,ndipo adakupatsani makutu,maso ndi mitima kuti mukhale othokoza).. [16:78].
Mulungu amene amapembedzedwa akuyenera kumadziwika ndi mbiri zachikwanekwane.
Mulungu amene ndi mlengi wathu adatipatsa nzeru kuti tidzigwiritsa ntchito pofuna kudziwa ukulu wake,ndipo anaika mwa ife chilengedwe chosonyeza kukwanira kwake ndikuti sizingatheke kuti Mulungu asimbidwe ndi mbiri zopunguka mkati mwake .
Ntchito iliyonse yabwino ikuyenera kuchitidwa pofuna kusangalatsa Mulungu m'modzi yekha amene ndi wa mbiri zokwanira amene ndi yekhayo ali oyenera kupembedzedwa. Ndipo chilichonse chimene chimapembedzedwa chosakhala Mulungu, ndi chosayenera kupembedzedwa ,chopunguka(chilibe mbiri za u Mulungu zochiyenereza kupembedzedwa),komanso chomwe chidzamwalire ndikutha.
Mulungu oyenera kupembedzedwa sangakhale munthu ,kapena fano kapena mtengo kapena chinyama!
Si zoyenera kuti munthu wanzeru kuti azipembedza chilichonse posakhala Mulungu amene ali okwanira bwino mbiri zake,nanga zitheka bwanji munthu kupembedza cholengedwa choti ndi cha pansi kuposa iyeyo!
Mulungu sizingatheke kuti nthawi ina akhale mwana wa khanda m'mimba mwa mzimai kenako ndikudzabadwa monga momwe amabadwira ana ena onse!
Mulungu ndi amene adalenga zolengedwa, ndipo zolengedwa zonse zili m'manja mwake ndi pansi pa mphamvu zake. Kotero sizingatheke kuti anthu ampatse mavuto, ndipo sizingatheke kuti wina wake amupachike pa mtanda ndikumuzunza ndikumunyoza!
SIzingatheke kuti Mulungu amwalire!
Mulungu ndi amene samaiwala, samagona,samadya chakudya; Iye ndi wamkulu amene sizingatheke kuti akhale ndi mkazi kapena mwana. Mulungu amene ndi Mlengi ali ndi mbiri zolemekezeka ndipo sizingatheke kuti asimbidwe ndi mbiri zosowekera kena kake kapena zopunguka. Mau alionse omwe mukupezeka zosemphana ndi ulemelero wa Mulungu amene ndi Mlengi mu zomwe amati ndi zoyankhula za atumiki, ndi mau anasinthidwa si oti ndi ochokera kwa Mulungu omwe adabwera nawo Mose , Yesu ndi atumiki ena mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa iwo.
Mulungu wapamwamba adanena kuti: (E inu anthu! Fanizo laperekedwa; choncho limvereni. Ndithu amene mukuwapembedza m'malo mwa Mulungu, sangathe kulenga ntchentche ngakhale atasonkhana kuti athandizane pachimenechi. Ndipo ngati ntchentche itawalanda chinthu, sangathe kuilanda chinthucho ntchentcheyo. Wafooka kwenikweni opempha ndi opemphedwa(73). Sadamulemekeze Mulungu kulemekeza komuyenera. Ndithu Mulungu ndi wamphamvu olemekezeka(74). [22:73-74].
Kodi ndi zotheka kuti Mulungu atisiye popanda kutitumizira uthenga wake?
Kodi pali nzeru kuti Mulungu adangolenga zolengedwa zonsezi popanda cholinga? Kodi adazilenga zolengedwa mwa chibwana kumachita kuti iye ndi Mulungu wa nzeru zakuya wodziwa?
Kodi ndi zotheka kuti yemwe adatilenga m’ndondomeko yotere ndi ukadaulo wake ndi kutifewetsera ife zonse zakumwamba ndi zapadziko lapansi, angatilenge popanda cholinga, kapena kutisiya opanda kutipatsa mayankho a mafunso ofunika kwambiri omwe amatizunguza nzeru monga: ndi chifukwa chiyani ife tili ndi pano? Nanga pambuyo pa imfa pali zotani? Kodi cholinga cha kulengedwa kwathu ndi chiyani?
Mulungu adatumiza Atumiki kuti tidziwe cholinga chopezekera pa dzikopa,nanga Mulungu akufuna chiyani pa ife!
Mulungu adatumiza atumiki kuti adzatiuze kuti Mulungu yekha ndi amene ali oyenera kupembedzedwa mwa choonadi, ndi kutiphunzitsa momwe tingamupembedzere, ndi kutidziwitsa malamulo ake ndi zoletsedwa zake,ndi kutiphunzitsa makhalidwe abwino omwe ngati titamawachita moyo wathu udzakhala wabwino, wodzazidwa ndi zabwino ndi madalitso.
Mulungu adatumiza atumiki ambiri monga (Nowa, Abrahamu, Mose ndi Yesu), ndipo Mulungu adawapatsa atumiki amenewa zizindikiro ndi zozizwitsa zosonyeza kukamba kwawo zoona ndi kuti adatumidwa kuchokera kwa Mlengi.
Ndipo omariza mwa aneneri a Mulungu ndi Muhammad - Mtendere ndi madalitso a Mulungu zipite kwa iye - ndipo Mulungu adavumbulutsa Qur'an yolemekezeka kwa iye.
Atumiki adatiuza momveka bwino kuti moyo omwe tikukhalawu ndi ongofuna kutiyesa mayeso,ndi kuti moyo weni weni udzakhala pambuyo pomwalira.
Ndikuti moyo omwe ukubwera kuli minda ya mtendere komwe akakhale anthu okhulupirira amene adali akupembedza Mulungu m'modzi yekha popanda kumuphatikiza ndi china chilichonse,komanso adali akukhulupilira atumiki onse. Ndikutinso kuli moto umene Mulungu wakonzera anthu osakhulupirira omwe adali kupembedza milungu ina momuphatikiza Mulungu,kapena adali akukanira mtumiki mwa mwa atumiki a Mulungu.
Mulungu wapamwamba adanena kuti:
(E, inu ana a Adam! Akakudzerani Atumiki ochokera mwa inu ndikumakuuzani za chivumbulutso changa avomerezeni ndikuwakhulupilira, choncho kwa omwe adzitchinjiriza kuzoletsedwa ndi kumachita zabwino, sadzakhala ndi mantha tsiku lotsiriza komanso pomwalira sadzakhala odandaula kalikonse pa omwe adzawasiye m'mbuyo(35). Ndipo amene atsutsa zivumbulutso zathu ndikumadzitukumula,posakhulupilira zomwe atumiki abweretsa,ndi potsasatira malamulo anga ndikusiya zomwe ndaletsa, awo ndi anthu amene akakhale akumoto komwe adzakhale kumeneko mpaka kalekale(36) [7:36-37].
Mulungu oyeretsedwa adanena kuti: (Kodi mukuganiza kuti tidakulengani chabe, ndikuti kwa ife simudzabwelera pa mbuyo pa imfa? [23:115].
QURÁN YOLEMEKEZEKA.
Qur'an yolemekezeka ndi mau a Mulungu wapamwamba mwamba, omwe adavumbulutsidwa kwa Mtumiki omariza, Muhammad, ndipo ndi chozizwitsa chachikulu kwambiri chomwe chikusonyeza kuti Muhammad ndi mtumiki wa choona - madalitso ndi mtendere zipite kwa iye- Quran ndi buku lomwe malamulo ake ndi a chilungamo ndipo nkhani zake ndi zoona.Ndipo Mulungu adawatsutsa anthu okanira kuti abweretse chaputala ngakhale chimodzi chofanana ndi Qur’an koma sadathe chifukwa cha kukongola kwa kalembedwe kake ndi luso la mau ake. Linaphatikizapo ma umboni ochuluka omveka bwino ndi mfundo za luso zomwe zikusonyeza kuti bukuli silingakhale kuti lidavumbulutsidwa ndi anthu, koma kuti ndi mau a Mulungu Mbuye wa anthu, Ulemerero ukhale kwa Iye Mulungu.
Ndi chifukwa chiyani Atumiki adatumizidwa ochuluka?
Mulungu adatumiza atumiki kuyambira kalekale kuti aitanire anthu kwa Mbuye wawo, ndikuwafikitsira malamulo ake ndi zoletsedwa zake, uthenga wawo onse udali oti: anthu adzipembedza Mulungu m'modzi yekha, wapamwamba mwamba. Ndipo nthawi zonse mtundu ukayamba kusiya kapena kupotoza pa zomwe adabweretsa Mtumiki wake, monga lamulo lomupatula Mulungu, Mulungu amatumiza Mtumiki wina kuti akonze njirayo, ndi kuwabwezeresa anthu ku chibadwa chabwino chopembedza Mulungu m'modzi ndi kumumvera Mulungu, mpaka Mulungu adatsiriza atumiki ake ndi Muhammad -mtendere ukhale pa iye,amene adadza ndi malamulo omwe adzakhale akugwira ntchito pa moyo wa anthu onse kufikira tsiku la chiweruzo, malamulo okwaniritsa ndikuchotsa malamulo akale, Mulungu adalonjeza zowatetedza malamulo amenewa kufikira tsiku la chiweruzo.
Choncho,ife Asilamu timakhulupirira - Atumiki ndi mabuku onse omwe adatumizidwa Quran isanatumizidwe monga momwe Mulungu adalamulira kuti tikhulupilire.
Mulungu wapamwamba adanena kuti: (Mtumiki wakhulupirira zimene zavumbulutsidwa kwa iye kuchokera kwa Mbuye wake. Naonso Asilamu (akhulupirira). Onse akhulupilira Mulungu, angelo ake, mabuku ake ndi atumiki ake. (Iwo pamodzi ndi Mtumiki wawoyo akunena kuti): ''Sitingalekanitse aliyense pakati pa atumiki ake. (Onse tikuwakhulupirira)."Ndipo akunena: "Tamva ndiponso tamvera. (choncho Tikukupemphani) chikhululuko chanu, E! Mbuye wathu! Ndipo kwa inu nkobwerera). "[2: 285].
Munthu sangakhale okhulupirira weni weni kufikira atakhulupirira mwa atumiki onse.
Amene adatuma atumikiwo ndi Mulungu, ndipo munthu amene angakanire uthenga wa m'modzi wa iwo, ndiye kuti wakanira onse, ndipo palibe tchimo lalikulu loposa kuti munthu akane chivumbulutso cha Mulungu.Choncho, kuti munthu akalowe ku mtendere akuyenera kukhulupirira atumiki onse.
Ndi zofunika kwa munthu wina aliyense pa nthawi ino kuti akhulupilire mwa atumiki onse a Mulungu, ndipo izi sizingatheke pokhapokha atakhulupilira ndi kutsatira mtumiki otsiriza mwa iwo, Muhammad-Madalitso ndi Mtendere zipite kwa iye.
Mulungu adatchula mu Qur’an kuti amene akukana kukhulupilira m’modzi mwa Atumiki a Mulungu ndiye kuti ndi munthu okanira Mulungu ndiponso ndi okanira mau ake.
Werengani vesi ili: "Ndithudi anthu-ochokera mwa ayuda ndi akhirisitu- amene sakhulupirira mwa Mulungu ndi Atumiki ake, ndikumafuna kulekanitsa pakati pa Mulungu ndi Atumiki ake pokhulupilira ena mwa atumiki ake ndikumawakana atumiki ena, ndikumafuna kuika njira yopeka yosocheretsa anthu(150) Anthu amenewo ndi omwe ali osakhulupilira eni eni, ndipo anthu osakhulupilira tawakonzera zilango zowakhumudwitsa ndikuwanyozetsa"(151). [4:150-151].
Kodi Chisilamu ndi chiyani?
Chisilamu ndi kugonjera mwa Mulungu wa mphamvu zonse pokhulupilira za umodzi wa Mulungu,kumugonjera potsatira malamulo ake, ndi kumatsatira pochita malamulo ake mwa nsangala ndi kuwavomereza.
Ndithu Mulungu adatumiza atumiki ndi uthenga umodzi: kuwalamulira anthu kuti azipembedza Mulungu m'modzi yekha, popanda omuphatikiza naye.
Chisilamu ndi chipembedzo cha Aneneri onse, ndipo uthenga wawo ndi umodzi,ndipo malamulo awo adali ndi osiyana. Asilamu masiku ano ndi okhawo amene amatsatira chipembedzo cholondola chimene Aneneri onse anabweretsa, ndipo uthenga wa Chisilamu mu nthawi ino ndi omwe uli owona. Ambuye Mulungu amene adatumiza Ibrahim, Musa, ndi Yesu ndi amene adatumiza Mtumiki omariza Muhammad, ndipo chilamulo cha Chisilamu chidadza ndikuchotsa malamulo omwe adadza patsogolo pake.
Ndithudi Zipembedzo zonse zomwe anthu amapemphera masiku ano - kupatula Chisilamu-,ndi zipembedzo zopangidwa ndi anthu, kapena zipembedzo zomwe zidali zochokera kwa Mulungu kenako ndi kusokonezedwa ndi manja a anthu ndipo zidakhala zosakanikirana ndi zinyalala zanthano, nthano zoyamwira, ndi maganizo a anthu.Pomwe chikhulupiriro cha Asilamu, ndi chikhulupiriro chimodzi chomveka bwino chomwe sichisintha, ndipo yang'ana buku la Qur’an lolemekezeka, ndi buku limodzi lomwe limagwiritsidwa ntchito mu maiko onse a Chisilamu.
Mulungu wapamwamba adayankhula mu Qur'an kuti:
Nena iwe Muhammad kwa anthu okhulupilira kuti anene kuti: takhulupirira mwa Mulungu ndi zomwe zavumbulutsidwa kwa ife, ndi zomwe zidavumbulutsidwa kwa Ibrahim, Ismail,Issac, Yakobo, ndi zidzukulu zake komanso mabuku omwe adapatsidwa Mussa,Yesu ndi aneneri ena onse kuchokera kwa Mbuye wawo ndipo sitisiyanitsa aliyense pakati pawo,ndipo ife tagonjera mwa iye (Mulungu)." Ndipo amene angatsate chipembedzo chosakhala Chisilamu, sichidzalandiridwa kwa iye,ndipo tsiku lomariza adzakhala m'modzi mwa anthu oludza [3:84-85].
Kodi Asilamu amakhulupirira chiyani zokhuza Yesu?
Kodi mumadziwa kuti Asilamu amayenera kumukhulupilira M'neneri wa Mulungu Yesu, kumamukonda, kumamulemekeza, ndi kumakhulupilira uthenga wake, omwe unali owaitanira anthu zopembedza Mulungu m'modzi yekha popanda omuphatikiza naye! Ndipo Asilamu amakhulupilira kuti M'neneri Yesu ndi Muhammad (madalitso ndi mtendere zikhale pa iwo) adali aneneri, ndikuti adatumizidwa kuti awasonyeze anthu njira ya Mulungu ndi njira yokalowera ku paradiso.
Ife timakhulupilira kuti Yesu-mtendere ukhale pa iye-,adali m’modzi mwa atumiki akulu akulu amene adatumizidwa ndi Mulungu wapamwamba, ndipo timakhulupilira kuti anabadwa mozizwitsa. Mulungu watiuza mu Qur’an kuti adamulenga Yesu popanda atate wake, monga momwe adachitira pomulenga Adamu popanda bambo kapena mai, Mulungu ndi okutha ndikukwaniritsa kuchita chilichonse.
Komanso timakhulupilira kuti Yesu si Mulungu komanso si mwana wa Mulungu, ndipo sanapachikidwe, iye adakali ndi moyo.Mulungu adamunyamula kupita kwa Mulunguyo ndikuti adzatsika kumapeto kwa dziko pomwe adzakhale akulamula mwa chilungamo, ndipo adzakhala ndi Asilamu chifukwa Asilamu ndi amene ali okhulupilira za umodzi wa Mulungu, omwe ndi uthenga umene udabwera ndi Yesu komanso atumiki onse.
Mulungu watiuza mu ’Qur’an yolemekzeka kuti Akhirisitu adasintha uthenga omwe udabwera ndi Yesu, ndikuti pali anthu osochera amene adasintha uthenga omwe udavumbulutsidwa mu baibulo ndipo adaonjezera mau awo oti Yesu sadayankhule. Zomwe zikuikira umboni zakusinthidwa kwa uthenga wa Yesu, ndikuchuluka kwa mabuku a baibulo komanso kuchuluka kwa mau otsutsana mu mabukuwo.
Mulungu watiuza kuti Yesu amapembedza Mbuye wake ndipo sadamulamulire wina aliyense kuti azimupembedzaYesuyo. Iye Yesu adali akuwalamulira anthu ake kuti adziapembedza Mlengi wake iyeyo, koma Satana adawapangitsa Akhrisitu kuti adzimupembedza Yesu.Mulungu watiuza mu Qur’an kuti iye sadzamukhululukira wina aliyense amene amapembedza zina kusiya Mulungu, ndi kuti Yesu pa tsiku lotsiriza adzawakana anthu amene amamupembedza iye powauza kuti: “Ndidakulamulilani kuti mudzipembedza Mlengi, ndipo sindidaskulamulileni kuti mudzindipembedza ine . Ena mwa maumboni a izi , ndi mau a Mulungu wapamwamba:
(Ee inu anthu a Buku! Musamalumphe malire pa Chipembedzo chanu,ndipo musamnenere Mulungu koma zowona (zokha zokha). Ndithu Mesiya- Yesu mwana wa Maria-, ndi mtumiki wa Mulungu amene adabadwa kudzera mu mphamvu ya mau ake oti ukhale chakuti omwe adawaika kudzera mwa Maria,komanso adautsira mzimu mwa Yesu ochokera kwa Mulunguyo (umo achitira ndi mizimu ya zolengedwa zonse). Choncho, Khulupilirani mwa Mulungu ndi atumiki ake. Musamanene za "utatu wa Mulungu; "siyani zikhulupiliro za utatu wa Mulungu. Kutero ndi zabwino kwa inu. Ndithudi, Mulungu ndi Mulungu m'modzi . Ulemelero ndi wake, ndipo ngotukuka kutali ndi kukhala ndi mwana. Zonse zakumwamba ndi dziko la pansi ndi zake, Mulungu wakwanira kukhala mtetedzi). [4:171].
Mulungu wapamwamba adanena kuti: (Ndipo kumbukira za tsiku lotsiriza pamene Mulungu adzanena kwa Yesu kuti: Kodi iwe Yesu udali kuwaudza anthu kuti nditengeni ine ndi mai wanga kukhala milungu iwiri yopembedzedwa kusiya Mulungu? Yesu adzayankha kuti: Ulemelero ukhale pa inu,sikunali koyenera kwa ine kunena zomwe sizili zoyenera kundichitira ine, ngati ndidanena, ndiye kuti mukudziwa chifukwa palibe chimabisika kwa inu, Inu mukudziwa zomwe zili mumtima mwanga, pomwe ine sindidziwa zomwe zili mwa inu. Ndithudi, inu ndinu odziwa zoonekera ndi zobisika zomwe). [5:116].
Kwa munthu amene akufuna kukapulumuka ku moyo umene ukubwera, akuyenera kulowa Chisilamu ndikumutsatira mtumiki Muhammad-mtendere ndi madalitso zikhale pa iye.
Mwa zinthu zoona zomwe atumiki onse adagwirizana,ndi zoti palibe amene akapulumuke pa tsiku lotsiriza osakhala Asilamu, anthu amene adakhulupilira mwa Mulungu ndipo samamuphatikiza iye ndi wina aliyense, komanso adakhulupilira atumiki onse. Anthu amene adali mu nthawi ya M'neneri Mose,ndipo adamukhulupilira iye ndipo adali akumatsatira chiphunzitso chake, amenewo adali Asilamu, anthu okhulupilira ndi olungama, koma pa mbuyo pomutumiza Yesu kukhala mtumiki, zinali zokakamizidwa kwa anthu omwe amamutsatira Mose kuti amukhulupilire Yesu ndikumamutsatira. Kwa anthu omwe adamukhulupilira Yesu, amenewo ndi Asilamu, anthu okhulupilira ndi olungama. Ndipo munthu amene angakane kumukhulupilira Yesu, ndikumanena kuti ine ndipitirizabe kutsatira Mose, amene si munthu okhulupilira kweni kweni; chifukwa kumeneko ndikukana kukhulupilira mtumiki amene Mulungu adamutumiza. Pambuyo poti Mulungu watumiza mtumiki omariza Muhammadi, ndi zokakamiizidwa kwa anthu onse kumukhulupilira mtumiki omarizayo. Mulungu ndi amene adatumiza Mose,Yesu, komanso iye ndi amene adatumiza Mtumiki otsiriza Muhammad (SAW). Tsono, kwa munthu amene angakanire uthenga wa Muhammad-mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa iye-,ndikunena kuti:Ndipitirizabe kutsatira Mose kapena Yesu, munthu ameneyo si okhulupilira weni weni.
Si kokwanira kwa munthu kungonena kuti amawalemekeza Asilamu, komanso si zokwanira kuti munthu kungopereka cha ulere ndikuthandiza osauka,kuti akakhale opambana moyo umene ukubwera,koma akuyenera kukhala okhulupilira mwa Mulungu, mabuku ake, atumiki ake, ndi tsiku lomariza; kuti Mulungu akamulandire ntchito zakezo.Palibe tchimo lalikulu kuposa kumuphatikiza Mlungu ndi zinthu zina, kumukanira Mlungu, kutsutsa chivumbulutso chimene Mulungu adavumbulutsa, kapena kukana uneneri wa Mtumiki wake omariza, Muhammad-mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa iye. Ayuda ndi Akhrisitu amene adamva za utumiki wa Muhammad, Mtumiki wa Mulungu-mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa iye- ndipo adakana kumukhulupilira mtumikiyo ndi kukana kulowa m’chipembedzo cha Chisilamu; iwo adzakhala kumoto wa mpaka muyaya, monga momwe Mulungu Wapamwamba adanenera:
{Anthu amene sadakhulupilire mwa magulu Ayuda, Akhirisitu komanso anthu omuphatikiza Mulungu ndi zinthu zina, zilango zawo ndikukalowa ku moto wa Gahena kumene akakhaleko mpaka muyaya, magulu a anthu atchulidwawa ndi zolengedwa zomwe zili zoipitsisa}. [6:98].
Popeza uthenga omariza ochokera kwa Mulungu kupita kwa anthu wavumbulutsidwa, aliyense amene wamva za Chisilamu ndi kumva za Mtumiki otsiriza Muhammad-mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa iye- akuyenera kumukhulupilira, kutsatira malamulo ake, ndi kumumvera pa zomwe adalamulira kuti tizichita ndi kusiya zomwe adatiletsa. Choncho,amene angamve za uthenga omarizawu ndi kuukana, Mulungu sadzalandira ntchito zake tsiku la chiweruzo ndipo adzamulanga ku umoyo omwe ukubwera. Ena mwa ma umboni a zimenezi ndi mau ake Mulungu wapamwamba:
(Munthu amene angafune Chipembedzo china chosakhala Chisilamu, Mulungu pa tsiku lotsiriza sakalandira ntchito zake ndipo moyo omwe ukubwera akakhala gulu la anthu oluza). [3:85].
Adanenanso Mulungu wapamwamba: (Nena-iwe mtumiki-uwauze eni mabuku Ayuda ndi Akhirisitu: bwerani ku liwu lomwe lili la chilungamo ndi loona lomwe tonse tikuyenera kulitsatira: loti tidzipembedza Mulungu m'modzi yekha, ndikuti tisamamuphatikize ndi zinthu zina monga mafano, miyala, satana ndi zina zotero, ndikuti pasapezeke mwa ife umutenga nzake kukhala Mulungu opembedzedwa kusiya Mulungu m'modzi. Koma ngati atakana pambuyo pamaitanidwe abwinowa, auzeni iwowo-inu anthu okhulupilira kuti-: ikirani umboni kuti ife ndi Asilamu omwe tavomereza zopembedza Mulungu m'modzi yekha). (3:64).
Kodi ndi chiyani chikufunika ndichite kuti ndikhale Msilamu?
Kuti munthu alowe m'chisilamu, akuyenera kukhulupilira nsichi zisanu ndi imodzi izi:
Kukhulupilira mwa Mulungu wapamwamba kuti iye ndi Mlengi, opereka zosowa, oyendetsa zinthu zonse,mwini chilichonse ndikuti palibe chilichonse chofanana ndi iye, alibe mkazi ngakhale mwana, ndikuti iye yekha ndi amene ali oyenera kupembedzedwa mwa choondi.
Kukhulupilira mwa Angelo kuti iwowo ndi akapolo a Mulungu wapamwamba mwamba, ndikuti adawalenga kuchokera mu kuwala. Ndipo adazipanga zina mwa ntchito zawo kubweretsa uthenga wa Mulungu kwa atumiki a Mulungu.
Kukhulupilira mabuku onse amene Mulungu adavumbulutsa kwa Aneneri Ake (monga chipangano cha kale ndi cha tsopano), ndikuti buku lomariza ndi Qur’an.
Kukhulupilira mwa atumiki onse monga Noah, Abraham, Mose, Yesu, ndipo otsiriza mwa atumikiwo ndi Muhammad. Atumikiwa ndi anthu omwe Mulungu amawavumbulutsira mau ake ndikupatsa zizindikiro ndi zozizwitsa zosonyeza kuyankhula kwawo zoona.
Kukhulupirira za tsiku lomariza lomwe Mulungu adzaukitsa m'manda anthu oyambilira ndi omarizira kuwalenga, ndikudzaweruza Mulungu pakati pa akapolo ake mu zomwe adali akusemphana pa chipembedzo, ndikuwalowesa anthu okhulupilira ku mtendere, komanso anthu okanira ku moto.
Kukhulupilira za chikonzero cha Mulungu,ndikuti Mulungu amadziwa chilichonse, zomwe zidalipo kale ndi zomwe zidzachitike mtsogolo, ndikuti Mulungu adalemba zimenezo, adachifuna, ndipo adalenga chilichonse.
Chisilamu ndi njira ya chisangalaro:
Chisilamu ndi chipembedzo cha aneneri onse ndipo si chipembedzo cha aluya okha.
Chisilamu ndi njira yomubweretsera munthu mtendere weni weni pa dziko pano komanso mtendere okhazikika ku moyo omwe ukubwera.
Chisilamu ndi chipembedzo chokhacho chomwe chimatha kukwaniritsa zosowa za moyo ndi thupi, ndikuthetsa mavuto onse a anthu.
Mulungu wapamwamba adanena kuti:
{Mulungu adati: Tsikani pansi awiri nonsenu (Adam ndi Satana)kuchokera kuno kupita pa dziko la pansi komwe mukakhale adani pakati panu. Muli pa dzikopo,chikakakupezani chiongoko kuchokera kwa ine(Mulungu), kwa munthu amene adzikatsatira chiongoko changa sadzasokera pa dziko la pansi kapena kukhala wa tsoka tsiku lotsiriza pokalowa kumoto. Kwa munthu amene angaonese nsana ndikuzitalikitsa potalikira ndi mau anga omwe ndikumukumbutsa nawo(Quran ndi zochita za mtumiki), ndithudi moyo wa masautso pa dziko la pansi (ngakhale atamaoneka kuti ali ndi mtendere pamaso pa anthu),ndipo adzalangidwanso m'manda,pa tsiku lotsiriza adzasonkhanisidwa ali munthu osapenya}. [20:123-124].
Kodi ndingapindule chani ngati nditalowa chisilamu?
Kulowa m'Chisilamu kuli ndi ma ubwino akulu, ena mwa ma ubwinowo ndi:
-Chipambano ndi ulemelero padziko lino lapansi chifukwa amakhala kapolo wa Mulungu yekha, akapanda kulowa chisilamu amakhala kapolo wa zilakolako,satana ndi zokhumba za moyo.
-Kupambana kwakukulu pa tsiku lomariza komwe ndi kupulumutsidwa ku chilango chaku moto,ndi kulowa ku minda ya mtendere,ndikupeza chisangalalo cha Mulungu ndikukhazikika mpaka muyaya ku minda yaku mtendere.
-Ndipo anthu omwe Mulungu akalowese ku minda ya mtendere, akakhala pa mtendere wa muyaya popanda kumwalira kapena kudwala mtundu ulionse wa matenda kapena kumva kuwawa kapena kudandaula, ndipo adzikapeza kalikonse komwe adzikakafuna.
Ku minda yaku mtendere kuli zisangalalo zoti maso sanayambe ataona,makutu sanayambe atamva ndipo sizinayambe zitabwera mu maganizo a munthu.
Ena mwa ma umboni a izi ndi mau a Mulungu wapamwamba: (Kwa munthu amene angamagwire ntchito zabwino,mamuna kapena mkazi ali munthu okhulupilira,tidzamukhazika umoyo wabwino odekha(ngakhale atakhala wa chuma chochepa),ndipo tidzawapatsa malipiro awo abwino tsiku lotsiriza potengera ntchito zabwino zomwe amachita pa dziko) [16:97].
Kodi ndingaluze chani ngati nditakana kulowa chisilamu?
Munthu adzaluza maphunziro akulu omwe ndi maphunziro okhuza Mulungu. Komanso adzaluza mwai okhulupilira mwa Mulungu amene amamupatsa munthu mtendere ndikudekha pa dziko lino la pansi,komanso mtendere wa muyaya moyo omwe ukubwera.
Munthu adzataya mwayi owerenga buku lalikulu kwambiri limene Mulungu adalivumbulutsa kwa anthu,komanso adzaluza mwayi okhulupilira bukuli.
Adzaluzanso mwayi okhulupilira mwa Aneneri olemekezeka,monga momwe adzaluzilenso mwayi okhala limodzi ndi atumiki tsiku lotsiriza, ndipo m'malo mwake adzakhala limodzi ku moto ndi satana komanso anthu ochita zoipa ndi zimafano zomwe zimapembededwa zikusangalasidwa,kaye kunyasa
Mulungu wapamwamba adanena kuti:
(Nena-kwa iwo iwe Muhammad-: Ndithu anthu oluza, ndi anthu omwe akaluze tsiku la chiweruzo pamodzi ndi aku banja kwawo,ndithudi kumeneko ndi kuluza kweni kweni(15) Anthu omwe adzakhale oluza pa tsiku lotsiriza adzakhala ndi zilango za moto pa mwamba pawo zomakhala ngati mthunzi ochita kumangidwa,chonchonso zilango zochokera pansi pawo, zilango zomwe Mulungu akuzifotokozazi akufuna kuwaopseza akapolo ake kuti azimuopa Mulunguyo, choncho ndiopeni ine inu akapolo anga pochita zomwe ndalamulira ndikusiya zomwe ndaletsa} [39:15-16].
Osachedwetsa chiganizo cholowa chisilamu!
Dziko lapansi simokhalamo muyaya...
Zokongola ndi zilako lako zonse za dziko la pansi zidzatha.
Lidzafika tsiku lomwe udzawerengesedwe pa chilichonse chimene udachita, lomwe ndi tsiku la chiweruzo. Mulungu Wampamwamba adati: {Ndipo kaundula adzaikidwa (pamaso pawo) Ndipo udzaona oipa ali oopa chifukwa cha zomwe zili m'menemo (mu mabuku a ntchito zawo),ndipo adzanena modzidandaulira kuti: kalanga ife taonongeka! Ndi buku lanji ili! losasiya chaching'ono ngakhale chachikulu, koma zonse kuzilemba ndipo adzapeza zonse zimene adazichita zitalembedwa m'menemo,ndipo Mbuye wako sapondereza aliyense (pomusenzetsa zomwe sizake kapena kumchitira zomwe sizikumuyenera). [18:49].
Mulungu wapamwamba watiuza kuti munthu amene sagonjera ndikulowa Chisilamu ndithu malo ake okafikira ndi kumoto komwe adzakhaleko mpaka kale kale.
Kuluza si chinthu chophweka,koma ndi chinthu cholemetsa ndikupweteka: {Ndipo amene angatsate Chipembedzo china chosakhala chisilamu, sichizalandiridwa kwa iye. Ndipo iye tsiku lomariza adzakhala m'modzi mwa oluza}. [3:85].
Chisilamu ndi chipembedzo chomwe Mulungu tsiku lotsiriza sakalandira zipembedzo zina posakhala chisilamu chokha.
Mulungu ndi amene adatilenga, ndipo kwa iye tidzabwerera, ndikuti moyo wa dziko lapansi ndi mayeso kwa ife.
Khalani ndi chitsimikizo kuti : moyo uno ndi waufupi ngati maloto...ndipo palibe amene akudziwa kuti adzamwalira liti!
Kodi yankho lako lidzakhala lotani kwa Mlengi wanu akakakufunsa tsiku lotsiriza kuti: Bwanji siunatsatire choona pambuyo pochidziwa? Chifukwa chiyani siunamutsatire Otsiriza mwa Aneneri?
Kodi udzamuyankha chiyani Mbuye wako pa tsiku lotsiriza?, Chonsecho wakuchenjezani zakuipa kosalowa chisilamu, ndipo wakuuzani zoti anthu okanira akafikira ku ng'anjo ya moto yomwe ikuwadikira tsiku lotsiriza.
Mulungu wapamwamba adanena kuti: (Koma amene sanakhulupilire natsutsa mau athu, Iwowo ndiwo anthu akumoto komwe akakhale mpaka muyaya) [2:39].
Palibe chifukwa chomveka chomwe akapereke munthu amene adasiya kusatira choona m'malo mwake ndikumatsatira makolo ndi azigogo ake.
Mulungu wapamwamba adatiuza kuti anthu ambiri amakana kulowa Chisilamu chifukwa choopa malo omwe amakhala.
Anthu ambiri amakana Chisilamu chifukwa chakuti safuna kusintha zikhulupiriro zawo zomwe adatengera kwa makolo awo ndi zomwe adazizolowera, ndipo ambiri mwa iwo amaletsedwa ndi kuchita zinthu kamba ka nsankho komanso kufuna kuteteza zabodza zomwe adatengera kwa makolo awo.
Anthu onsewa alibe chifukwa chomveka kuwalesa kulowa chisilamu pa zifukwa zomwe zakambidwazi,ndipo akadzaima pa maso pa Mulungu tsiku lotsiriza adzakhale alibe umboni omveka omwe sadalowere chisilamu.
Palibe chifukwa chomveka kwa munthu amene samakhulupilira zoti kuli Mulungu kuti ayankhule mau oti:"Ndidzapitirizabe kukhala osakhulupirira kuti Mulungu alipo chifukwa ndinabadwira m’banja losakhulupirira kuti kuli Mulungu!”.M’malo mwake, akuyenera kugwiritsa ntchito nzeru zake zimene Mulungu adamupatsa, ndi kumasinkhasinkha za zilengedwe zikulu zikulu ngati kumitambo ndi nthaka, ndi kumalingalira pogwiritsa ntchito nzeru zake zomwe Mlengi wake adamupatsa kuti athe kudzindikira kuzera mu nzeruzo kuti dzikoli lili ndi Mlengi wake. Chimodzimodzi,munthu amene amapembedza miyala ndi mafano alibe chifukwa chomveka chowatsatilira makolo ake popembedza zimenezo, chomwe chili chofunikira kwa iyeyo ndi kufufuza choona cheni cheni ndi kumadzifunsa yekha kuti: zitheka bwanji ine kuti ndizipembedza chinthu chopanda moyo choti sichimandimva ngakhale kundiona kapena kundithandiza pa china chilichonse?
Chimodzimodzinso M'khirisitu amene amakhulupilira zinthu zosemphana ndi chilengedwe chabwino cha munthu ndi nzeru zabwino,akuyenera kumadzifunsa yekha kuti: kodi zingatheke bwanji kuti Mulungu amuphe mwana wake amene analibe mchimo lomwe anachita lomuyenereza kuphedwa chifukwa cha machimo a anthu ena! Uku ndikupanda chilungamo! Zingatheke bwanji kuti anthu amupachike pa mtanda ndikumupha mwana wa Mulungu?Kodi Mulungu alibe kuthekera kokhululuka machimo a anthu popanda kuwalola anthu kuti aphe mwana wake Mulunguyo?Kodi Mulungu alibe kuthekera komuteteza mwana wake kuti asaphedwe?
Ndi zoyenera kwa munthu wanzeru kutsatira choona, osati kutsanzira makolo ndi azigogo ake pa zinthu za bodza.
Mulungu wapamwamba adanena kuti: (Ndipo akauzidwa: Tadzani kuchilungamo cha zomwe Mulungu wavumbulutsa ndi (zomwe Akunena) Mtumiki ,amanena kuti: Tikukwaniritsidwa ndi zomwe tidawapeza nazo makolo athu akuchita ," kodi iwo atsatira za makolo awo ngakhale atakhala kuti makolo awowo sadali kudziwa chinthu chili chonse ndipo sadali owongoka, (awatsatirabe)? [5:104].
Kodi munthu amene akufuna kulowa Chisilamu koma akuziopezera yekha kumadzuzo ochokera kwa abale ake achite chiyani?
Munthu amene akufuna kulowa Chisilamu koma akuopa anthu omwe amuzungulira, atha kulowa Chisilamu ndi kumabisa zakulowa kwake Chisilamu kufikira nthawi imene Mulungu adzamupepusire njira yabwino ndikukhala ozimira pa yekha ndikumaonesera zoti iyeyo ndi Msilamu.
Ndi zofunika kwa iwe kulowa Chisilamu pa nthawi yomwe wachimvesesa,koma sizokakamizidwa kwa iwe kuwauza anthu omwe akuzungulira zakulowa kwako chisilamu kapena kulengeza zakulowa chisilamu kwako, ngati patakhala kuti pali zopweteka zomwe zingakupeze pambuyo polengeza.
Ndipo udziwe kuti ukalowa chipembedzo cha Chisilamu,udzakhala m'bale wa asilamu ochuluka kwambiri, ndipo utha kulumikizana ndi anthu oyang'anira mzikiti kapena malo ochitira zinthu za chipembedzo cha chisilamu dera la kwanu,ndikuwapempha kuti ukambirane nawo kapena kuwapempha thandizo, ndipo anthuwo zidzawasangalatsa zakulowa kwako chisilamu komanso adzakuthandiza.
Mulungu wapamwamba adanena kuti:
{Ndipo amene akumuopa Mulungu (potsatira malamulo ake) amuikira njira yotulukira mu zovuta zake ndikumupatsa zosowa zake mu njira yoti samayembekezera}. [65:2-3].
Okondedwa owerenga
Kodi kumukondweresa Mulungu amene ndi mlengi wako-amene adakupatsa mtundu ulionse wa mtendere, amene amakupatsa chakudya uli mwana wosabadwa m'mimba mwa mai ako,ndipo amakupatsa mpweya umene ukupuma panowo-kodi Mulungu ameneyo ndi amene ali ofunika kumusangala?
Kodi mayesa kuti munthu akhale opambana pa dziko pano komanso moyo ukubwera ,akuyenera kuzipereka posiya zilakolako zokutha za moyo uno?nde, ndikulumbira!
Choncho,usalole kuti zolakwika zako zakale zikukanikise kukonza zolakwika zakalezo ndikuchita zinthu zabwino.
Khala okhulupilira weniweni lero! Usalole Satana kukuimitsa kuti usatsatire choona.
Mulungu wapamwamba adanena kuti:
(E inu anthu! Ndithudi, wakubwelerani inu umboni-omwe ndi mtumiki wathu Muhammad- ochokera kwa Mbuye wanu,ndipo takuvumbulutsirani inu buku kukhala chiongoko komanso dangalira lokunikira njira yoongoka(174) Tsono anthu amene akhulupilira mwa Mulungu ndi kugwiritsitsa buku la Quran,anthu amenewo pa tsiku lotsiriza Mulungu adzakawalowesa ku minda yaku mtendere chifukwa cha chisoni ni ubwino wake Mulunguyo,ndipo pa dziko la pansi lino awafewesera kuti adziyenda njira yowongoka yokawafikitsa ku minda yaku mtendere tsiku lotsiriza(175). [4:174-175].
Kodi ndiwe okonzeka kuchita chiganizo chachikulu kwambiri pa moyo wako?
Ngati zonsezi zikumveka kwa iwe,ndiye kuti mtima wavomereza za choona. Choncho ukuyenera kuchita chinthu choti ulowe usanduke msilamu. Kodi ukufuna kuti ine ndikuthandize kuchita chiganizo chabwino pa moyo wako,komanso ndikusonyeze njira yomwe ungasate kuti usanduke msilamu?
Usawachite machimo ako kuti akuletse kulowa m'chisilamu. Mulungu watiuza mu buku la Qur’an kut iye amakhululuka machimo onse a munthu ngati walapa kwa mlengi wake ndikulowa chisilamu. Ngakhalenso pambuyo polowa chisilamu, ndi chilengedwe cha munthu kulakwa popanga machimo ena kamba koti ndife anthu sikuti ndife angelo omwe ali otetezedwa ku machimo. Koma zomwe zili zofunikira kwa ife ndikupempha chikhululuko kwa Mulungu ndikumalapa machimo athu kwa iye, ndipo Mulungu akaona mwa iwe kuti wafulumiza povomereza zoti chisilamu ndi chipembedzo choona ndipo walowa m'chisilamu, ndikuyankhula mau oikira umboni za umodzi ndikuyenera kopembedzedwa Mulungu yekha ndikuikiranso umboni za utumiki wa Muhammad,Mulungu adzakuthandiza pokupepusira kusiya machimo ena. Poonjera apo, munthu amene amabwelera kwa Mulungu ndikumatsatira choona,Mulungu amamupepusira kuti adzichita zabwino. Choncho, usachite chidodo polowa chisilamu panopa.
Ena mwa ma umboni a izi ndi kuyankhula kwa Mulungu wapamwamba: (Nena kwa osakhulupilira kuti: ngati asiya zochita zawo zoipa adzakhululukidwa zimene machimo omwe adatsogoza..). [8:38].
Nditani kuti ndikhale msilamu?
Kulowa m’chisilamu ndi chinthu chopepuka ndipo sichifuna miyambo, kapena kukonza mwambo wapadera, kapena kupezeka kwa odziwika wina aliyense. Munthu akuyenera kuyankhula mau oikira umboni umodzi wa Mulungu popembedzedwa komanso utumiki wa Muhammad uku akudziwa bwino lomwe tanthauzo lake ndi kuwakhulupilira mau ndi matanthauzowo,ponena kuti:(Ndikuikira umboni kuti palibe Mulungu oyenera kupembedzedwa mwa choonadi koma Mulungu m'modzi yekha, ndikuikiranso umboni kuti Muhammad ndi mtumiki wa Mulungu), ngati kuli kotheka kwa iwe kunena zimenezo mu chinenero cha chiluya ndi zabwino, ngati zitakuvuta kutero,ndi zokwanira kunena mu chinenero chako ndipo umakhala kuti ndiwe msilamu.Kenako ukuyenera kuphunzira malamulo achipembedzo chako, chomwe chingakhale chiyambi chakupambana kwako moyo uno komanso chipulumutso chako moyo omwe ukubwera.
Kuti mudziwe zambiri za malamulo a Chisilamu, ndikukulangiza zowerenga zomwe zili pa tsamba ili:
Kuti mudziwe momwe mungachitire malamulo a Chisilamu, tikukulangizani kuti mulowe pa tsamba lino: