Skip to content
وجوب العمل بالسنة وكفر من أنكرها

وجوب العمل بالسنة وكفر من أنكرها

CHIKAKAMIZO CHOGWIRITSA NTCHITO SUNNA ZA MTUMIKI(SAW)NDIKUKANIRA KWA MUNTHU YEMWE ANGAZIKANE SUNNAZO. WOLEMBA BUKU: ABDUL AZIZ BIN ABDUL ALLAH BIN BAZ(ALLAH AWACHITIRE CHISONI). M'dzina la Mulungu ,Wachifundo Chambiri ,Wachisoni Chosatha. MAU OYAMBA Kuyamikidwa konse ndikwa Mulungu, mbuye wa zolengedwa zonse, ndipo mathero abwino pa chinthu chilichonse amakhala kwa anthu oopa Mulungu, mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa kapolo komanso mtumiki wake,mneneri wathu Muhammad; amene anatumizidwa kuti akhale ozichitira chisoni zolengedwa zonse,komanso mtendere ukhale kwa anthu aku banja…

Language: lang_ny
Prepared by:
Version: 1.0

CHIKAKAMIZO CHOGWIRITSA NTCHITO SUNNA ZA MTUMIKI(SAW)NDIKUKANIRA KWA MUNTHU YEMWE ANGAZIKANE SUNNAZO. WOLEMBA BUKU:

ABDUL AZIZ BIN ABDUL ALLAH BIN BAZ(ALLAH AWACHITIRE CHISONI).

M'dzina la Mulungu ,Wachifundo Chambiri ,Wachisoni Chosatha.

MAU OYAMBA

Kuyamikidwa konse ndikwa Mulungu, mbuye wa zolengedwa zonse, ndipo mathero abwino pa chinthu chilichonse amakhala kwa anthu oopa Mulungu, mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa kapolo komanso mtumiki wake,mneneri wathu Muhammad; amene anatumizidwa kuti akhale ozichitira chisoni zolengedwa zonse,komanso mtendere ukhale kwa anthu aku banja kwake,ophunzira ake anthu amene anatenga uthenga ochokera mu buku la mbuye wawo pamodzi ndi chiphunzitso(sunna) cha mtumiki wawo-mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa mtumikiyo-kupitisa kwa anthu omwe adabwera pambuyo pawo, mokhulupirika kwambiri ndi molondoloza,komanso kuteteza matanthauzo ndi mau a bukuli ndi sunna-Mulungu asangalasidwe nawo ophunzira onsewo ndikusangalasa powapasa malipiro abwino- ndikuti atipange ife kukhala owatsatira iwowo mu zinthu zabwino,ndikuti tidzakhale mboni za mulungu pa akapolo ake onse, pambuyo pa mau awa:

Anthu ophunzira kuyambira akale ndi atsopano, adagwirizana kuti mapata a malamulo odalirika potsindika za malamulo achipembedzo, ndi kufotokoza zinthu zololedwa ndi zoletsedwa ndi buku la Mulungu lomwe ndi lotetedzedwa mau komanso matanthauzo ake,kenako chiphunzitso(sunna)cha mtumiki wa mulungu -mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa iye-amene samayankhula za m'mutu mwake ,koma kuti zonse amayankhula zimachokera kwa Mulungu mu njira zosiyanasiyana,tsinde lina la malamulo ndi mgwirizano wa anthu ophunzira,koma anthu ophunzira bwino malamulo achipembedzo adasemphana zokhuza mapata ena a malamulo ngati QIYAS(komwe : ndikufananiza kwa lamulo pakati pa phata ndi nthambi yake poyang'ana kufanana kwa chomwe chachitika),ndipo gulu la anthu ambiri ophunzira adanena kuti limeneli ndi limodzi mwa mapata odalirika pa malamulo achipembedzo ngati zonse zoyenera kuti likhale lamulo zapezeka. Ma umboni a mapata a zimenezi ndi ochuluka komanso odziwika osalira kuwatchula.

MAPATA WODALIRIKA POTSINDIKA MALAMULO ACHIPEMBEDZO

PHATA LOYAMBA: BUKU LA MULUNGU.

Tsinde loyamba la malamulo achipembedzo ndi buku la Mulungu lolemekezeka, ndipo mbuye wathu olemekezeka wayankhula mmalo ochuluka zakufunika ndikukakamizidwa kotsatira buku limeneli ndikuligwiritsa kwambiri ndikumvera malamulo ake.

Mulungu wapamwambamwamba akuyankhula kuti: (Ndipo talibvumbulutsa buku ili la Quran lomwe ndi lodalitsika , choncho tsatirani ndikumvera malamulo ake komanso mudzimuopa Mulungu ndicholinga choti Mulungu akumvereni chisoni).

Mulungu wapamwambamwamba akuyankhulanso kuti:

(Ndithudi wakufikirani inu(ayuda ndi akhirisitu) mtumiki wathu amene akukufotokozerani zinthu zambiri zomwe munali mukuzibitsa ngati zina mwa mbiri za mtumiki ndi malamulo ena ngati kugededwa ukagwidwa ukuchita chigololo pomwe ndiwe wapa banja poopa kuyaluka- kuchokera mu mabuku a mulungu(chipangano chakale ndi chatsopano),koma mtumikiyo sakutchula zambiri mu zomwe mwakhala mukuzibitsa chifukwa chopanda phindu zomwe sakutchulazo,ndithudi wakufikirani inu Muhammad komanso buku la Quran lomwe mulungu akuwawongola nalo anthu omwe amagwira ntchito zomusangalasa mulunguyo ndikusiya zomwe zimamunyasa,komanso kuwatulutsa anthu omutsatira mulungu malamulo ake kuchokera ku m'dima opembedza mafano,kusamukhulupilira mulungu ndikukhala anthu omukhulupirila mulungu ndikumamupembedza iye yekha powaongolera ku chipembedzo cha chisilamu).

Mulungu wapamwambamwamba akuyankhulanso kuti:

(Ndithudi anthu amene amaikanira Quran pambuyo pobvulutsidwa kwa iwowo, adziwe kuti ndithudi limeneli ndi buku lomwe ndi lotetedzedwa mau komanso matanthauzo ake moti ziwanda komanso anthu sangathe kuonjezera kapena kupungula chilichonse mu bukuli, ndithudi buku limeneli ndi chibvumbulutso chochokera kwa mulungu amene ndiwa nzeru zakuya komanso otamandidwa ndi zolengedwa zonse).

Mulungu wapamwambamwamba akuyankhulanso kuti:

(Ndipo Quran iyi yavubvulutsidwa kwaine ndi cholinga choti ndikuchenjezeni inu ndi anthu onse omwe Quran yawafika za zilango za mulungu ngati mutanyoza malamu ake).

Mulungu wapamwambamwamba akuyankhulanso kuti:

(Buku ili la Quran muli uthenga ochokera kwa mulungu kupita kwa anthu omwe wabwera ndi mtumiki wake Muhammad ndicholinga choti anthuwo achenjezedwe zakuopsa konyoza malamulo a mulungu).

Mau a mulungu komanso zoyankhula za mtumiki wa mulungu-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-zomwe zikulamulira zogwiritsitsa kwambiri malamulo a m'buku la Quran omwe akukamba zoti munthu amene angagwiritsitse malamulo a mulungu akhala ali pa chiwongoko ndikuti amene angasiye osagwiritsitsa malamulowo akhala wasochela, ndipo zina mwa zoyankhula za mtumiki-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye- zolamulira kugwiritsitsa malamulo a Quran ndi sunna , ndi mau omwe adayankhula pa mapemphero a hajj momwe anasanzikana ndi asilamu anthawi imeneyo ndipo adati:

(Ndithu ine ndakusiyirani inu buku loti ngati mutaligwiritsitsa simungasochere).

Hadith idachokera kwa Muslim.

Hadith ina yomwe ikuchokeranso kwa Muslim kudzera kwa Zaid bin Arqam-mulungu asangalasidwe naye-adanena kuti mtumiki wa mulungu mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye adanena kuti:

"Ndithu ine ndakusiyirani zinthu ziwiri zikuluzikulu , choyamba mu ziwirizi ndi buku la mulungu momwe muli chiwongoko chokwanira komanso dangalira lomuunikira munthu njira ya umoyo opambana, choncho tengani ndikugwiritsa ntchito buku la mulungu poliloweza,kuwerenga komanso kuligwiritsitsa pogwiritsa ntchito malamulo ake".

Mtumiki wa mulungu adalimbikitsa zogwiritsitsa buku la mulungu ndikuwauza anthu zakufunika kogwiritsitsa bukuli ndipo kenako adayankhula kuti:

"Komanso ndikukulamulirani zowachitira zabwino aku banja kwanga, ndikukulamulirani zowachitira zabwino aku banja kwanga".

Pofuna kutambasula mau amu buku la Quran adanena kuti:

Quran ndi malamulo a mulungu , ndipo munthu amene angagwiritsitse malamulo a m'buku limeneli akhala ali pachiwongoko ndipo amene angasiye osagwiritsitsa malamulo ake abukuli akhala wasochera.

Ndipo ma hadith omwe akukamba zakufunika kogwiritsitsa buku la Quran alipo ambiri,komanso m'gwirizano wa anthu ophunzira bwino komanso okwanira bwino chikhulupiliro chawo kuyambira ophunzira a mtumiki ndi ena omwe anabwera pa mbuyo pawo iwowo pakukakamizidwa ndikufunika kugwiritsitsa buku la mulungu, ndizokwanira kukhalanso umboni popewa kutalikitsa potchula ma umboni ochuluka omwe akukamba zokhuza kugwiritsitsa buku la mulungu.

PHATA LACHIWIRI: ZOCHITA ZOTSIMIKIZIKA ZA MTUMIKI-MTENDERE NDI MADALITSO A MULUNGU ZIKHALE PA IYE-, NDI OPHUNZIRA AKE , NDI OMWE ANABWERA PA MBUYO PAWO MWA ANTHU ODALIRIKA PA MAPHUNZIRO NDI CHIKHULUPILIRO CHAWO.

Tsono phata lachiwiri mu mapata a malamulo atatu achipembedzo cha chisilamu omwe anthu ophunzira bwino adagwirizana za mapatawo, ndi zochita zotsimikizika za mtumiki-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa mtumikiyo-,ndi ophunzira ake mtumikiyo-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-,ndi anthu omwe adabwera pambuyo pa ophunzira amtumikiyo mwa anthu ophunzira komanso achikhulupiliro chokwanira ndi chodalirika, amene anali akhulupilira phata la mapatali ndikumaligwiritsa ntchito komanso kumawaphunzitsa anthu zakufunika kogwiritsa ntchito phatali. Anthu ophunzira bwino komanso ndi odalirika pa maphunziro awo achipembedzo adalemba mabuku ochuluka momwe adafotokoza momveka bwino za phata limeneli mu mabuku ngati a malamulo a fiqh(kumvesesa malamulo akachitidwe ka zinthu mu chipembedzo)komanso malamulo achipembedzo cha chisilamu,ndipo ma umboni ake alipo ochuluka osawerengeka. Ena mwa ma umboniwo ndi omwe akupezeka mu buku la mulungu lolemekezeka momwe muli malamulo omusatira mtumiki ndikumumvera, ndipo lamulo limenelo limapita kwa asilamu a nthawi yake komanso omwe adabwera pa mbuyo pawo chifukwa choti mtumikiyo anatumizidwa kwa anthu onse,ndikuti asilamu onse akukakamizidwa zomusata ndikumvera mtumiki mu zomwe akulamulira ndikuletsa kufikira tsiku lotsiriza,ndikutinso mtumikiyo-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye- ndi amene anapasidwa ntchito yotanthauzira ndikufotokoza matanthauzo a buku la mulungu, ndikufotokoza motambasula malamulo omwe sanatambasulidwe mu buku la mulungu pogwiritsa ntchito zoyankhula,zochita zake, ndi zomwe ophunzira ake adachita iye ali pompo ndikuzivomereza osazuzula. Kupanda sunna(zochita)za mtumiki wa mulungu sibwenzi asilamu akudziwa chiwerengero cha mapemphero omwe amapemphera,kapemberedwe kake ,komanso zofunikira kuchita nthawi yopemphera,komanso asilamu sakanadziwa ndondomeko zokhuza malamulo akusala kudya(mwezi wa ramadhan ndi kusala kosakakamizidwa), kupereka zakah(chaulere chapa chaka),Hajj,malamulo okhuza kumenya nkhondo mu njira ya mulungu(Jihad),malamulo okhuza kulamulira zabwino ndikuletsa zoipa, komanso asilamu sakanadziwa tsatanetsatane wa malamulo okhuza makhalidwe a anthu pakatipo pawo komanso sakanadziwa tsatanetsatane wa malamulo okhuzana zinthu zoletsedwa,komanso asilamu sakadadziwa za zilango zomwe mulungu adalamulira kuti munthu akachitamo azilandira zilangozo potengera ndi zomwe zikupezeka mu mavesi a m'buku la Quran. Ena mwa mavesi omwe akulamulira zotsatira zochita za mtumiki wa mulungu akupezeka mu suratu al-imran:

(Ndipo muzisatira malamulo a mulungu ndi amtumiki wake ndi cholinga choti mulungu akuchitireni chisoni).

Komanso mau a mulungu wapamwambamwamba ochokera mu suratu al-nisa:

(Ee! inu anthu okhulupilira tsatirani ndikumvera malamulo a mulungu ndi a mtumiki wake komanso muziwamvera atsogoleri anu pa zomwe akukulamulirani mu zinthu zosasemphana ndi malamulo amulungu ndi mtumiki ndipo ngati mutasemphana pa kena kalikonse bwelerani ku buku la mulungu komanso zochita za mtumiki kuti mukapeze lamulo la chomwe mwasiyana maganizocho ngati inu mumakhulupilira mwa mulungu komanso za tsiku lotsiriza,kubwelera ku buku la mulungu komanso zochita za mtumiki pa zinthu mwasiyana maganizo ndizomwe zili zabwino kamba koti zimathesa kusemphana maganizo ndipo mumakhaka okondana).

Mulungu wapamwambamwamba akuyankhulanso mu suratu al-nisa:

(Munthu amene angatsatire ndikumvera malamulo a mtumiki ndithudi munthu ameneyo amakhala kuti watsatira malamulo a mulungu,tsono kwa munthu amene anganyoze malamulo ako , dziwa kuti iwe sitinakutumize kukhala oyang 'ana ntchito zawo ndikuwawerengesera koma kuti tinakutumiza ngati mtumiki owaitanira ku zinthu zabwino ndikwaletsa zoipa).

Zingatheke bwanji mulungu kulamulira zomvera ndikutsatira malamulo ake a mtumiki komanso kubwelera ku buku la mulungu ndi zochita za mtumiki nthawi yomwe anthu asemphana maganizo ngati zochita (sunna) za mtumikizo siuli umboni okwanira kapena sunna(zochita)za mtumikiyo sizili zotetedwa?Ngati zitakhala choncho kuti zochita za mtumiki sizikukwanira kukhala umboni ndekuti zitanthauza kuti mulungu analamulira anthu kutsatira chinthu choti palibe , limenelo ndi bodza lalikulu komanso ndi kumukanira mulungu kwakukulu ndikumuganizira mulungu maganizo oipa.

Mulungu mwini ulemelero akuyankhula mu suratu al-nahl:

(Ndipo takupatsa iwe sunna ndi cholinga choti uwafotokozere anthu za malamulo omwe abvumbulitsidwa kwa anthuwo ndi cholinga choti adziwe zomwe zabwelera iwowo kuchokera kwa mulungu).

Mulungu akuyankhulanso mu suratu yomweyi kuti:

(Ndipo ife sitinakubvulutsire iwe buku la Quran koma kuti tinatumiza bukuli ndi cholinga choti wafotokozere anthu zinthu zomwe amakhala akusemphana mu malamulo a mu bukulo ndikuti wasogolere anthu ku zinthu zoona ndikukhala chisoni kwa anthu okhulupilira).

Zingatheke bwanji kuti mulungu mwini ulemelero onse amupatse mtumiki wake -mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-udindo ofotokoza motambasula malamulo a buku la Quran pogwiritsa ntchito zochita (sunna)zake kumachita kuti sunnayo palibe komanso mulibe umboni ulionse pa malamulo achipembedzo?

Mau ena a mulungu ofanana ndi omwe ali mmwambamu olamulira zotsatira malamulo a mtumiki wa mulungu akupezeka mu suratu al-nur:

(Nena iwe Muhammad powauza anthu okhulupilira kuti mverani ndikutsatira malamulo a mulungu ndi mtumiki wake,koma ngati mutanyozera malamulo a amulungu ndi mtumiki wake dziwani kuti mtumikiyo ali ndi zake zolakwika zomwe wasenzedwa inunso muli ndi zanu zolakwika zomwe mwasenzedwa, koma ngati mutamutsatira ndikumvera mtumiki wa mulungu ndekuti mukhala anthu owongoka, ndipo dziwani kuti ntchito ya mtumiki wa mulungu ndikungofalitsa uthenga wa mulungu basi).

Mulungu wamwambamwamba akuyankhula mu suratu yomweyi kuti:

(Ndipo muziimika mapemphero ndikumapereka chopereka chaulere ndikumamvera ndikumutsatirsa mtumiki wa mulungu kuti mulungu akuchitireni chisoni).

Mulungu akuyankhula mu suratu al-a'araf kuti:

(Nena iwe Muhammad powauza anthu kuti ndithudi ine ndi mtumiki wa mulungu amene ndatumizidwa kwainu nonse , mulungu wake amene wanditumiza ine ndi amene ufumu waku mwamba ndi pa dziko pano uli mmanja mwake, ndipo palibe mulungu opembedzedwa mwa choonadi koma mulungu mmodzi yekha amene amapereka moyo ndi imfa, choncho mu khulupilireni iye pamodzi ndi mtumiki wake yemwe sanali kudziwa kulemba komanso kuwerenga Quran isanabvulitsidwe kwa iye chifukwa choti palibe munthu anamuphunzitsa asanaphunzitsidwe ndi mulungu,mtumiki wake amene amakhulupilira mwa mulungu komanso mau ake(quran)choncho tsatirani ndikumvera malamulo ake mtumikiyo kuti mukhale anthu otsogoleredwa ku njira yowongoka).

Mu ndime zomwe zatchulidwa mmwambamu,muli umboni owonekera osonyeza kuti chiwongoko komanso chisoni cha mulungu zagona potsatira malamulo a mtumiki -mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-nanga zimenezo zingatheke bwanji kukhala choncho popanda kugwiritsa ntchito sunna(zochita)za mtumiki kapensa kuyankhula kuti palibe kalikonse kolondola mu zochita za mtumiki kapena kunena kuti zochita za mtumiki sizodaliridwa ngati malamulo achipembedzo.

Mulungu mwini ulemelero wapamwamba akuyankhula mu suratu al-nur:

(Anthu amene amasemphana ndi malamulo a mtumiki wa mulungu akuyenera kukhala ndi mantha kuti atha kukhala osochera kapena kuwapeza zilango zochokera kwa mulungu chifukwa chosemphana ndi malamulo a mtumiki wa mulungu).

Mulungu akuyankhula mu suratu al-hashir:

(Zina zilizonse zomwe mtumiki wa mulungu wakulamulirani kuti muzichite zichiteni ndipo zilizonse zomwe wakuletsani kuti musazichite zisiyeni).

Ndime zamu Quraan zimene zili ndi matanthauzo a zomwe zikunenedwazi ndi ambiri ndipo ndime zonsezo zikusonyeza kukakamizidwa komutsatira ndikumumvera mtumiki -mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-,komanso mavesiwo akulamulira zotsatira kalikonse komwe anabwera nako kuchokera kwa mulungu monga mmene maumboni otsonyeza kukakamizidwa kotsatira malamulo a buku la mulungu komanso kugwiritsitsa buku la Quran ndikumvera malamulo ake komanso kusiya zomwe zaletsedwa mu Quran mo anenera,mapata awiri amenewa amayenda limodzi samasiyana(Quran ndi sunna),ndipo amene angakanire chimodzi mwa mapata awiriwa ndekuti wakanira phata linalonso ndipo watsutsana nalo,kuchita choncho ndekuti munthu amasanduka okanira ,amasokera,komanso amatuluka chisilamu, izo motengera ndi mgwirizano omwe anthu ophnuzira bwino maphunziro achisilamu adagwirizana.

Mu maumboni ena omwe akukambanso zokakamizidwa kotsatira zochita za mtumiki ndi zoyankhula zochokera kwa mtumiki-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye.

Zoyankhula zoona za mtumiki -mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye - zokamba zokhuza kukakamizidwa kumutsatira ndikumvera mtumikiyo , ndikutsatira zonse zomwe adabwera nazo, komanso zoyankhula zoletsa kumunyoza ndikunyoza malamulo ake,malamulo amenewo akupita kwa asilamu onse omwe analipo nthawi yake koma asilamu omwe adzakhale akubwera pa mbuyo pa mtumikiyo kufikira tsiku lotsiriza, zina mwa zoyankhula za mtumikiyo ndi zomwe zatsindikizika mu mabuku awiri(Bukhar ndi Muslim)kuchokera mu zoyakhula za mtumiki zomwe akutiuza Abi Huraira-chisangalalo cha mulungu chikhale pa iye-yemwe adati : mtumiki wa mulungu- mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye adati:

"Munthu amene anganditsatire ine ndithu munthu ameneyo zoona zake ndi zoti wamutsatira mulungu,ndipo munthu amene angandinyoze ine potsatsatira malamulo anga ndekuti munthu ameneyo zoona zake zikhala wanyoza mulungu".

Mu zoyankhula zina za mtumiki-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye- zomwe zikuchokera mu buku la Bukhar-mulungu amuchitire chisoni -,mtumiki adati:

Anthu anga onse akalowa ku mtendere kupatula munthu amene angakane kukalowa ku mtendereko. Ndiye kunanenedwa mofunsa kuti: ee! inu mtumiki wa mulungu; ndi ndani amene angakane kukalowa ku mtendere? Mtumiki adati: munthu amene anganditsatire ndikundimvera ine ndi amene akalowe ku mtendere, ndipo munthu amene angandinyoze ine potsatsatira malamulo anga ndi amene wakana kukalowa ku mtendere".

Hadith ina ikuchokera kwa Ahmad,Abu Dawood,Al-Hakim ndi gulu la anthu odalirika omwe adaitenga hadithyo kuchokera kwa Miqdaad bin ma'ad karb ,yemwe adaitenga kuchokera kwa mtumiki -mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye -yemwe adati mtumiki wa mulungu adanena kuti:

"Dziwani kuti ndithu ine ndapatsidwa buku la Quran ndi sunna yomwe ikufanana ndi Quranyo kuti zonse ndi mau a mulungu, dziwaninso kuti nthawi ya wandikira yomwe padzapezeke munthu oti wakhuta nde wakhala pa mpando wake ndikumayankhula kuti; muzingogwiritsa ntchito malamulo mukuwapeza mu buku la Quran lokha, mukapeza kuti mu buku la Quran muli malamulo omwe akuloleza chinthu china chake nanunso chilolezeni chinthu chimenecho, ndipo mukapeza mu malamulo amu Quran akuletsa chinthu china chake nanunso chiletseni".

Hadith idachokera kwa Abu Dawood,Ibn Majah kudzera mwa gulu la anthu odalirika: hadith inadzera kwa mwana wa raafi'u yemwe adawamva a bambo ake ndipo a bambo akewo adamva kwa mtumiki- mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-, mtumiki wa mulungu adati:

"Ndisamupeze m'modzi mwa inu atakhala pa mpando kenako ndikumupeza nkhani ina iliyonse yochokera kwa ine kuchokera mu zomwe ndidalamulira kuti anthu azichita kapena mu zinthu zomwe ndidawaletsa anthu kuti asamachite, iye akafunsidwa za lamulo la chinthucho ndikumanena kuti: sitikudziwa lamulo lochokera mu zochita za mtumiki,koma ife tizitsatira zomwe tazipeza mu buku la mulungu osati za mtumiki".

Hadith ikuchokera kwa Hassan mwana wa Jabir yemwe adati: ndidamumva Miqdaad bin Ma'ad bin Karib-chisangalalo cha mulungu chipite kwa iye-akuyankhula kuti:

Tsiku la nkhondo ya Khaibar mtumiki wa mulungu - mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-adaletsa zinthu zambiri kenako nde adayankhula kuti: nthawi yatsala pang'ono kufika pomwe padzapezeke munthu onditsutsa ndikundikanira ine, adzakhala kuti wakhala pa mpando ndikumauzidwa za nkhani yokhuza ine , kenako azidzayankhula kuti: pakati pathu pali buku la mulungu (Quran),tsono malamulo omwe tawapeza mu buku la Quran omwe akuloledza zinthu, ifenso tiziziloledza zinthu zimenezo, ndipo zomwe tazipeza kuti mulungu wadziletsa mu bukulo, ifenso tiziziletsa, dziwani kuti ndithudi zomwe adaziletsa mtumiki sizikusiyana ndi zomwe analetsa mulungu chifukwa zonsezo ndi malamulo a mulungu.

Hadith idachokera kwa Al-Hakim,Tirmidhi ndi Ibn Majah kudzera mwa anthu odalirika.

Zoyankhula zoona za mtumiki -mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-zomwe zikukamba kuti mtumiki amawalangiza ophunzira ake kuzera mu ma ulaliki ake mtumikiyo kuti anthu omwe amaveserawo adzikafikitsa uthenga wakewo kwa anthu omwe panalibe ndipo amayankhula kuti: "Kuthenga munthu ouzidwa uthenga mkumvetsesa ndikuwusunga bwino ndikumagwiritsa ntchito kuposa munthu yemwe akupereka uthengawo".

Zina mwa zoyankhula za mtumiki zokhuza kukakamizidwa kogwiritsa ntchito zochita zake ndi zomwe zikupezeka mu mabuku awiri la Bukhar ndi Muslim, momwe muli zoti mtumiki wa mulungu-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-, pa tsiku lomwe adaima pa phiri la Arafa komanso tsiku lozinga zinyama(pa malo otchedwa mina) pomwe amapanga Hajj momwe adatsazikana ndi asilamu ,adapereka ulaliki kwa asilamu ndipo adanena kwa iwo kuti:

"Munthu amene wapezeka pano ndikumva uthenga ndanenawu,akamuze munthu amene sanapezeke pano chifukwa kutheka munthu yemwe uthenga wamufikira kuchokera mwa m'modzi mwainu omwe mwamva pano, ndikukhala omvesesa ndikusunga bwino ndikugwiritsa ntchito uthengawo kuposa amene wamva kuchokera kwa ine".

Zikanakhala kuti zochita za mtumiki si umboni okwanira kwa munthu amene wamva kapena zamufikira zochita za mtumikizo,zikanakhala kuti zochita za mtumiki sizokhazikika kufikira tsiku lotsiriza, mtumiki sakadawalamula ophunzira ake kuti afalitse zochita zake kwa anthu ena omwe pomwe mtumiki amayankhula panalibepo. Chifukwa cha lamulo limenelo lomwe mtumiki adalamulira ophunzira ake zofalitsa zochita zake,zadziwikano kuti zochita za mtumiki ndi umboni omwe uli opitilira kwa wina aliyense yemwe uthengawo wamufika-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-komanso ndi umboni okwanira kwa munthu amene uthengawo wafikitsidwa kwa iyeyo kudutsira mu gulu la anthu odalirika komanso njira zabwino.

Ndipo ophunzira a mtumiki-mtendere ndi madalitso a mulungu zipite kwa mtumikiyo-adateteza zochita za mtumiki-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-,kaya ndi zoyankhula,zochita zake ndipo adafalitsa kwa anthu omwe adabwera pambuyo pawo, nawonso omwe adabwera pambuyo pa ophunzira amtumiki adafalitsa zochita(sunna za mtumiki kwa omwe adabwera pambuyo pa iwowo. Chimodzimodzi anthu odalirika pa maphunziro awo achipembedzo,adali akufikitsa zochita za ntumiki kwa anthu omwe amabwera pambuyo pawo , ndipo adazisonkhanitsa mu mabuku awo omwe adalemba ndikufotokoza mosiyanitsa zolondola ndi zabodza,ndipo adaika malamulo odziwira zomwe zili zoona ndi zabodza mu zochita za mtumiki,ndipo anthu odalirika pa maphunziro okhuza zochita za mtumiki adali akutenga zoyankhula zochokera mabuku awiri (Bukhar ndi Muslim)komanso mabuku ena zinthu zokhuza zochita za mtumiki, ndipo adaziteteza mokwanira monga umo mulungu adatetezera buku lake kuchokera ku chibwana cha anthu achibwana, komanso kukanira kwa anthu omwe amakanira zoti kuli mulungu,komanso makhalidwe owonjezera kapena kuchotsa ndime za mu buku lake pofuna kutsindika za mau ake mulungu oti iye adzateteza buku lake:

(Ndithudi ife tavumbulutsa buku la Quran, ndipo ife tidzaitetedza Quranyo).

Palibe chikaiko kuti zochita(sunna) za mtumiki-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye- ndi uthenga ochokera kwa mulungu,omwe mulungu anauteteza monga mmene anatetezera buku lake, ndipo adawapatsa anthu ophunzira bwino kukhala opulumutsa zochita za mtumiki, omwe amatsutsa kuwonjezera kapena kupungula kulikonse komwe kungachitike mu buku la mulungu ndi anthu owononga, komanso amatsutsa za matanthauziridwe a buku la mulungu omwe amatanthauzira anthu osazindikira, komanso amakhala akuiteteza sunna(zochita) za mtumiki kwa anthu osazindikira,anthu a bodza, anthu omwe amakana zoti mulungu alipo, chifukwa choti mulungu adaipanga sunna kukhala yotanthauzira buku lake lolemekezeka la Quran , komanso kufotokoza malamulo omwe sanafotokozedwe motambasula, ndiponso sunna muli malamulo ena oti mu Quran mulibemo,chitsanzo; kufotokoza kwa malamulo okhuza kuyamwisa mwana, ndi malamulo ena okhuza kagawidwe ka chuma munthu akamwalira,komanso malamulo ofotokoza zoletsedwa kophatikiza powakwatira pakati pa mkazi ndi azakhali ake ambali ya bambo komanso mai,ndi malamulo ena osiyana siyana omwe adabwera mu zochita za mtumiki ndipo mu Quran sanatchulidwe malamulo amenewo. Mu zoyankhula zina zomwe zidachokera kwa ophunzira a mtumiki(maswahaba) komanso anthu omwe adabwera pa mbuyo pa ophunzira amtumikiwo(ma tabi'na) ndi anthu enanso ophunzira omwe adabwera pa mbuyo pawo,mu zoyankhula zokhuza kufunika kolemekeza zochita za mtumiki komanso kukakamizidwa kuzigwiritsa ntchito zochita za mtumikizo..

Mu mabuku a Bukhar ndi Muslim mukupezeka mau a mtumiki omwe akudzera kwa Abu Huraira-chisangalalo cha mulungu chikhale pa iye-adati:

Atamwalira mtumiki wa mulungu -mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-,ndipo pomwe ena mwa aluya adatuluka chisilamu Abubakar Siddiq-chisangalalo cha mulungu chikhale pa iye- adayankhula kuti: ndikulumbira mu dzina la mulungu ndimumenya nkhondo munthu wina aliyense amene angasiyanitse pakati pa lamulo la swala ndi zakat, Umar -chisangalalo cha mulungu chikhale pa iye-atamva mau amenewo adati:" zitheka bwanji kuwamenya nkhondo iwowo kumachita kuti mtumiki wa mulungu-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye- adanena kuti-:" "ndalamulidwa kuti ndiwamenye nkhondo anthu(ma quraish) kufikira atayankhula mau oti palibe mulungu opembedzedwa mwa choonadi koma mulungu m'modzi yekha, ndipo ngati atayankhula mau amenewo ndekuti awateteza magazi awo,,chuma chawo kuchokera kwaine koma kupatula ngati atachimwa uchimo omwe chilango chake ndikuphedwa kapena kutenda chuma chawo movomerekeza ndi malamulo achipembedzo". Kenako Abubakar Siddiq adayankhula kuti: Kodi kupereka Zakat si lamulo la mulungu loti ngati munthu akukana kupereka akuyenera kumenydwa nkhondo?. Ndikulumbira mu dzina la mulungu, ngakhale akanati iwowo andikanize ine kambuzi kakang ono komwe amapereka kwa mtumiki-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-, ndikanawamenya nkhondo chifukwa chondikaniza mbuzi imeneyo,Umar nde adati: pomwe Abubakar adayankhula mau amenewa ndinadziwa kuti mulungu watsekula chifuwa cha Abubakar kuti awamenye nkhondo anthu omwe amakana kupereka Zakat pambuyo pomwalira mtumiki ndipo ndinadziwa kuti zimenezo ndi zimene zinali zoona zake.

Ophunzira a mtumiki ena onse -chisangalalo cha mulungu chikhale pa iwo-adamutsatira Abubakar pa maganizo owamenya nkhondo anthu omwe amakana kupereka Zakat(Chaulere chapa chaka chifukwa choti iwowo akuti amapereka kwa mtumiki nde mtumiki wamwalira kusonyeza kuti lamulonso latha)ndipo anamenya nkhondo anthu anatuluka chisilamuwo mpaka ena adakwanitsa kwabweza ena ku chisilamu , ndipo kwa omwe adapitiriza kukana kupereka Zakat adawapha chifukwa chakutuluka kwawo mu chisilamu. Mu nkhani imeneyi muli umboni owonekera poyera kufunika koilemekeza sunna(zochita za mtumiki)komanso kukakamizidwa kozigwiritsa ntchito. Chitsanzo china ndi choti: Gogo wachizimai adabwera kwa Abubakar kudzafunsa zokhuza gawo lake mu chuma chamasiye ndiye Abubakar adayankhula kwa iye kuti:

"Palibe gawo lina lilonse lomwe mulungu wakupatsa mu chuma chamasiye, komanso sindikudziwa kuti mtumiki wa mulungu-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-adaperekapo kwa gogo ngati iwe china chilichonse mu chuma chamasiye", kenako Abubakar adawafunsa anthu(ophunzira ena a mtumiki wa mulungu ngati anali ndikuzindikira zokhuza gawo la gogo wamkazi pa chuma chamasiye): Kenako Abubakar -chisangalalo cha mulungu chikhale pa iye-adawafunsa ena mwa ophunzira a mtumiki -mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-ndipo adaikira umboni oti mtumiki wa mulungu-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye- adamupatsa gogo wa mkazi zinthu zisanu ndi chimodzi mu gawo la chuma cha masiye, ndiye Abubakar adamupatsa gogo amafunsa uja gawo limenelo. Chimodzimodzi Umar -chisangalalo cha mulungu chikhale pa iye- pa nthawi imene adali mtsogoleri wa asilamu,amawalangiza a ntchito ake(adindo ake amadera osiyanasiyana) kuti azikagwiritsa ntchito buku la mulungu poweruza pakati pa anthu omwe amawayang 'anira, ngati sanepeze lamulo la nkhani yomwe yapeza mu buku la mulungu, amawauza kuti akagwiritse ntchito zochita(sunna)za mtumiki-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye.

Mu nthawi ya ulamuliro wa Umar Bin Khatwabi-chisangalalo cha mulungu chikhale pa iye, idachitika nkhani yoti munthu wamumenya mzimai oyembekezera mpaka mzimai kudutsa padera,ndiye Umar samadziwa lamulo la nkhani ngati imeneyi, kenako Umar adamfunsa m'modzi mwa ophunzira amtumiki-mulungu asangalasidwe ndi ophunzira a mtumiki onsewo-zokhuza lamulo la nkhani imeneyo, ndiye Muhammad bin Musallama ndi Mughirat bin Shu'ubat -chisangalalo cha mulungu chikhale pa awiriwa- adaikira umboni kuti mtumiki wa mulungu-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-adagamula pa nkhani ngati imeneyo kuti munthu wapangitsa mzimai kupita pa dera amasule kapolo wammuna kapena wamkazi,naye Umar adagamula mofanana ndi mmene mtumiki wa mulungu adachitira.

Pomwe Uthman Bin Affan adakhalano msogoleri wa asilamu,padabwera nkhani yokhuza mzimai amene mamuna wake wamwalira ndiye amafuna kudziwa kutali kwa nthawi yomwe angalire maliro a mamuna wakeyo. Uthman zinamuvuta kudziwa lamulo lake ndiye kenako anamfunsa mzimai yemwe dzina lake ndi Fari'atu bintu Malik Bin Sinan mlongo wake wa Abu saidi -mulungu asangalale ndi awiriwa, yemwe adamuza Uthman kuti: mtumiki wa mulungu -mtendere ndi chisoni cha mulungu zikhale pa iye-adalamula iyeyo pambuyo pomwalira mamuna wake kuti alire maliro amuna wakeyo kufikira pomwe nthawi yake yolira maliro itatha. Nde uthman adagamula motengera ndi chigamulo cha mtumiki.

Chimodzimodzi Uthman bin Affan adagwiritsa ntchito zochita za mtumiki popereka chilango cha mowa kwa Walid mwana wa U'quba. Chimodzimodzinso, pomwe Ali-mulungu asangalatsidwe naye -pomwe adamva kuti Uthman Bin Affan-mulungu asangalatsidwe naye-akuletsa kuti anthu akavalamo Ihram(nsalu yoyera imavalidwa ku mapemphero a Hajj ndi Umrah)pofuna kupanga Hajj asamavulenso, ndiye Alie -mulungu asangalale naye adaika chitsimikizo(niya)ya mapemphero a Umrah komanso Hajj atavala nsalu ya Ihram ndkuivula atamariza kupanga Umrah asanapange Hajj, kenako adati: "Sindingasiye zochita za mtumiki wa mulungu -mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-chifukwa cha mau a munthu wina aliyense". Pomwe anthu ena adaikira umboni pamaso pa Abdul Allah mwana wa Abbas-chisangalalo cha mulungu chipite kwa awiriwa-, mau a Abubakar ndi Umar pa nkhani yokhuza kusiyanitsa zovala za Hajj ndi Umrah,Abdul Allah mwana wa Abbas-mulungu asangalatsidwe nawo awiriwa adati: "Nthawi yatsala pang'ono yomwe mwala udzakugwereni kuchoka kumwamba(ngati mtundu wa chilango) chifukwa choti ine ndikunena kuti: mtumiki wa mulungu-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-adati chakuti , inu nde mukumayankhula kuti:Abubakar ndi Umar adati chakuti". Ngati munthu amene wasemphana ndi zochita za mtumiki chifukwa chotsatira zoyankhula Abubakar ndi Umar akuopezeredwa chilango chochokera kwa mulungu, nanga kuli bwanji kwa munthu amene amasemphana ndi mtumiki chifukwa cha zoyankhula za anthu wamba kapena kamba kotsatira zomwe iwowo akumva mu zoyankhula za mulungu ndi mtumiki?. Anthu ena pomwe adasemphana ndi Abdul Allah mwana wa Umar-chisangalalo cha mulungu chikhale pa awiriwa pa nkhani yokhuza zina mu zochita za mtumiki,Abdul Allah adanena kuti: Kodi ife talamuridwa zomutsatira Umar kapena zochita za mtumiki?

Pa nthawi yomwe munthu wina adayankhula kwa Imran Bin Huswain-chisangalalo cha mulungu chikhale pa iyeyo ndi bambo ake:tatiuze zokhuza buku la mulungu, pomwe iye adali akuwauza zokhuza zochita za mtumiki,Imran Bin Huswain adapsa mtima kamba ka mau a munthuyo ndipo adati: Ndithudi zochita za mtumiki(sunna) ndi zomwe zimatanthauzira buku la mulungu, kupanda zochita za mtumiki ife sitikanadziwa kuti swala ya Zuhr imapempheredwa ma rakat anayi, swala ya maghrib ma rakat atatu, swala ya fajr (subh)ma rakat awiri, komanso kupanda zochita za mtumiki sitikanadziwa tsatanetsatane wa malamulo a Zakat(chopereka chaulere chapa chaka) ndi malamulo osiyanasiyana omwe adafotokozedwa bwino ndi zochita za mtumiki. Zoyankhula za ophunzira a mtumiki-chisangalalo cha mulungu chikhale pa iwo,zokhuza kulemekeza komanso kukakamizidwa kogwiritsa ntchito zochita za mtumiki, komanso kuwachenjeza anthu zakuipa kosemphana ndi zochita za mtumiki, ndi zochuluka kwambiri. Zina mwa zoyankhula za ophunzira a mtumiki, ndi zomwe adayankhula Abdul Allah mwana wa Umar-chisangalalo cha mulungu chikhale pa awiriwa- amene pa nthawi yomwe adatchula mau a mtumiki-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-oti: (Musamawaletse akapolo achikazi a mulungu kupita kukapemphelera ku mizikiti ya mulungu).

Ena mwa ophunzira ake adanena kuti: tikulumbira mu dzina la mulungu, ife tidziwaletsa akapolo achikazi a mulungu kupita ku mizikiti,ndiye Abdul Allah mwana wa Umar adapsa mtima ndipo adamukalipira adayankhula mau amenewo kenako adayankhula kuti: Ine ndikunena kuti mtumiki wa mulungu adanena zakuti zakuti inu nde mukuti tikulumbira mu dzina la mulungu tidziwaletsa iwowo. Chitsanzo china ndi zoyankhula za Abdul Allah mwana wa Maghfar wa mtundu wa Mazni-chisangalalo cha mulungu chikhale pa iye-amene adali m'modzi mwa ophunzira a mtumiki -mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-,iyeyu adamuona m'modzi mwa abale ake atatenga legeni ndikuika mwala ndikumagendana ndiye anamuletsa za mchitidwe umenewo, kenako anamuza za mau a mtumiki -mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-, oti mtumikiyo "adaletsa zogendana ndi timiyala pogwiritsa ntchito legeni chifukwa choti mwala wa mu legeni sungatsakire chinyama kapena kuphera m'dani wake koma umangoswa dzino kapena kuchotsa kapena kuvulaza diso". Kenako pambuyo pomuza mau a mtumikiwa adamuonanso akuchitanso zomwe anamuletsazo ndiye adayankhula kuti: ndikulumbira mu dzina la mulungu sindidzakuyankhulanso mpaka kale,ndikukuza kuti mtumiki wa mulungu adaletsa zogendana ndi miyara yomwe yaikidwa mu legeni ndiye ukukabwerezanso kuchita?.

Hadith ina ikuchokera kwa Baihaq yomwe adaitenga kwa Ayyubu Al-Sakhitiyani m'modzi mwa ophunzira akulu akulu a ophunzira a mtumiki, momwe iyeyu adanena kuti: "Ngati ukumuza munthu zokhuza zochita za mtumiki, munthu ouzidwayo ndikuyankhula kuti musatiuze zimenezo, koma muzitiuza zochokera mu buku la Quran lokha, udziwe kuti munthu ameneyo ndi osochera". Al-Auza'i -mulungu amuchitire chisoni adayankhula kuti: "Zochita(sunna) za mtumiki zimapereka chigamulo mu malamulo akupezeka mu buku la Quran poika malire pa zinthu zomwe Quran sinaike malire kapena kubweresa malamulo oti mu buku la Quran sanatchulidwe, monga m'mene zilili mu mau a mulungu awa:

(Ndipo takubvulutsira iwe sunna(zochita zako)ndi cholinga choti wafotokozere anthu pogwiritsa ntchito zochita zakozo, malamulo omwe atumizidwa kwa anthuwo kudzera mu buku la Quran, kuti mwina angakhale anthu oganiza mkumagwiritsa ntchito malamulo a mulungu ndi mtumiki wake).

Takamba kale zokhuza mau a mtumiki wa mulungu -mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye oti: "Dziwani kuti ndithudi ine ndapatsidwa buku la Quran limodzi ndi sunna zomwe malamulo ake ndi ofanana".

Mau ena adachokera kwa Baihaq amene nayenso adawamva kuchokera kwa A'amir Al-Sha'abi -mulungu amumvere chisoni-amene adayankhula kuwauza anthu ena kuti:

"Anthu inu mudzaonongeka pa nthawi yomwe mudzasiye kugwiritsa ndikutsatira zochita za mtumiki wa mulungu zomwe zili zotsimikizika kuti ndi zoona". Mau ena akuchokeranso kwa Baihaq omwe adawanva kuchokera kwa Al-Auza'i-mulungu amumvere chisoni-amene adawauza ena mwa ophunzira ake kuti: "Ngati zakupeza zoyankhula zochokera kwa mtumiki wa mulungu-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-,upewe kutenga ndikugwiritsa ntchito zoyankhula za munthu wina chifukwa choti mtumiki wa mulungu, adali mthenga wofalitsa uthenga wa mulungu wamwambamwamba".

Mau ena akuchokera kwa Baihaq amene adamva kuchokera kwa imaam wamkulu Sufyan mwana wa saidi al-thauri-mulungu aumvere chisoni- amene adanena kuti: "Maphunziro onse achipembedzo agona pophunzira maphunziro okhuza zochita(sunna) za mtumiki wa mulungu". Malik -mulungu amuchitire chison-adanena kuti: "Palibe wina aliyense mwa ife (anthu ophunzira ndi odalirika pa maphunziro awo) amene angayankhule mau, kupatula kuti mauwo amatha kukanidwa ndikubwezedwa kwa mwini wake oyankhula , kupatula zoyankhula za mwini manda awa, ndipo anali akulozera manda a mtumiki wa mulungu- mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-, ndi zokhazo zomwe sizimakanidwa ndikubwezedwa ndikusasatidwa".

Abu Hanifa -mulungu awamvere chisoni -adanena kuti: "Ngati pabwera mau a mtumiki wa mulungu-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-pa nkhani ina iliyonse, ine kwanga ndikumvera ndikutsatira zomwe zili mu mau amenewo".

Shafie-mulungu amuchitire chisoni- adanena kuti: "Ndikadzauzidwa za mau a mtumiki wa mulungu-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-omwe mauwo ndi owona, kenako ine nde osawatenga ndikuwatsatira, nthawi imeneyo mudzaikire umboni kuti mutu wanga sukugwira ntchito".

Shafie-mulungu amuchitire chisoni-adanenanso kuti: "Ngati nditayankhula mau , kenako ndikupezeka mau a mtumiki wa mulungu-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-,omwe akusiyana ndi zomwe ndayankhula ine, asiyeni mau angawo ndikutenga mau a mtumiki wa mulungu".

Imaam Ahmad Bin Hambal-mulungu amuchitire chisoni-adayankhula kuwauza ena mwa ophunzira ake kuti: "Musamanditsatire ine kapena Malik kapena Shafie, koma mudzitsatira zoyankhula zomwe ife tatenga kuchokera kwa mtumiki wa mulungu".

Imaam Ahmad Bin Hambal-mulungu amuchitire chisoni -adanenanso kuti: "Ndikudabwa ndi anthu oti ali ndikuzindikira kokhuzana njira zabwino zomwe anthu amatengera mau a mtumiki wa mulungu-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-kuzera mwa anthu odalirika, kenako ndikumapita kwa Sufiyan kumakatenga zoyankhula zake kusiya za mtumiki , kumachita kuti mulungu mwini ulemelero akuyankhula kuti: "Anthu amene amasemphana ndi malamulo a mtumiki wa mulungu akuyenera kukhala ndi mantha,kuti atha kusochera kapena kuwapeza zilango zowawa kuchokera kwa mulungu".

Kenako imaam Ahmad Bin Hambal adanena momufunsa m'modzi mwa ophunzira ake kuti: kodi ukudziwa tanthauzo la mau oti Fitna? Fitna akutanthauza kumuphatikiza mulungu ndi zinthu zina, zomwe zikutanthauza kuti: munthu kukanira zina mu zoyankhula za mtumiki-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-,mu mtima mwake mumayamba kupezeka maganizo osokera kenako munthu umaonongeka.

Mau ena akuchokera kwa Baihaq omwe iyeyo anawamva kuchokera kwa Mujahid mwana wa Jabar m'modzi mwa ophunzira akulu akulu a ophunzira a mtumiki wa mulungu, amene adanena mau poikira ndemanga mau a mulungu olemekezeka onena kuti:

(Ngati mwasemphana maganizo pa chinthu china chilichonse, bwelerani kwa mulungu(ku buku la mulungu)ndikwa mtumiki (zochita za mtumiki) kuti mukapeze chigamulo pa chinthu chomwe mwasemphanacho).

Iye adanena kuti: kubwelera kwa kwa mulungu kukutanthauza kubwelera ku buku la mulungu , ndipo kubwelera kwa mtumiki zikutanthauza kubwelera ku zochita za mtumiki wa mulungu. Mau ena akuchokera kwa Baihaq omwe iyeyo anawamva kuchokera kwa Al-Zuhuri- mulungu amuchitire chisoni- amene adanena kuti: "Anthu omwe adamwalira mwa omwe adali odalirika pa maphunziro awo, amakhala akuyankhula kuti kugwiritsitsa zochita za mtumiki ndi chomwe chimabweretsa chipulumutso". Muwaffiqu Deen Ibn Qudama- mulungu amuchitire chisoni-adanena mu buku lake "Raudhwatu Al Nadhwir": potambasula zokhuza mapata a malamulo mu chipembedzo cha chisilamu ndipo adati: Phata lachiwiri ndi umboni umodzi mu maumboni a zochita za mtumiki wa mulungu-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-,komanso zoyankhula za mtumiki wa mulungu-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-,ndi umboninso chifukwa choonekera kwa zozizwitsa zomwe zimaikira umboni zoti ndithudi iyeyo ndi mtumiki wa mulungu amene anabwera ndi uthenga owona, komanso mulungu adalamulira zomutsatira pa zomwe amalamula , ndi chenjezo lake lomwe mulungu adapereka zakuopsa kosemphana ndi malamulo ake mtumikiyo.

Cholinga chatha.

Ibn Kathir-mulungu amuchitire chison-adanena moikira ndemanga potanthauzira mau a mulungu awa:

"Anthu amene amasemphana ndi malamulo a mtumiki wa mulungu akuyenera kukhala ndi mantha,kuti atha kusochera kapena kuwapeza zilango zowawa kuchokera kwa mulungu".

Kutanthauza: kusemphana ndi lamulo la mtumiki wa mulungu-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-;kusemphana ndi njira yake, zochita zake, malamulo ake, zoyankhula, ntchito zonse mulingo oyezera wake ndi zoyankhula za mtumiki komanso zintchito zake, mu zoyankhula komanso zochita zomwe zafanana ndi mtumiki wa mulungu,zimalandiridwa kwa mulungu,ndipo zoyankhula ndi zochita zomwe zasemphana ndi mtumiki zimenezo zimabwezedwa kwa mwini oyankhulayo ndi ogwira ntchitoyo popanda kuyang'ana kuti wachita kapena kuyankhulayo ndi ndani.

Mau a mtumiki wa mulungu-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye- omwe ndi otsimikizika akupezeka mu mabuku awiri a Bukhar ndi Muslim,momwe mtumiki wa mulungu adanena kuti:

"Munthu amene angagwire ntchito ina iliyonse yomwe mu malamulo athu achisilamu mulibe lamulo lolamulira ntchito imeneyo,ntchito imeneyo idzabwezedwa kwa mwini wake anagwirayo ndipo sadzaripidwa pa tsiku lotsiriza".

Kutanthauza kuti: munthu amene amasemphana ndi malamulo a mtumiki owonekera kapena obisika akuyenera kukhala ndi mantha pa zotsatira zoipa zomwe zingamupeze kamba kosemphana ndi malamulo a mtumiki.

(Powopezera kukhala anthu osokera).

kutanthauza: kuwopezera kukhala anthu osokera mmitima mwawo pokanira zomwe mulungu adalamulira, kapena kukhala munthu obisa kukanira kwake ndikumaonesera chikhulupiliro kapena kukhala munthu opeka zinthu mu chipembedzo cha chisilamu.

(Kapena powopezera kuwapeza zilango za mulungu).

Kuwapeza zilango za mulungu pa dziko pompano pophedwa kapena kupasidwa chilango kapena kutsekerezedwa ndi zilango zosiyana siyana. Imaam Ahmad akuti Abdul Razaq adatiuza naye Abdul Razaq akuti adauzidwa ndi Ma'amar naye Ma'amar akuti adamumva Himmam mwana wa Munabih amene adati: izi ndi zomwe adatiuza Abu Huraira , amene adanena kuti: Mtumiki wa mulungu -mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-adati-:

"Fanizo langa pa inuyo zili ngati munthu amene wayatsa moto omwe wawalitsa malo onse ozungulira motowo, ndiye tizilombo ting 'ono ting'ono tikumauluka ndikumagwera pa motopo, munthu wayatsa moto uja ndiye akumakhala akutiteteza tizilomboto kuti tisagwere pa motopo, koma tizilombo tija tikumamugonjetsa munthu uja nde tikumagwera pa motopo,limenelo ndi fanizo laine pa inu ,ine ndikumakutetezani kuti musakalowe ku moto tsiku la chiweruzo pokuzani kuti muzitsatira zochita zanga, koma inu mukumandigonjetsa ine posamatsatira malamulo anga ndikumagwira ntchito yosemphana ndi malamulo anga zomwe zikakuchitiseni kukalowa ku moto tsiku lotsiriza"

Hadith imeneyi idachokera kwa Bukhar ndi Muslim kuchokera mu hadith yochokera kwa Abdul Razaq.

Al-Suyutwi-mulungu amuchitire chisoni-mu buku lake lotchedwa: "Miftahu al-janna fil-ihtijaj bi-sunna" muli mau oti:

"Dziwani inu asilamu-mulungu akuchitireni chisoni-kuti; munthu amene angakanire zoti zochita komanso zoyankhula za mtumiki wa mulungu-mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa iye-,kumachita kuti malamulo onse opangisa zoyankhula za mtumiki kuti zikhale zoona ndi zovomerezeka kwa anthu alipo zomwe zingapangitse zochita za mtumiki kukhala umboni, munthu ameneyo amakhala wakanira za mulungu komanso watuluka chipembedzo cha chisilamu, ndipo tsiku la chiweruzo akasonkhanitsidwa malo amodzi ndi ayuda ndi akhirisitu , kapena ndi anthu omwe mulungu akafune kuti akamusonkhanitse nawo limodzi mu magulu a anthu okanira.

Cholinga chatha.

Zoyankhula za ophunzira a mtumiki wa mulungu komanso anthu omwe adabwera pa mbuyo pawo ndi enanso anabwera pambuyo pa ophunzira a ophunzira a mtumiki mwa anthu odalirika pa maphunziro awo achipembedzo , zomwe zikukamba zokhuza kufunika kolemekeza zochita za mtumiki ndikukakamizidwa kugwiritsa ntchito zochita zake ,komanso kuchenjeza zakuipa kosemphana ndi zochita zake ,zilipo zochuluka zedi. Ndili ndi chikhulupiliro kuti zomwe tatchula mu bukuli kuyambira ndime za mu buku la mulungu, zochita ndi zoyankhula za mtumiki wa mulungu komanso zoyankhula za ophunzira a mtumiki ndi ena omwe adabwera pa mbuyo pawo mwa anthu odalirika pa maphunziro awo,ndizokwanira komanso zoti munthu ofunafuna choona angakhutitsidwe nazo. Tikumupempha mulungu komanso kuwapemphera asilamu kuti mulungu awafewesere kuti tizigwira ntchito zomusangalatsa mulunguyo,ndikuti atitalikitse ku zonse zomwe zingabweretse mkwiyo wake, ndikuti tonse atiwongolere ku njira yowongoka yachisilamu chifukwa choti mulunguyo ndi okumva kupempha komanso ali pafupi kwambiri ndi zolengedwa zake.

Mtendere ndi madalitso a mulungu zikhale pa kapolo komanso mtumiki wake, mtumiki wathu Muhammad pamodzi ndi aku banja kwake, ophunzira ake ndi onse omwe amumusatira mu zinthu zabwino zomwe adalamulira.

Abdul Aziz Bin Abdul Allah Bin Baz-mulungu awachitire chisoni.