Skip to content
Zina mwa zizindikiro za umodzi wa Mulungu(Tauhid).

Zina mwa zizindikiro za umodzi wa Mulungu(Tauhid).

M’dzina la Mulungu, Wachifundo Chambiri, Wachisoni. Kuyamikidwa konse ndi kwa Mulungu, Mbuye wa zolengedwa zonse, ndipo mathero abwino akakhala kwa anthu owopa Mulungu, ndipo ine ndikuikira umboni kuti palibe Mulungu opembedzedwa mwachoonadi koma Mulungu m'modzi yekha, opanda othandizana naye,ndipo ndikuikiranso umboni kuti Muhammad ndi kapolo ndi Mtumiki wake,mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa iye, aku banja kwake ndi ophunzira ake onse, pambuyo pa mau amenewa: Kukhulupilira za umodzi wa Mulungu ndi chiyambi ndi mathero a chipembedzo, ntchito zobisika ndi zoonekera zonse zagona…

Language: lang_ny
Prepared by: Abdul Razzaq bin Abdul Mohsen Al-Badr
Version: 1.0

Zina mwa zizindikiro za umodzi wa Mulungu(Tauhid).

Abdul Razzaq bin Abdul Mohsen Al-Badr

M’dzina la Mulungu, Wachifundo Chambiri, Wachisoni.

Kuyamikidwa konse ndi kwa Mulungu, Mbuye wa zolengedwa zonse, ndipo mathero abwino akakhala kwa anthu owopa Mulungu, ndipo ine ndikuikira umboni kuti palibe Mulungu opembedzedwa mwachoonadi koma Mulungu m'modzi yekha, opanda othandizana naye,ndipo ndikuikiranso umboni kuti Muhammad ndi kapolo ndi Mtumiki wake,mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa iye, aku banja kwake ndi ophunzira ake onse, pambuyo pa mau amenewa:

Kukhulupilira za umodzi wa Mulungu ndi chiyambi ndi mathero a chipembedzo, ntchito zobisika ndi zoonekera zonse zagona pokhulupilira za umodzi wa Mulungu, umenewo ndi uthenga oyamba ndi otsiriza wa Atumiki a Mulungu,kukhulupilira za umodzi wa Mulungu ndi tanthaunzo la mawu oti:"palibe Mulungu oyenera kupembedzedwa mwachoonadi koma Mulungu mmodzi yekha, pa chifukwa cha umodzi wa Mulungu,zidalengedwa zolengedwa,ndikutumizidwa Atumiki,komanso kuvumbulusidwa mabuku,kudzera mu umodzi wa Mulungu anthu adagawikana ena kukhala okhulupilira ndipo ena kukhala okanira,ena akakhala osangalala pokalowa ku moyo osatha ndipo ena akakhala atsoka pokalowa ku moto, chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndi ntchito yoyambilira yomwe ili yokakamizidwa kwa munthu amene watha nsinkhu, chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndi ndi chomwe chamanga chipembedzo cha Chisilamu chomwe Mulungu sakalandira tsiku la chiweruzo kuchokera kwa wina aliyense posakhala chimenechi,chikhulupiliro chimenechi ndi chofunikira kwambiri ndipo wina aliyense mwa ife amasowekera kukumbusidwa ndikuphunzitsidwa za chikhulupiliro chimenechi. Mu uthenga umenewu(zizindikiro za umodzi wa Mulungu),mwafotokozedwa zina mwa zizindikiro zake kuzera mu zinthu zikubwerazi:

Nkhani yoyamba: Zizindikiro za umodzi wa Mulungu ndi ubwino wake.

Nkhani yachiwiri: Tanthauzo ndi choona cha umodzi wa Mulungu.

Nkhani yachitatu: kukwaniritsa za chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu.

Nkhani yachinayi: Zoononga ndi Zopungula chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu.

Nkhani yachisanu:Komwe kumatengedwa chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu.

Nkhani yachisanu ndi chimodzi: Zipatso ndi Phindo la chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu.

Izi ndi nkhani zisanu ndi imodzi zomwe uthenga uwu uzungulila mwachidule,nkhani iliyonse mwa nkhanizi ikufuna kuilongosola momveka bwino, koma ine ndifotokoza mwachidule zomwe zidzakwaniritse cholinga Mulungu akafuna- wapamwambamwamba-ndipo kwa iye yekha ndi kumene kumapemphedwa thandizo ,ndipo kupempha kufeweseredwa zinthu.

Nkhani yoyamba:

Zizindikiro za chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndi ma ubwino ake.

Dziwa kuti chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu chili ndi zizindikiro zochuluka komanso ma ubwino ambiri zomwe zimasonyeza kukhala kwake pa mwamba, komanso upamwamba wake, apapa apa ndilangiza zinthu khumi,zina mwa izo ndi izi:

Chinthu Choyamba: chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu, ndi cholinga chimene tidalengedwela ndi kutipezekesa pa dziko la pansi pofuna kukwaniritsa cholinga chimenechi; monga momwe mau a Mulungu mwini ulemelero wapamwambamwamba akutisonyezera: {Sin.idalenge Ziwanda ndi Anthu koma kuti azindipembedza}. [Surah Al-Dhariyat:56]. Tanthauzo la mau oti(kupatula kuti adzindipembedza ine): Tanthauzo lake ndi loti: kuti adzikhulupilira za umodzi wanga pa kena kalikonse. Chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndi cholinga chomwe tidalengedwera moyo uno wa dziko la pansi, Mulungu sadangotilenga mwa macheza komanso sanangotisiya osatipasa malamulo, koma adalenga zolengedwa ndi cholinga choti zizimupembedza iye yekha, ndipo adazipezekesa zolengedwa pa dziko la pansi-Mulungu wapamwambamwamba-kuti azimupembedza iye yekha, ndipo uwu wakwanila kukhala umboni osonyeza kulemekezeka kwa chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndi upamwamba wa chikhulupiliro chimenechi.

Chinthu cha chiwiri: ndi choti chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndi tsinde la uthenga wa Aneneri ndi Atumiki onse,kutanthauza kuti: Mneneri wina aliyense amene adatumizidwa ndi Mulungu mwini ulemelero-uthenga wawo umagona pa nkhani ya chikhulupiliro cha umodzi wa mulungu, ndipo ma umboni wa mau amenewa alipo ambiri,ena mwa iwo ndi: mau a Mulungu mwini ulemelero ndikukwezedwa: {Ndithudi ife tidatumiza Mtumiki ku mtundu ulionse wa anthu kuti awauze anthu kuti adzipembedza mulungu mmodzi yekha ndikupewa kupembedza Satana(mafano)}. [Al-Nahl:36]. Ndi mau a Mulungu mwini ukulu onse: {Ndipo sitidatumize Mtumiki wina aliyense iwe usadabwera koma kupatula kuti timamupatsa uthenga onena kuti palibe Mulungu oyenera kupembedzedwa mwa choonadi koma ine(Mulungu), choncho mudzindipembedza ine ndekha}. [Surah Al-Anbiya:25]. Mulungu akuyankhula kuti: {Ndipo afunse Aneneri athu amene tidawatumiza iwe usadadze kuti:"kodi tidapanga milungu ina kuti ipembedzedwe kusiya Mulungu wachifundo chambiri?}. [Surah Az-Zukhruf:45]. Mulungu akuyankhula kuti: (Atchulire-iwe Mtumiki-anthu omuphatikiza Mulunguwo za nkhani ya m bale wawo obadwana osati wa chipembedzo wa mtundu wa Adi,pa nthawi yomwe adawachenjeza anthu ake za chilango cha Mulungu chomwe chingawapeze iwo ali mnyumba zawo zopangidwa ndi mchenga,Atumiki ena adabwera iye asadabwere komanso pambuyo pobwera iyeyo ndi uthenga owauza anthu kuti asapembedze Mulungu wina koma mmodzi yekha). [Al-Ahqaf:21]. Achenjezi: Atumiki; kutanthauza kuti: Atumiki omwe adabwera iye asadabwere komanso pambuyo pobwera kwake,onse adagwirizana pokhwaniritsa cholinga chimenechi. (Musampembedze Mulungu wina koma Mulungu mmodzi yekha), Choncho,chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndi pomwe padagona uthenga omwe Aneneri ndi Atumiki onse amaitanira anthu awo kuti akhulupilire; pa chifukwa chimenecho, mau oyambilira amene anthu amawanva kuchokera kwa Aneneri awo, ndipo chinthu choyamba chimene iwo amayamba nacho pa nkhani yoitanira anthu kwa Mulungu: chinali kuwaitanira kuti akhulupilire umodzi wa Mulunguyo; chifukwa ndi tsinde lomwe malamulo achipembedzo amayambira; Chipembedzo chimafanana ndi mtengo, ndipo ndi zodziwika kuti mtengo umakhala ndi phata komanso nthambi,ndipo mtengo sungalongosoke koma kudzera mukupezeka kwa phata lake, ndipo chipembedzo sizichingalongosoke popanda phata lake lomwe ndi umodzi wa Mulungu(Tauhid). (Kodi sukudziwa-iwe Mtumiki-momwe Mulungu wafanizilira liwu la umodzi wake"palibe Mulungu oyenera kumupembedza mwa choonadi koma iwe yekha" polifanizira ndi mtengo waukulu, omwe ndi mtengo wa zipatso za Tende,mitsitsi yake yalowa pansi , ndipo nthambi zake zili m'mwamba mbali ya mtambo? [Surah Ibrahim:24]. Monga momwe zimakhalira kuti mitsitsi ya mtengo ikadulidwa,mtengowo umafa,chimodzimodzi chipembedzo ngati chitakhala kuti sichinakhazikisidwe ndi umodzi wa Mulungu,palibe phindu lililonse lingabwere pa chipembedzo chimenecho. choncho, chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu pa chipembedzo cha Chisilamu, zili ngati mitsitsi ya mitengo komanso tsinde(faundeshoni)la zomangamanga.

Zomwe zikusonyeza kuti chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndilo phata la uthenga wa Aneneri ndi Atumwi onse ndipo uthenga wawo onse unagona powaitanira anthu ku chikhulupiliro chimenechi. Zinatsimikizika kuti Mtumiki -mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa iyeyo adayankhula kuti: “Aneneri ndi abale ochokera kwa bambo mmodzi,ndipo azimayi awo ndi osiyana, chipembedzo chawo ndi chimodzi.”([1]) Chikhulupiliro chawo ndi chimodzi, onse ndi oitanira ku umodzi wa Mulungu, ndipo azimayi awo ndi osiyana, kutanthauza kuti malamulo awo ndi osiyana. (Choncho, m'bado ulionse mwainu tidaupangira malamulo ake ndi njira yake yochitira malamulowo). [Al-Maidah:48]. Nkhani ikupezeka mu buku la Muslim(2365),mu nkhani yomwe ikuchokera kwa Abu Huraira-Mulungu asangalasidwe naye.

Mfundo yachitatu: china mwa zizindikiro za chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndi choti cimenecho ndi chinthu choyambilira chomwe munthu wakakamizidwa kugwira ntchito akuyenera kuchita; chinthu choyamba chimene ndi chokakamizidwa kwa munthu kuti alowe nacho mu chipembedzo ichi ndicho chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu,ndipo ndi chinthu choyamba chimene munthu akuyenera kuyamba nacho powaitanira anthu ku chipembedzo cha Mulungu, ndi chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu, ndipo izi zikusonyezedwa ndi ma umboni ambiri; ena mwa ma umboniwo ndi : kuyankhula kwa Mtumiki-mtendere ndi madalitso zikhale pa iye: “Ndalamulidwa zowathira nkhondo anthu opembedza mafano ochokera mu mtundu wa Aluya kufikira mpakana ndi anthu ataikira umboni kuti palibe Mulungu oyenera kupembedzedwa mwa choonadi koma Mulungu m'modzi yekha". Nkhani([2]): Wina mwa ma umboni ndi mau ake Mtumiki-mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa iye-pomwe amamuza Muadhi mwana wa Jabal- Mulungu asangalale naye-pa nthawi imene amamutumiza Muadhiyo ku Yemen: “Ndithu iwe ukupita kwa anthu eni mabuku, choncho chinthu choyamba chimene mukawaitanire chikhale kupembedza Mulungu Wamphamvuzonse.” Nkhani ([3]); Ndipo mu kuyankhula kwina: “Ndithu Iwe ukupita kwa anthu amene adatumiziridwa mabuku, choncho chinthu choyamba chimene ukawaitanire kuti achite chikakhale kukhulupirira umodzi wa Mulungu Wapamwamba” ([4]). Ndipo mu kuyankhula kwina; “Ndithu iwe ukupita kwa anthu amene adatumiziridwa mabuku, ndipo ukakafika kwa anthu amenewo, ukawaitanire kuti achitire umboni kuti palibe opembedzedwa mwa choonadi koma Mulungu mmodzi yekha, ndikuti Muhammad ndi Mtumiki wa Mulungu”( [5]), Kukhulupilira Mulungu m'modzi ndi chinthu choyamba chomwe chili chokakamizidwa kwa anthu otha nsinkhu omwe amayenera kutsatira malamulo a Mulungu, ndipo ndi zomwe zimayambidwa munthu kuti akhale Msilamu,ndi chinthu choyamba chimene munthu amalowa nacho m’chipembedzochi, chipembedzo chagona pa kukhulupiliro cha umodzi wa Mulungu, chomwe ndi tsinde lake lomwe malamulo onse amabwera pa mwamba pake. ( ) Nkhani adailemba ndi Bukhar(25, 1399),ndi Muslim (21, 22) mu nkhani yomwe inadzera kwa Abu Huraira, Ibn Umar ndi ena mwa ophunzira a Mtumiki- Mulungu asangalale nawo onsewo. Nkhani ikupezeka mu la Bukhar(1458) ndi Muslim(19). ()Nkhani ikupezeka mu buku la Bukhar(7372). ()NKhani ikupezeka mu buku la Bukhar(1496).

Mfundo yachinayi: china mwa zizindikiro za chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndi choti ndi chinthu chomwe chimabweresa kudekha ndi chiongoko kwa munthu pa dziko la pansi lino komanso tsiku lotsiriza pokalowa ku minda ya mtendere, werenga zimenezi mu mau a Mulungu mwini ulemelero komanso wapamwamba: (Anthu amene adakhulupilira Mulungu ndi Mtumiki wake, ndikumagwiritsa ntchito malamulo ake,ndipo sanasakanize chikhulupiliro chawo ndi khalidwe lomuphatikiza Mulungu ndi zinthu zina,anthu amenewo Mulungu amawapasa kudekha komanso mtendere,ndipo ndi anthu amene amapepusiridwa potsatira njira yowona). [Surah Al-An'am:82]. Kudekha kumakhala mmanja mwa Mulungu, ndipo Mulungu sapereka kudekha posakhala kwa munthu amene amamupembedza iye yekha mwini ulemelero. Pa nthawi yomwe chaputala ichi chidatsika-potengera ndi mmene zikunenedwera mu zoyankhula za Mtumiki-zidawavuta ophunzira a Mtumiki kuti amvesese zomwe Mulungu akutanthauza mu mau akewa, ndiye adapita kwa Mtumiki-mtendere ndi madalitso zikhale pa iyeyo ndipo adayankhula kuti:" e inu Mtumiki wa Mulungu! ndi ndani mwa ife amene samadzipondereza yekha?palibe munthu wina aliyense mwa ife koma kupatula kuti amachita machimo, Mulungu ndiye akuyankhula kuti: (Anthu amene adakhulupilira Mulungu ndi Mtumiki wake, ndikumagwiritsa ntchito malamulo ake,ndipo sanasakanize chikhulupiliro chawo ndi khalidwe lomuphatikiza Mulungu ndi zinthu zina,anthu amenewo Mulungu amawapasa kudekha komanso mtendere,ndipo ndi anthu amene amapepusiridwa potsatira njira yowona) Ophunzira a Mtumiki adanena za tanthauzo la mau a Mulungu kuti: ife tilibe gawo la kudekha komanso chiongoko; chifukwa wina aliyense mwa ife amazichitira zoipa iye mwini pochita machimo. Kenako Mtumiki-mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa iye-adayankhula kuti: " amenewo si matanthauzo ake ayi-amenewa si matanthauzo a mau akupondereza mu chaputala chimenechi-; kodi simunawerenge mau a kapolo olungama-amatanthauza Luqman amene adali wa luntha mu zochita zake zonse-: (Ndithudi kumuphatikiza Mulungu, ndi mchimo lalikulu kwambiri). [Surah Luqman:13]. Mtumiki-mtendere ndi madalitso zikhale pa iye- adatanthauzira Mulungu amdalitse ndi kumupatsa mtendere - kupondereza mu ndime imeneyi kuti ndikumuphatikiza Mulungu; choncho ndime imeneyi mmene ilili ikusonyeza kuti munthu amene wakhulupilira ndipo sakumusakaniza Mulungu ndi zinthu zina;iye amakhala ndi kudekha komanso chiongoko pa dziko la pansi pano komanso umoyo ukubwera,ichi ndi chimodzi mu zizindikiro za chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu choti: munthu amene angakhale okhulupilira mwa Mulungu mmodzi, Mulungu amamupasa kudekha komanso chiongoko pa dziko la pansi pano komanso moyo omwe ukubwera.

Mfundo yachisanu: china mwa zizindikiro za chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndi kukhala ndi mtendere posakhala munthu osausika komanso kutsutsana kwa chiphunzitso cha chikhulupiliro chimenechi, zomwe zikusemphana ndi zikhulupiliro zina, zomwe zili zosausa mmaganizo komanso zotsutsana mu ziphunzitso zake, umboni wa mau amenewa ndi mau ake a Mulungo mwini ulemelero wapamwamba: (Likanakhala kuti buku la Quran lidachokera kwa wina osati Mulungu,anthu akadapeza kusiyana kwakukulu mu mau ake a bukuli). [Surah Al-Nisa:82]. Zikhulupiliro zomwe anthu amazipeka ndikuyambisa,mumapezeka mau owasausa anthu ndikutsutsana kwakuluku, pomwe chikhulupiliro chowona ndi chabwino, ndi chikhulupiliro cholimba cha umodzi wa Mulungu, chomwe chimachokera mu buku la Mulungu ndi zochita za Mtumiki-mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa iye- ndi zabwino zilibe zosausa kapena zotsutsana.

Cha chisanu ndi chimodzi: Chimodzi mwa zizindikiro za chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndi choti chikhulupiliro chimenechi chimagwirizana ndi chilengedwe cha munthu chabwino ndi nzeru za munthu zowongoka; choncho, chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndi chipembedzo cha chilengedwe, ndipo ngati munthu atasiyidwa ndi mmene analengedwera, sakanavomera chikhulupiliro china chosakhala cha umodzi wa Mulungu; chifukwa ndi chikhulupiliro chogwirizana ndi chilengedwe cha munthu,kunena motsindika chikhulupiliro chimenechi ndi chomwe anthu adalengedwera nacho monga momwe Mulungu akuyankhulira: (Lunjika-iwe Mtumiki- iwe pamodzi ndi anthu omwe akukusatira iwe kuchipembedzo chimene Mulungu wakusonyeza,ndikusiya posatembenukira zipembedzo zina zonse,iwe ulunjike ku chipembedzo cha Chisilamu chomwe Mulungu adawalamulira anthu kuti achitsatire ndi kukhala chogwirizana ndi chilengedwe chawo, palibe kusintha chilengedwe cha Mulungu, chimenechi ndi chipembedzo cha Chisilamu chomwe mulibe kupotoka mkati mwa njira yake,koma anthu ambiri samadziwa kuti chipembedzo chimenechi ndi choona kusiya zipembedzo zina zonse). [Surah Ar-Rum:30] Tsono mchitidwe omuphatikiza Mulungu ndi zinthu zina, kupembedza milungu yambiri; kumeneko ndi kutuluka komanso kusiya chilengedwe chomwe unalengedwa nacho, ndi chifukwa zikunenedwa mu buku la "Muslim" momwe muli nkhani yochokera kwa Mulungu, yomwe Mulungu akuyankhula mu nkhanimo kuti: “Ndipo ndithu ine ndidawalenga akapolo anga onse ndi chibadwa chokhulupilira Mulungu m'modzi, koma asatana adawatembenuza ndikuwachosa ku chikhulupiliro cha Mulungu m'modzi kuwapitisa ku zikhulupiliro zosochera” ([6]). Ndidawalenga akapolo anga kukhala okhulupirira Mulungu m'modzi:kutanthauza pa chilengedwe chokhulupilira umodzi wa Mulungu, kenako asatana anawabwelera ndikuwatembenuza powasiyisa chikhulupiliro chawo cholondola. ()Nkhani ikupezeka mu buku la Muslim (2865) mu nkhani yomwe ikunenedwa ndi Iyadhi mwana wa Himar al-Mujashi- Mulungu asangalasidwe naye.

Zinalembedwa mu mabuku a "Bukhar ndi Muslim",mu nkhani yomwe ikunenedwa ndi Abu Huraira-Mulungu asangalasidwe naye-amene adanena kuti Mtumiki wa Mulungu mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale kwa iye-adanena kuti: “Mwana aliyense amabadwa ali okonzeka kugonjera malamulo a Mulungu(kutsatira chipembedzo cha chisilamu),koma makolo ake ndi amene amamusandusa kukhala myuda,komanso mkhirisitu monga momwe nyama imaberekera mwana wake,mumaona chilema china chilichonse pa mwanayo? ndipo ndinu amene mumaipasa chilema nyamayo"[7]. Ndipo mu kuyankhula kwina: “Makolo ake amamupanga kukhala Myuda, Mkhirisitu, kapena opembedza moto, monga momwe nyama imaberekera nyama mwana wake ali okwanira ziwalo zonse; Kodi mumaona pa nyamayo ili yosakwanira ziwalo zake?” ([8] Nyamayo imatuluka m’mimba mwa mai ake yokwanira ziwalo zake, ili ndi makutu awiri athunthu ndi ziwalo zonse, ndipo ukadulidwa mwendo, kapena dzanja,kapena khutu, kapena chiwalo china chilichonse, maonekedwe amenewo sikuti ndi omwe chinalengedwera ai,koma kuti izi zimachitika chifukwa cha zochita za anthu pambuyo poti chinyamacho chinatuluka mmimba mwa kholo lake chili chokwanira ziwalo zake, Mtumiki wa Mulungu-mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa iye adati: "Ndipo inu ndamene mumachipanga kukhala ndi ziwalo zopunguka". Chimodzimodzi mwana wina aliyense amabadwa ali ndi chilengedwe chogonjera mwa Mulungu, ndiye ngati atasanduka Mkhirisitu, Myuda, Opembedza Moto, kapena kugwera mu mtundu ulionse osintha chikhalidwe,kusiya njira yolondola,kusochera ndi zinthu zoipa,zonsezi zimachitika chifukwa cha makolo awiri kapena dera lomwe wabadwira ndikukulira. Ikupezeka mu buku la Bukhar (6599). Ikupezeka mu mabuku a Bukhar(1358) ndi Muslim (2658).

Ndipo anyamata pakati pathu amakula*** pazimene makolo awo ankawazoloweza.

Mtumiki -mtendere ndi madalitso zikhale pa iye-adati: "Makolo ake ndi amene amamupanga kukhala Myuda, kapena Mkhirisitu, kapena opembedza moto". Mtumiki sananene kuti: “makolo ake awiri amumapanga kukhala msilamu”chifukwa choti adabadwa ali msilamu kale, choncho chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndicho chikhulupiliro chogwirizana ndi chibadwa cha munthu. Tsono mchitidwe omuphatikiza Mulungu ndi makhalidwe ena monga kusokonekera,zinthu za bodza zonsezi zimasusana ndi kumasemphana ndi chilengedwe chomwe munthu analengedwa nacho. Sono kugwirizana kwake ndi mzeru zoongoka chifukwa mzeru, zoongoka ndizimene sizinapatuke kapena kusokonekera, ndipo sizisangalatsidwa ndi china chilichonse kupatula kupembedza Mulungu m'modzi ndipo savomereza china chilichonse kupatula kukhulupilira Mulungu mmodzi, ndi ndani amene ali ndi nzeru zomagwira bwino ntchito amene angamakondwe ndi kuchuluka kwa milungu, kapena moyo wako munthu kuyezamira ku zinthu zomanga kapena dothi. (Yusuf-mtendere ukhale pa iye-adayankhula kuwafunsa anzake omwe adalowa nawo limodzi ku ndende kuti kodi milungu yosiyanasiyana ndi yabwino kapena Mulungu m'modzi yekha amene mphamvu zake zimaposa kalikonse{39}. Zomwe mukuzipembedza pa mbali pa Mulungu oyenera kupembedzedwa ndi maina chabe opanda matanthauzo omwe inu munawatcha pamodzi ndi makolo anu mwa umbuli komanso mosokera, ndipo Mulungu sadavumbulutse umboni osonyeza kulondola pa zomwe mumazipembedza kusiya iye Mulungu m'modzi). [Surah Yusuf:39-40].

Pa nthawi yomwe Zaidu mwana wa Amru mwana wa Nufail- m'modzi mwa okhulupilira za umodzi wa Mulungu mu nthawi yomwe chisilamu chinali chisanabwere- adasiya chipembedzo cha anthu ake adayankhula kuti:([9]): ( ) “Al-Seerah” olemba Ibn Ishaqa (2/96).

Kodi mbuye ndi mmozi kapena ambiri okwana chikwi***nditsatire ngati zinthu zagawikana

Ndawasiya Al-Lat ndi Al-Uzza, izo ndi zomwe amachita munthu wopilira.

Sindikhulupilira umulungu wa Uza kapena ana ake achikazi awiri*** kapena mafano a mtundu wa Amri ndi Adiru.

“Iye ankanyazitsa mchitidwe wa ma Quraysh omazinga zinyama posakhala mu dzina la Mulungu ponena kuti: “mbudzi yoti adailenga Mulungu ndipo adai madzi kuchokera ku mwamba ndikumeresera nsipu kuchokera pansi pa nthaka kenako mukumaizinga posakhala mu dzina la Mulungu-kuwazuzula pa mchitidwe amachitawo komanso pofuna kumukweza ndikumulemekeza Mulunguyo”([10]). ()“Sahih Al-Bukhar ”(3826)

Mu nzeru za munthu, palibe chinthu chomwe chili chofotokozedwa bwino kwambiri komanso choonekera kwambiri chomwe munthu amachidziwa kuposa kukwanira kwa mbiri za Mlengi wa zolengedwa zonse, ndikumuyeresa ku mbiri zonse zochitisa manyazi komanso zomwe ndi zopunguka,ndikumupatula iye pomugonjera iye yekha. Atumiki a Mulungu onse adabwera kudzawakumbutsa anthu za kufunika kodziwa zimenezi komanso kudzifotokoza motambasula bwino kwa anthu,komanso kufotokoza za ubwino wa umodzi wa Mulungu ndikuipa komuphatikiza Mulungu ndi zinthu zina ndi zinthu zokhazikika mu nzeru ndi chilengedwe chabwino cha munthu, zimenezi ndi zodziwika kwa munthu aliyense amene ali ndi mtima wa moyo(omagwira ntchito),komanso nzeru zomagwira ntchito bwino ndi chilengedwe chabwino.

Mfundo Yachisanu ndi Chiwiri: Chimodzi mwa zizindikiro za chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndi choti ubale wapakati pa anthu okhulupilira Mulungu mmodzi umakhala weni weni komanso opitilira pa dziko pano komanso moyo omwe ukubwera, ndipo palibe ubale omwe ukupezeka pakati pa anthu ofanana ndi ubale obwera kamba kokhulupilira umodzi wa Mulungu; chifukwa choti ubale umenewu omwe umakhala pakati pa anthu okhulupilira za umodzi wa Mulungu, ndi ubale omwe uli opitilira pa dziko pano komanso moyo omwe ukubwera. (Abwenzi omwe amathandizana pa zinthu zomulakwira Mulungu,tsiku la chiweruzo akadzitalikisa wina ndi nzake pa tsikulo, koma abwenzi omwe amachezerana ndikumalangizana zoopa Mulungu,ubwenzi wawo umakhala opitilira pa dziko pano komanso ukapitilira tsiku lotsiriza)[67]. [Surah Az-Zukhruf:67] Mu ndime ina,Mulungu akuyankhula kuti: (Pomwe anthu omuphatikiza Mulungu ndi zinthu zina adzaone zilango pa tsiku lotsiriza,anthu omwe atsatidwa mu zochita zawo za dziko la pansi, chipembedzo akazitalikisa ndi anthu omwe amawatsatira pa zinthu zimenezo). [Surah Al-Baqarah:166] Mgwirizano uliwonse ndi kulumikizana; Kulumikizana kulikonse ndi kokutha, chikondi chilichonse ndi chokutha, ndipo kulumikizana kulikonse ndi kokutha,kupatula chikondi ndi ubale komanso kulumikizana komwe kumakhala pokhulupilira mwa Mulungu ndi umodzi wake, chilichonse chomwe chimachitika chifukwa cha Mulungu, chimakhala chopitilira ndi cholumikizana mpaka kale, ndipo chomwe chimakhala pa chinthu china osati Mulungu,sichimapitilira komanso chomaduka ndikusiyana,ubale ngakhale utakhala wa mphamvu chotani kapena wakuya chotani,ngati suli kamba ka Mulungu umatha ndikuduka pa dziko lino kapena moyo omwe ukubwera-popanda chikaiko-kupatula ubale omwe umakhala kamba kokhulupilira umodzi wa Mulungu ndikukhulupilira mwa ubwino za umodzi wa Mulungu, ndi ubale omwe umakhala opitilira mpaka kale kale pa dziko pano komanso moyo omwe ukubwera udzakhala opitilira.

12. Mfundo yachisanu ndi chitatu: Mu zizindikiro zina za chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu, ndi kudalirika komanso kupanda zolakwika kwa komwe chikhulupilirochi chimatengedwa. Chikhulupiliro chimenechi chimatengedwa kuchokera mu zoyankhula zozuna komanso zopanda zolakwika zilizonse, zochokera mu buku la Mulungu mwini kuzikweza, ndi zochita za Mtumiki wake-mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa iye-amene sayankhula za mmutu mwake koma kuti zonse zimachokera kwa iye zimakhala kuti zachokera kwa Mulungu,ndipo gawo ili lisanthulidwabe.

Mfundo yachisanu ndi chinayi: Zina zizindikiro za umodzi wa Mulungu ndi kukhazikika ndikutetezedwa,-Mulungu-mwini ulemelero-adalonjeza zoteteza chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu chi komanso kutetedza chipembedzo cha Chisilamu ndikuchichita kukhala chopitilira,Mulungu akuyankhula kuti: (Mulungu ndi amene adamutumiza Mtumiki wake Muhammad-mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa iye- ndi buku la Quran komanso chipembedzo cha Chisilamu; ndi cholinga choti chikhale pa mwamba pa zipembedzo zonse, ngakhale anthu opembedza mafano chitawanyasa chipembedzo cha Chisilamu ndikukhala kwake pa mwamba pa zipembedzo zina)[33]. [Surah Al-Taubah:33], Mulungu-wapamwamba-akuyankhula kuti: (Ndithudi Mulungu amawateteza anthu okhulupilira ku udani wa anthu okanira komanso chiwembu cha anthu oipa). [Al-Hajj:38], Mulungu-mwini ulemelero-akuyankhula kuti: (Tidazipanga kukhala zokakamizidwa pa ife kuwathandiza ndikuwateteza anthu okhulupilira ndikutsatira Atumiki a Mulungu ndipo tidadzichita zimenezo kukhala mu gulu la ma ufulu awo ndipo tidawalonjeza zowathandiza,choncho zingoyenera kuchitika)[47] [Surah Ar-Rum:47] Mulungu-wapamwamba-akuyankhula kuti: (Mulungu amawalimbikitsa anthu okhulupilira ndi mau achilimbikitso,omwe ndi: oikira umboni za umodzi ndikuyenera kopembedzedwa kwa Mulungu mmodzi ndikutinso Muhammad ndi Mtumiki wa Mulungu, ndi zomwe adabwera nazo Mtumikiyo mu malamulo achipembedzo amawalimbikitsa nawo pa dziko la pansi pano,komanso pa nthawi yomwe akumwalira powafewesera kuti atsirize moyo wawo ndi ntchito zabwino, ndipo akalowa mmanda amawalimbikitsa pa nthawi yomwe akufunsidwa mafunso a mmanda ndi angelo awiri powapasa mayankho olondola). [Ibrahim:27].

Mfundo ya Khumi: Zina mu zizindikiro za chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndikupezeka kwa zipatso zochuluka komanso maubwino ambiri ndi zotsatira zabwino zosiyanasiyana pa dziko la pansi pano ndi tsiku lomariza. Nkhani yokhuza zimenezi,ikambidwa ku mapeto kwa buku limeneli.

NKHANI YACHIWIRI:

MATANTHAUZO A TAUHID NDI ZOONA ZAKE ZENI ZENI.

TAUHID: mau ochokera ku mneni oti wagwirizanitsa,akugwirizanitsa,kugwirizanitsa, ndi tsinde lomwe limasonyeza umodzi wa chinthu.Kukhulupilira umodzi wa Mulungu ndikumupanga iye kukhala wa yekha ndikukana china chilichonse chomuphatikiza naye iye mu zoyenera kumuchitira komanso mbiri zake iyeyo, palibe chilichonse chophatikizana ndi iye mu mbiri zake, kapena mu zomwe walamulira akapolo ake kuti azimuchitira iye.

Kukhulupilira umodzi wa Mulungu pa zichitochito zake- ndikukhulupilira zoti iye Mulungu ndamene amayendesa kena kalikonse pa dziko pano,kuyambira kulenga zolengedwa,kupereka zosowa za zolengedwa,kupereka moyo,kupereka imfa komanso kuyendesa kena kalikonse. Izi zonsezi ndi zina zomwe amachita Mulungu yekha.

Maina Ake okongola, mbiri zake zapamwamba, chifuniro chimachitika monga wafunira, Kuthekera kokwanira, kuzindikira kwakwe kotambasuka,kukwanira kwake mu maina komanso mbiri zake ndi zina zomwe palibe amafanana nayenso,choncho munthu amene angachikire cholengedwa zina mwa mbiri kapena maina a Mulunguwa, chikhulupiliro chake pa umodzi wa Mulungu chimaonongeka.

Zoyenera akapolo kumuchitira Mulungu ndi kuti amupembedze iye yekha ndipo asamuphatikize ndi china chilichonse,monga mmene zikunenedwera mu nkhani yomwe ikuchokera kwa Muadh-Mulungu asangalale naye-amene akuti Mtumiki-mtendere ndi madalitso zikhale pa iye-adanena kuti: "E iwe Muadh! Kodi ukudziwa zoyenera akapolo kumuchitira Mulungu?Nanga zoyenera Mulungu kuwachitira akapolo akachita zoyenera kumuchitira Mulungu ndi ziti?" Muadh adati: ndidati: Mulungu ndi Mtumiki wake ndi amene akudziwa , Mtumiki adayankhula kuti: "zoyenera akapolo kumuchitira Mulungu ndikuti amupembedze iye yekha,ndikupewa kumuphatikiza ndi china chilichonse, ndipo zoyenera Mulungu kuwachitira akapolo ngati atachita zoyenera kumuchitira Mulunguyo, ndikuti asakamupase chilango munthu amene samamuphatikiza Mulungu ndi china chilichonse([11]) Ntchito ina iliyonse yabwino ndi yoyenera kuchitira pofuna kusangalasa Mulungu yekha; choncho munthu amene angagwire ntchito iliyonse yabwino pofuna kusangalasa wina osakhala Mulungu mmodzi,chikhulupiliro chake cha umodzi wa Mulungu chimaonongeka. ()Ikupezeka mu buku la Bukhar(2856, 5967) ndi Muslim (30).

Chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu: chimatanthauza kumupatula Mulungu posamuphatikiza ndi chili chonse mu zoyenera kumuchitira komanso mbiri zake. Kumuphatikiza Mulungu: zimatanthauza kumafananiza chomwe chisali Mulungu ndi Mulungu mu zoyenera kumuchitira Mulungu kapena mu mbiri zake. Ichi ndi choona cheni cheni cha chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu: tikuyenera kumupatula Mulungu ndikuti tisamuikire ophatikzana naye monga momwe Mulungu akuyankhulira: (Mudzipembedza Mulungu mmodzi yekha ndipo mudzimvera malamulo ake iye yekha, ndipo musamuikire ophatikizana naye mu zochita zake komanso popembedzedwa pake..) [Al-Nisa:36] Mulungu akuyankhula kuti: (Ndipo Mbuye wako-iwe munthu-walamulira kuti usapembedze Mulungu wina koma iye yekha....). [Al-Isra:23] Mulungu akuyankhula kuti: (Anthu omwe adalipo inu Asilamu musanabwere,sadalamuridwe mu malamulo awo onse koma kupatula kuti apembedze Mulungu mmodzi yekha pofuna kumusangalasa iye, ndikusiya kupembedza milungu ina..). [Al-Bayyinah:5] Mavesi okhala ndi matanthauza amenewa alipo ochuluka kwambiri.

Kudzera mu kufotokoza kwa mmwambamo,zikumveka kuti chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu chili magawo atatu: kukhulupilira za umodzi wa Mulungu pa zochita zake,kukhulupilira za umodzi wa Mulungu pa maina komanso mbiri zake ndi kukhulupilira za umodzi wa Mulungu popembedzedwa.

Tanthauzo la chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu pa zochita zake: kumeneko ndi kumpatula Mulungu wa mphamvu zonse pokhulupilira kuti iye yekha ndiye Mlengi, opereka zosowa za zolengedwa zonse, mwini chilichonse,opereka mtendere, amene amayendesa china chilichonse,opanda othandizana naye mu zochita zakezo, Mulungu akuyankhula kuti: (Nena-iwe Mtumiki-wauze anthu opembedza mafano kuti: kodi Mlengi wa mitambo ndi nthaka komanso amene amayendesa ziwirizi ndi ndani? Nena: Mulungu ndi amene ali Mlengi wa zimenezo komanso amene amaziyendesa). [Ar-Rad:16] Mulungu akuyankhula kuti: (Nena-iwe Mtumiki-wauze anthuwo kuti: kodi mwini wake nthakayi ndi onse akupezeka pa nthaka ndi ndani ngati muli ndi kuzindikira pa zimenezo)[84]. (Adzavomereza mopanda chikaiko kuti mwini wake ndi Mulungu kuti ndamene adadzilenga komanso ndamene ali mwini wake,choncho auze iwowo kuti: ndiye inu simungakumbukire kuti iye Mulungu ali ndikuthekera kuwadzusa anthu akufa tsiku lotsiriza?)[85]. (Nena kodi ndani amene ali Mbuye wa mitambo isanu ndi iwiri,komanso wampando wa ufumu omwe ndi waukulu kwambiri)[86]. (Adzanena mopanda chikaiko kuti zonsezi ndi za Mulungu,choncho nena kwa iwo kuti: ndiye simumaopa chilango chake mukamapembedza milungu ina kusiya iye?)[87]. (Nena: kodi mwini wa zinthu zonse ndi ndani?nanga mwini wa chuma chonse ndi ndani?Mulungu ndamene amatetedza wina aliyense ndipo palibe angamutetedze amene Mulungu wafuna kuti amuononge,ngati inu mukudziwa zimenezo)[88]. Adzanena kuti zonse ndi za Mulungu, choncho, nena kwa iwo kuti: nanga nzeru zanu zapita kuti,ndipo mukumanyengeka ndikumasiya kupembedza komanso kumvera Mulungu, ndikumakhulupilira zouka kwa akufa komanso kutuluka mmanda). [Surah Al-Muminun:84-89]. Mulungu akuyankhula kuti: (Mulungu amene anakupasani mtendere omwe muli nawo,ameneyo ndiye Mbuye wanu,zabwino zake ndi zochuluka,ndipo wayeresedwa ku zonse zosamuyenera iyeyo, iye ndi Mbuye wa zolengedwa zonse). [Surah Ghafir:64]. Mulungu akuyankhula kuti: (Mulungu ndi Mlengi wa zinthu zonse,Mbuye wa zonsezo,mwini wake,oyendesa kalikonse ndipo iye ndi mtetedzi wa chilichonse amene amayendesa zonse zokhuza zolengedwa zake). [Surah Az-Zumar:64]. Ndi mavesi ena.

Gawo lachiwiri: Kukhulupilira za umodzi wa Mulungu pa mayina ndi mbiri zake: Kumeneko ndi kumupatula Mulungu mwini ulemelero pokhulupilira zoti iye ali ndi mayina okongola komanso mbiri zapamwamba zomwe zikupezeka mu buku lake komanso zochita za Mtumiki wake, Mulungu akuyankhula kuti: (Mulungu iye ndi mmodzi yekha ndipo iye yekha ndi amene ali oyenera kupembedzedwa mwa choonadi,iye Mulungu ali ndi maina okongola ndi mbizi za pamwamba)[8]. [Surah Taha:8] Mulungu akuyankhula kuti: (Nena-iwe Mtumiki-wauze anthu kuti azimupempha Mulungu pogwiritsa ntchito dzina lililonse mu maina ake okongola-kaya loti Allah kapena Al-Rahman,dzina lililonse lomwe angagwiritse ntchito ndi lake Mulungu ndipo iye ali ndi maina okongola kwambiri). [Al-Isra:110] Mulungu akuyankhula kuti: (Iye ndi Mulungu amene palibe Mulungu wina oyenera kupembedzedwa mwa choonadi koma iye yekha,odziwa zinthu zobisika komanso zoonekera, iye ndi wa chisoni kwa zolengedwa zonse komanso akawachitira chifundo anthu okhulupilira tsiku lotsiriza powalowesa ku mtendere)[22]. (Iye ndi Mulungu opembedzedwa yemwe palibe wina opembedzedwa mwa choonadi koma iye yekha amene ndi mwini wa kena kalikonse mwini ulemelero ndikuyeresedwa ku zonse zoipa,mwini kupereka mtendere komanso opereka zozizwitsa kwa Atumiki kukhala maumboni akuyankhula kwawo zoona pa zomwe Mulungu watumiza nazo,amene amayang anira ntchito zonse za akapolo ake,wa mphamvu amene sagonjesedwa,amene ali pa mwamba pa zolengedwa zonse, mwini kuzitukumula ndi ulemelero,wayeresedwa Mulungu ku zonse zomwe opembedza mafano amamuphatikiza nazo)[23]. (Iye ndi Mulungu Mlengi wa zolengedwa zonse,amene amazipezekesa zolengedwa potengera ndi nzeru zake zakuya,amene amalenga zolengedwa ndikuzipasa maonekedwe omwe iye wafuna,Mulungu ali ndi maina okongola komanso mbiri zabwino,zonse zili ku mwamba komanso pansi pa mtambo zimamupembedza iye, iye ndi wa mphamvu amene amawalanga adani ake ndi chilango chachikulu akafuna kuwabwezera chipongwe,ndi wa nzeru zakuya pokonza zinthu zokhuza zolengedwa zake)[24]. [Surah Al-Hashr:22-24].

Gawo lachitatu: Chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu popembedzedwa komwe ndikukhulupilira za umodzi wa Mulungu popembedzedwa monga kumupempha,kukhala ndi chiyembekezo pa zabwino zochokera kwa iye, kumuopa,kukwaniritsa malonjezo,kuzinga zinyama,mapemphero,kusala kudya ndi zina zotero zomwe ndi gulu la ntchito zabwino, komanso kugwira ntchito pofuna kusangalasa iye yekha, ndikuzitalikitsa ku mchitidwe omuphatikiza iye ndi zinthu zina, monga momwe Mulungu akuyankhulira: (Ndipo iwo (Ayuda ndi Akhirisitu)mu malamulo awo onse sadalamuridwe kupatula kuti adzipembedza Mulungu mmodzi yekha pofuna kumusangalasa iye yekha ndikusiya kumuphatikiza ndi zinthu zina pomukhulupilira iye yekha). Mulungu akuyankhula kuti: (Dziwani kuti Mulungu yekha ndamene akuyenera kutsatiridwa malamulo ake popanda kuphatikizidwa ndi chilichonse) [Az-Zumar:3] Mulungu akuyankhula kuti: (Nena-iwe Mtumiki-wauze anthu opembedza mafano kuti: mapemphero anga,zozinga zanga zomwe ndimazinga pofuna kusangalatsa Mulungu yekha,osati mafano kapena anthu omwalira kapena ziwanda, kapena zina zotero zomwe inu mumazizingira kumusiya Mulungu,komanso osati mu dzina la Mulungu monga momwe mumachitira-moyo wanga komanso imfa yanga zonse zili mmanja mwa Mulungu Mbuye wa zolengedwa zonse)[162]. (Palibe amene ali bwenzi lake lophatikizana nalo popembedzedwa,mu zochita zake ngakhalenso mu maina komanso mbiri zake, chimenechi ndicho chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu chenicheni chomwe Mbuye wanga wandilamulira kuti ndizichitsatira). [Surah Al-An 'am:162-163] Mtumiki-mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa iye-adati: “Munthu wina aliyense amene angamwalire akumapempha wina osakhala Mulungu mmodzi yekha ndikumamufanizira Mulungu oyenera kupembedzedwa mwa choonadi ndi zinthu zina,akalowa kumoto tsiku lotsiriza” ([12]) Ichi ndi chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndipo zafotokozedwazi ndizo zoona za chikhulupiliro chimenechi. ()Nkhani imeneyi ikupezeka mu buku la Bukhar,nambala yake ndi (4497) ndipo mau awa ndi ake, komanso mu buku la Muslim, nambala yake ndi (92), yomwe ikuchokera kwa Abdul-Allah mwana wa Masoud-Mulungu asangalale naye.

Mtundu ulionse mu mitundu ya chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu, uli ndi chotsutsana nacho; “ngati wadziwa kuti chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu pa zochita zake zimatanthauza kuvomereza kuti Mulungu ndiye Mlengi, opereka zosowa za zolengedwa, opereka moyo, opereka Imfa, oyendesa zinthu zonse,ochita kena kalikonse pa zolengedwa zake,ndi kuti Iye alibe bwenzi lothandizana nalo mu ufumu wake; zotsutsana ndi chikhulupiliro chimenechi ndi kukhulupilira komwe kapolo angakhulupilire kuti pali amene amayendesa zinthu limodzi ndi Mulungu mu zinthu zomwe wina aliyense sangathe kupanga kupatula Mulungu yekha.

Ngati wadziwa kuti kukhulupilira za umodzi wa Mulungu pa maina ndi mbiri zake zimatanthauza kuti Mulungu azipemphedwa pogwiritsa ntchito maina omwe adazipatsa iye yekha, ndikufotokozedwa pogwiritsa ntchito mbiri zomwe iye mwini wazifotokoza nazo pamodzi ndi mbiri zomwe Mtumiki wake-mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa iye-adamufotokoza nazo, ndikukana kumufananiza ndi china chilichonse; chotsutsana ndi chikhulupiliro chimenecho ndi zinthu ziwiri, zomwe zikupezeka mu dzina loti"al-ilhad-kukana zoti Mulungu alipo":

Chimodzi mwa ziwirizo ndi: Kukana zoti Mulungu ali ndi maina komanso mbiri zabwino, ndikukana mbiri zosonyeza kukwanira kwa Mulungu, komanso zofotokozera ukulu wake zomwe ndi zotsimikizika mu buku la Quran komanso zochita za Mtumiki.

Chachiwiri chake: Kufanizira mbiri za Mulungu ndi mbiri za zolengedwa zake,kumachita kuti Mulungu akuyankhula kuti: (Palibe cholengedwa chomwe chimafanana ndi iye mu kaonekedwe kake,kapena mu maina ake kapena mu mbiri zake,iye ndi okumva komanso openya). [Surah As-Shura:11]. Mulungu akuyankhula kuti: (Mulungu amadziwa zomwe zili patsogolo pa anthu zokhuza tsiku lotsiriza komanso za m'mbuyo mwawo zokhuza dziko la pansi,ndipo zolengedwa sizimadziwa zokhuza Mulungu mmene Mulungu amaziziwira zolengedwa zake). [Twaha:110].

Ngati wadziwa kuti kukhulupilira za umodzi wa Mulungu popembedzedwa zimatanthauza kuti mitundu yonse ya ntchito zabwino ikuyenera kuchitidwa pofuna kusangalasa Mlungu yekha ,ndikukana kupembedza china chilichose posakhala Mulungu m'modzi opembedzedwa mwa choonadi-mwini ulemelero wamwambamwamba-; chotsutsana ndi chikhulupiliro chimenechi ndi kugwira ntchito ina iliyose yabwino mu mitundu ya ntchito zabwino pofuna kusangalasa amene si Mulungu m'modzi, kachitidwe kameneka ndiko komwe kachulukira mwa onse opembedza mafano,ndipo mkangano omwe umakhala pakati pa Atumiki ndi anthu awo gwero lake linali lopembedza milungu ina([13]). ()"Ma'rij-Al-qabul" lolembedwa ndi Sheikh Hafiz Al-Hakami (1/418).

Nkhani Yachitatu:

KUKWANIRITSA ZA CHIKHULUPILIRO CHA UMODZI WA MULUNGU

Kukwaniritsa zofunika kuchita za chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu zikapangisa munthu kukakhala malo a pamwamba ku minda ya mtendere,Mtumiki-mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa iye-adanena kuti anthu omwe angakwaniritse zofunika za chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu akalowa ku minda ya mtendere popanda kuwawerengera ntchito zawo kapena kupasidwa zilango zilizonse pa zochimwa zawo zing ono zing ono. Izi zikukambidwa mu nkhani yotchuka yomwe ikudzera kwa mwana wa Abbas ndi anthu ena -Mulungu asangalasidwe naye-amene adanena kuti Mtumiki-mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa iye-adanena kuti: (Mwa anthu omwe akalowe ku minda ya mtendere mukakhalanso anthu ena okwana sevente sauzande omwe akalowe ku minda ya mtendere popanda kuwerengeseredwa ntchito zawo komanso popanda kupasidwa zilango kamba ka machimo ang ono ang ono). Kenako anawatchula m'mau ake oti: (Anthu omwe akalowe ku minda ya mtendere popanda kuwerengeseredwa ntchito zawo ngakhale kulangidwa,samadzipemphelera okha,komanso samawapempha ena kuti awapemphelere,komanso sakhulupilira zoti mbalame zimatha kubweretsa mwai kapena tsoka,komanso samagwiritsa ntchito zisulo zamoto poziwambitsa pa thupi pawo,koma kuti iwo amayezamira mwa Mbuye wawo Mulungu mmodzi” ([14]) Awa ndi malo apa mwamba omwe akakhale anthu okhulupilira kweni kweni za umodzi wa Mulungu komwe ndikukwaniritsa koyenera za umodzi wa Mulungu. ()Nkhani ikupezeka mu buku la Bukhar ndipo nambala yake (5705) komanso mu buku la Muslim ndipo nambala yake ndi (220).

Tanthauzo lokwaniritsa chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndi loti: kukwaniritsa chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndikuchiyeretsa chikhulupilirocho ku zonyasa zomuphatikiza nazo Mulungu,zinthu zopeka komanso machimo. Zinthu zitatu zimenezi,anthu ophunzira amazitchula kuti ndi: zotchinga zomwe zimamutchinga munthu mu njira yake yoyenda popita kwa Mulungu komanso umoyo ukubwera: zotchinga zobwera kamba komuphatikiza Mulungu,zotchinga zobwera kamba kopeka zinthu mu chipembedzo komanso zotchinga zobwera kamba ka machimo.

Tsono chotchinga chobwera kamba komuphatikiza Mulungu ndi zinthu zina; njira yothanirana ndi vuto limeneli ndi kugwira ntchito pofuna kusangalatsa Mulungu mmodzi yekha, pomwe chotchinga chobwera kamba ka zopeka mu chipembedzo; njira yothanirana nalo vuto limenelo ndi kugwiritsitsa zochita za Mtumiki ndikumamutsatira Mtumiki-mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa iye-ndikumatsatira njira yake, pomwe chotchinga chobwera kamba ka uchimo;njira yothanirana ndi vuto limenelo ndi kutalikirana ndikupewa machimowo komanso kulapa kwa Mulungu kulapa kweni kweni ngati munthu wachita machimo, ngati kapolo atafika pa khalidwe loteleri,amakhala kuti wakwaniritsa chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu.

Kukwaniritsa za chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu-kulinso-magulu awiri-kukwaniritsa kokakamizidwa ndikukwaniritsa kosakakamizidwa, anthu onse amagulu awiriwa akalowa ku minda ya mtendere tsiku la chiweruzo popanda kuwerengesedwa ntchito zawo ngakhalenso kulangidwa:

Gulu loyamba la anthu okwaniritsa chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu: ndi gulu la anthu ochita zomwe Mulungu wakakamiza ndikupewa zomwe waletsa. Ngati kapolo ali otere,ochita zomwe Mulungu wakakamiza ndikumapewa zomwe Mulungu waletsa mu machimo ndi sambi zikulu zikulu; kapolo ameneyo amakhala wakwaniritsa chinthu chokakamizidwa cha chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndipo amakhala gulu la anthu omwe amachita zomwe Mulungu wakakamiza ndikumasiya zomwe Mulungu waletsa, ndipo amenewa ndi ena mwa omwe akalowe ku minda ya mtendere popanda kuwerengeseredwa kapena kulangidwa, ili ndi gulu limodzi.

Gulu la chiwiri, ndi gulu lomwe lili lapamwamba kuposa loyamba ndipo ndi la anthu oti: amakwaniritsa chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu chomwe sichokakamizidwa lomwe ndi gulu la anthu okangaza pogwira ntchito zabwino. Amenewa ndi anthu omwe amasunga ndikuikira mtima pogwira ntchito zomwe Mulungu wakakamiza komanso amakhala akutalikira machimo akulu akulu ndi zinthu zoletsedwa, ndipo amakhala akupikisana pogwiranso ntchito zosakakamizidwa.

Anthu amenewa ndi magulu awiri omwe amakhala kuti akwaniritsa za chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu-anthu ochita zomwe Mulungu wakakamiza ndi kumapewa zomwe Mulungu waletsa komanso anthu omwe amakhala akukangaza pogwira ntchito zabwino-onsewa akalowa ku minda yaku mtendere tsiku lotsiriza popanda kuwerengeseredwa ntchito zawo kapena kulangidwa,Mulungu akuyankhula kuti: (Kenako tidawapasa-pambuyo powonongeka kwa mibado yomwe idalipo-buku la Quran anthu omwe tidawasankha ochokera mu gulu la Muhammad-mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa iye-: ena mwa iwo ndi anthu ochita zoipa, ena ochita zomwe Mulungu walamulira ndikumapewa zomwe waletsa, ndipo ena mwa iwo ndi ofulumiza pogwira ntchito yabwino zokakamizidwa komanso zosakakamizidwa,kupasidwa buku limeneli ndikusankhidwa kwa gulu limeneli ndi ubwino waukulu ochokera kwa Mulungu)[32]. Minda yaku mparadiso momwe akakhalemo mpaka kale kale anthu omwe Mulungu adawasankha ndikuwapasa buku lake la Quran). [Surah Fatir:32-33]. Kutanthauza kuti: magulu atatu a wanthu akalowa ku minda ya mtendere: omwe anali okhulupilira omwe adali ndi machimo okhululukidwa nawo,omwe amatsatira malamulo a Mulungu ndikumapewa zomwe walesa ndi omwe adali ofulumira pogwira ntchito zabwino zokakamizidwa komanso zosakakamizidwa.

Tsono munthu amene amachita zomwe Mulungu wakakamiza ndikumapewa zomwe waletsa ndi munthu amene amafulumira kuchita ntchito zabwino; kulowa kwawo ku minda ya mtendere kukakhala kulowa koyambilira popanda kuwerengesedwa kena kalikonse.

Pomwe munthu amene amagwira yoipa pochita machimo omwe sali gulu lomuphatikiza Mulungu, munthu ameneyo akalowa ku minda yaku mtendere,koma sakalowa kulowa koyambilira popanda kuwerengesedwa ntchito zake kapena popanda kulangidwa monga momwe zikakhalire ndi munthu amene amachita zomwe Mulungu amakakamiza ndikumapewa zomwe Mulungu amaletsa ndi munthu amene amafulumira pogwira ntchito yabwino; koma kuti munthu ameneyu akapasidwa kaye chilango ndikuwerengesedwa ntchito zake,ndipo munthu ameneyu akakhala pansi pa chifuniro cha Mulungu ,akakafuna Mulungu akampasa chilango akakafunanso akamukhululukira machimo ake kenako ndikumulowesa ku minda ya mtendere.

NKHANI YACHINAYI:

ZINTHU ZOONONGA NDI KUPUNGULA CHIKHULUPILIRO CHA UMODZI WA MULUNGU

Chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu chili ndi zomwe zimaononga ndi kupungula; ndipo zinthu zoononga chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndi zomwe zimaononga ntchito yabwino ndikuononganso chipembedzo chonse cha munthu.Kumeneko ndikukanira mwa Mulungu pomuphatikiza ndi zinthu zina,umthira kuwiri weni weni,kukanira mwa Mulungu ndi mitundu yokanira,umthira kuwiri waukulu ndi mitundu yake,zonsezi ndi zinthu zowononga chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu. Kumuphatikiza Mulungu pochita mtundu waukulu ndi mitundu yake ya mchitidwewu,kukanira mwa Mulungu pochita mtundu waukulu ndi mitundu yake,umthira kuwiri waukulu ndi mitundu yake,zonsezi zimaononga chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu,Mulungu akuyankhula kuti: (Ndithu anthu amene amazionesera ngati okhulupilira ndikumabisa kukanira kwawo mwa Mulungu,tsiku la chiweruzo akakhala pansi pa moto waku gahena) [Al-Nisa:145], Mulungu-wapamwamba-akuyankhula kuti: (Ndipo munthu amene angakanire malamulo a Chipembedzo,ntchito imaonongeka). [Al-Maidah:5], Adanenanso Mulungu wapamwamba: (Ndithu zabvumbulutsidwa kwa iwe-ee! Mtumiki-komanso kwa Atumiki omwe adabwera iwe usanabwere mau oti: ngati utamuphatikiza Mulungu ndi zinthu zina ntchito zako zizaonongeka ndipo udzakhala gulu la anthu owonongeka pa chipembedzo chako komanso umoyo ukudza ukakhala gulu la oluza chifukwa ntchito yabwino yogwiridwa momuphatikiza Mulungu ndi zinthu zina simalandiridwa). [Surah Az-Zumar:65]. Chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu chimaonongeka ndi mchitidwe omuphatikiza Mulungu ndi zinthu zina kudzera mu mitundu yonse yomuphatikira Mulungu,komanso kudzera mu mchitidwe wa mthira kuwiri waukulu ndi mitundu yake ndikukanira mwa Mulungu kwa mtundu waukulu ndi mitundu yake yonse. Kukamba ndi kufotokoza za zomwe zalemebedwazi nkhani yake ikhala yaitali.

Tsono zinthu zopungula kukwanira kwa chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu zimenezo ndi zinthu zimene zimapungula kukwanira kwa chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu koma si zimawononga chikhulupilirocho kapena ndipo sizimaononga tsinde la chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu; zina mwa zimenezi ndi kukanira mwa Mulungu kwa mtundu wa ung' ono,umthira kuwiri pogwira ntchito,monga zomwe zili mu zoyankhula za Mtumiki: “Zizindikiro za munthu wa mthira kuwiri zilipo zitatu: pamene akuyankhula amanama, akalonjeza samakwaniritsa malonjezo, ndipo akasungisidwa chinthu amachita chinyengo” ([15]). Zinthu zopungula kukwanira kwa chikhulupiliro cha umodzi wa Mulunguzi, zikangopezeka mwa kapolo wa Mulungu,chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu chimapunguka, chimodzimodzinso kumuphatikiza Mulungu ndi mtundu omuphatikizira Mulungu wa ung ono,mau omwe amakhala oti muli kumuphatikiza Mulungu ndi zinthu zina omwe amakhala kuti munthu sakutanthauza zomwe akuyankhulazo koma zimangochitika kuti wawayankhula,izinso zimapungula chikhulupiliro chake pa umodzi wa Mulungu. Koma ngati munthu atakhulupilira zoona za mau amene wayankhulawo,amakhala kuti mauwo ali mu gulu la mtundu wa ukulu omuphatikizira Mulungu omwe amaononga chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu. ()Nkhani imeneyi ikupezeka mu buku la Bukhar(33) ndi Muslim (58) yomwe ikuchokera kwa Abu Hurairah.

Pa chifukwa chimenechi, ndi zofunika kwa munthu wina aliyense okhulupirira kuti akhale ochisamala chikhulupiliro chake cha umodzi wa Mulungu ndikumachiteteza pochitalikitsa chikhulupilirocho ndi zonse zowononga ndikupungula kukwanira kwake.

Sheikh Abdul Rahman mwana wa Hassan adati :“Dziwa kuti chinthu chotsutsana ndi chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndi mchitidwe omuphatikiza ndi Milungu ina; ndipo mchitidwe umenewo uli magulu atatu: mchitidwe waukulu omuphatikiza Mulungu,mchitidwe wa ung'ono omuphatikiza Mulungu, ndi mchitidwe obisika omuphatikiza Mulungu.

Umboni wa kuopsa kwa mchitidwe waukulu omuphatikiza Mulungu ndi zinthu zina, ndi mau ake a Mulungu onena kuti: (Ndithudi Mulungu sakakhuluka mchimo lomuphatikiza iye ndi zinthu pa tsiku la chiweruzo koma akakhululuka kwa amene wamfuna machimo ena osakhala omuphatikiza ndi zinthu zina,ndipo munthu amene angamuphatikize Mulungu ndi zinthu zina,amakhala kuti watalikirana ndi choona kutalikirana kwakukulu). [Surah Al-Nisa:116]. Mulungu akuyankhula kuti: (Mulungu wanena kuti Mesiya adayankhula kwa ana a Israil kuti: pembedzani Mulungu mmodzi yekha amene alibe ophatikizana naye,inu ndine pomupembedza Mulungu ndi chimodzimodzi, ndithudi munthu amene angapembedze Mulungu pomuphatikiza ndi china chilichonse,Mulungu waletsa kwa Munthu ameneyo kukalowa ku minda ya mtendere tsiku lomariza, ndikuti malo ake omwe akafikire ndi kumoto, ndipo anthu omuphatikiza Mulungu ndi zinthu zina sakapeza pa tsikuli athandizi ku zilango za Mulungu). [Surah Al-Maidah:72].

Ili ndi mitundu inayi:

Mtundu woyamba: mchitidwe omuphatikiza Mulungu popempha, umboni wake wa mtundu umenewu ndi mau ake a Mulungu: (Anthu okanira mwa Mulungu akakwera chombo chomwe chimayenda pa nyanja, ndipo akuopa kumira m'madzi,amakhulupilira Mulungu mmodzi ndikumamupempha iye yekha popanda kumuphatikiza ndi milungu ina,koma akawapulumutsa kupita ku mtunda ndi kuwachotsera vuto lomwe lidapeza, amabwelera kuyamba kumuphatikiza Mulungu ndi zinthu zina). Pongofuna kuti pamapeto pake akanire mtendere omwe tawapatsa iwowo komanso mu chuma chawo, ndikufuna kukwaniritsa kusangalala kwawo pa moyo wa dziko lino,pompanopa adzadziwa kuipa kwa ntchito zawo komanso zilango zowawa zomwe Mulungu wakonzera tsiku lotsiriza) [Surah Al-Ankabut:65-66].

Mtundu wachiwiri:kuphatikiza Mulungu mu cholinga, chomwe ndi: chifuniro ndi cholinga, ndipo umboni wake ndi kunena kwa Mulungu Wamphamvu zonse: (Amene akufuna moyo wa dziko lapansi ndi zokometsera zake, tiwapatsa pompo pa dziko lapansi malipiro a zochita zawo mokwanira ndipo iwo m’menemo sachepetseredwa chilichonse). Iwo ndi omwe sadzakhala ndi kanthu tsiku lotsiriza koma Moto basi,ndipo zimene adachita m’menemo zidzaonongeka, ndiponso zikakhala zopanda phindu zimene ankachita). [Surah Hud:15-16].

Mtundu wachitatu: Kumuphatikiza Mulungu pomvera, ndipo umboni wake ndikunena kwa Mulungu koti: (Ayuda ndi Akhirisitu adawapanga anthu ophunzira ndi opemphera kwambiri mwa iwowo kukhala milungu yawo yowapangira malamulo ndikumatsatira malamulo oikidwa ndi anthu amenewo ndikumasiya osasatira malamulo a Mulungu, ndipo adamusandusa Mesiya-Yesu mwana wa Mariya kukhala Mulungu ndikumamupembedza kumachita kuti Mulungu sadawalamule onsewo zopembedza milungu ina koma mmodzi yekha amene ndi Mulungu oyenera kupembedzedwa mwa choonadi,wayeresedwa Mulungu ku zomwe anthu omuphatikiza Mulungu ndi zinthu zina komanso kusochera amapakhala akumunamizira). [Surah At-Taubah:31]. Tanthauzo lake lomwe lilibe vuto ndi lakuti: Kuwamvera ophunzira ndi opembedza ponyoza Mulungu, osati kuwapempha anthuwo, monga momwe Mtumiki-mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa iye-adatanthauzilira pomuza a Adiy mwana wa Hatim pamene iye adamfunsa Mtumikiyo, ndipo adati poyankha: "Ife sitimawapembedza iwowo, choncho adamuuza kuti kuwapembedza kwa iwowo kuli powamvera zoyankhula zawo pa zinthu zonyoza malumulo a Mulungu.

Mtundu Wachinayi: kumuphatikiza Mulungu pa chikondi, ndipo umboni wake ndikunena kwa Mulungu koti: (Ndi maumboni omveka bwinowa,gulu lina la anthu limawapanga mafano komanso anthu olungama kukhala ofanana ndi Mulungu, ndikumawakonda,kuwalemekeza ndikumawamvera,zomwe sizoyenera kumuchitira wina aliyense posakhala Mulungu mmodzi. Pomwe anthu okhulupilira mwa Mulungu,amamukonda kwambiri Mulungu kuposa anthu okanirawo ndi milungu yawo; chifukwa choti anthu okhulupilira amamukonda Mulungu mwa chiyero,pomwe enawo amamukonda Mulungu momuphatikiza ndi zina,akadadziwa anthu opembedza mafano pa dziko lapansi,pomwe akaone zilango pa tsiku lotsiriza ndikuti Mulungu yekha ndi amene ali ndi mphamvu zonse, ndikuti zilango za Mulungu ndi zopweteka,sakadaika milungu ina pambali pa Mulungu mmodzi ndikumaipembedza ndikuziyandikisa kwa Mulungu kuzera mu timilunguyo). kufika mau ake oti: (Ndipo iwo sadzatulukanso ku Moto)[167] [Surah Al-Baqarah:165-167].

Mtundu wachiwiri: Kumuphatikiza Mulungu ndi mtundu wa ung' ono: kumuphatikiza Mulungu ndi mtundu wa ung ono,kumeneko ndikuzionesera pogwira ntchito yabwino kuti anthu akutamandile, umboni wake ndi mau a Mulungu oti: (Kwa munthu amene amaopa chilango cha Mbuye wake ndikumayembekezera malipiro a bwino kuchokera kwa Mbuye wakeyo,akuyenera kumagwira ntchito yabwino pomusangalasa Mbuye wakeyo mogwirizana ndi malamulo ake, ndipo sakuyenera kumuphatikiza Mulungu ndi china chilichonse pomwe akugwira ntchito yabwino). [Surah Al-Kahf:110].

Mtundu wachitatu: Kumuphatikiza Mulungu pogwira ntchito yobisika,umboni wake ndi mau a Mtumiki-mtendere ndi madalitso zikhale pa iyeyo: “Mchitidwe omuphatikiza Mulungu ndi zinthu zina mu gulu la anthu ili udzakhala obisika kwambiri kuposa nyerere yokuda yomwe yabisala pamwala okuda pa nthawi yomwe kuli mdima wa usiku” Ndipo kufafaniza kwake ndi kuyankhula mau a Mtumiki-mtendere ndi madalitso zikhale pa iye-onena kuti: "Allahumma 'inni 'audhu bika' an 'ushrika bika shay'an waana 'aelamu, wa'astaghfiruka min aldhanbi alladhi la 'aelamu". Tanthauzo lake: Ambuye Mulungu ndikuzitchinjiriza mwa inu kuti ndisakuphatikizeni ndi kena kalikonse kumachita kuti ine ndikuziwa, komanso ndikupempha chikhululuko ku zochimwa zomwe ndapanga ndisakuziwa».

Kusakhulupilira kuli mitundu iwiri:

Kusakhulupirira komwe kumatulutsa munthu m'Chisilamu, ndipo kuli mitundu isanu:

Mtundu Oyamba: Kusakhulupilira kotsutsa, ndipo umboni wake ndi mau ake a Mulungu: (Palibe munthu ochimwisisa kuposa amene wamupekera Mulungu bodza,kenako ndikumayankhula kuti bodzalo lachokera kwa Mulungu,kapena amene amatsutsa choona chomwe Mulungu adamutumiza nacho Mtumiki wake Muhammad-mtendere ndi madalitso zikhale pa iye-,ndithudi ku moto wa tsiku lotsiriza ndi komwe akafikire anthu okanira Mulungu,ndikumakanira umodzi wake ndikumatsutsa zomwe zidabwera ndi Mtumikiyo). [Surah Al-Ankabut:68].

Mtundu Wachiwiri: kukanira pozitukumula ndikukana koma utavomereza, umboni wake ndi mau a Mulungu oti: (Tawauze-iwe Mtumiki-anthuwo za ulemelero omwe Mulungu adamulemekeza nawo Adam pa nthawi yomwe Mulungu adawauza Angelo kuti: mgwadireni Adam pomulekeza pofuna kuonesa ubwino omwe ali nawo,Angelo onse adamvera kupatula Satana adakana zopereka ulemu kwa Adam kamba kozikweza ndi nsanje, ndipo adali gulu la okanira mwa Mulungu ndi onyoza malamulo ake). [Surah Al-Baqarah:34].

Mtundu Wachitatu: kukanira kokaikira, komwe ndi kukanira kopenekera kosasimikiza ,ndipo umboni wake ndi mau a Mulungu oti: (Ndipo adalowa m’munda mwake uku akudzichitira yekha zoipa pokanira zuwuka kwa akufa ndipo zomera zake zidamusangalasa ndikuyankhula mau oti: sindikukhulupilira kuti munda uwu ungaonongeke mpaka kale kale)[35]. Ndiponso sindikukhulupilira kuti kuli tsiku lotsiriza,ndipo ngati zitakhala kuti tsiku lotsiriza lilipodi-monga momwe ukuganizira iwe okhulupilira-ndipo ndikuchitikadi kuti ndabwelera kwa Mbuye wanga Mulungu, ndikapeza zabwino kuposa munda uwuwu potengera ndi ulemelero omwe ndili nawo pamaso pa Mulunguyo)[36]. Nzake amene adali okhulupilira adamuyankhula -pomwe iye amamulangiza mkati mokambirana kwawo-: zitheka bwanji iwe kukanira mwa Mulungu amene adakulenga iwe kuchokera ku dothi,kenako kudzera ku madzi a mamuna ndi mkazi,kenako ndikukutcha iwe kuti ndi munthu amene ali okwanira mu kalengedwe kake)[37]. [Surah Al-Kahf:35-37].

Mtundu Wachinayi: kukanira pozitalikitsa ndi chipembedzo, ndipo umboni wake ndi kuyankhula kwa Mulungu koti: (Anthu omwe adakanira zoti Mulungu ndiye opembedzedwa mwa choonadi,zomwe buku la Quran lawachenjeza iwo amazitalikitsa nazo,samamvera ulaliki wake ngakhale kulingalira). [Surah Al-Ahqaf:3]

Mtundu Wachisanu: kukanira kwa umthira kuwiri,ndipo umboni wake ndikunena kwa Mulungu: (Zimenezo ndi chifukwa choti iwowo adakhulupilira mowonesera,kenako ndikukanira mu mtima mwawo, ndipo zotsatira zake ndi zoti Mulungu adatseka mitima yawo kamba kokanira kwawoko,iwo samamvesesa china chili chonse chomwe chingawathandize iwowo). [Surah Al-Munafiqun:3].

Ndipo mtundu wakusakhulupilira komwe ndi kwakung ono, sikumamutulusa munthu mu chipembedzo,kumeneko ndi : kukanira mtendere omwe Mulungu wakupasa,umboni wa zimenezi ndi mau a Mulungu oti: (Mulungu wafanizira mzinda wa Makkah ndi mudzi omwe eni ake adalibe mantha a china chilichonse,zosowa zawo zimawapeza mosavutikira kuchokera mbali zosiyasiyana, ndipo anthuwo adakanira mtendere wa Mulungu pomukana Mtumiki,kuikana Quran ndipo Mulungu adawalipira powapatsa njala,mantha pa zomwe iwo adali kuchita). [Al-Nahl:112] Komanso mau a Mulungu oti: (Ndithu munthu amachulusa kuzipondereza yekha,ochulutsa kukanira mtendere wa Mulungu omwe wamupasa). [Surah Ibrahim:34].

Tsono umthira kuwiri: uli magulu awiri: umthira kuwiri wapa chikhulupiliro , ndi umthira kuwiri wapa zochita.

Chinyengo cha Chikhulupiliro:

Ili mitundu isanu ndi umodzi:

Kumutsutsa Mtumiki, kapena kutsutsa zina mwa zimene adadza nazo Mtumiki, kapena kuipidwa ndi Mtumiki, kapena kuipidwa ndi zomwe Mtumiki adabwera nazo, kapena kukondwera ndi kupita pansi kwa chipembedzo cha Mtumiki, kapena kunyasidwa ndi kupambana kwa chipembedzo cha Mtumiki; mitundu isanu ndi umodzi imeneyi, munthu amene angamachite zimenezi akakhala pansi pa moto-tikudzitchinjiriza mwa Mulungu ku mchitidwe onyoza ndi wa mthira kuwiri.

Tsono za chinyengo cha zichitochito:

Chili mitundu isanu:

"Pa nthawi yomwe akuyankhula amanama, akamakangana amatukwana,akalonjeza malonjezo amachita chinyengo, akasungisidwa chinthu amasokoneza,akalonjeza amaswa malonjezo;Mulungu ndiye mwini kudziwa"([16]) ( ) “Al-Durar Al-Sunniyah” (3/66).

Nkhani Yachisanu:

KOMWE CHIPHUNZITSO CHA CHIKHULUPILIRO CHA UMODZI WA MULUNGU CHIMATENGEDWA

Chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndi chipembedzo cholondola komanso chikhulupiriro champhamvu chochokera mu buku la Mulungu ndi zochita za Mtumiki wake-madalitso ndi mtendere wa Mulungu zikhale pa iye-, ndi chipembedzo chokhacho chimene mau a Mulungu chidatsika nacho kuchokera ku mwamba, ndipo zikhulupiliro zonse zomwe anthu ali nazo zimasiyana ndi kususana ndi chikhulupiliroc cha umodzi wa Mulungu; zimenezo ndi zikhulupiliro zochokera pa dziko la pansi pano zomwe adaziyambisa ndikuzipeka anthu, pomwe chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu, ndi chikhulupiliro chokhacho chomwe chidasika kuchokera kumwamba kuzera mu uthenga wa Mulungu, chimenecho ndi chipembedzo cha Mulungu chomwe iye adasangalasidwa nacho powasankhira akapolo ake,Mulungu akuyankhula kuti: (Ndipo ndasangalala kukusankhirani Chisilamu kukhala chipembedzo chanu). [Al-Maidah: 3] Mulungu akuyankhula kuti: (Kwa munthu amene angafune chipembedzo china osati cha Chisilamu chomwe ndikugonjera mwa Mulungu pokhulupilira za umodzi wake komanso ndikumamutsata pomvera malamulo ake, ndikukhala kapolo wa iye yekha,komanso pomumvera Mtumiki wake otsiriza Muhammad-mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa iye-pomukhulupilira ndikumutsatira ndikumukonda mowonesera komanso mobisa,chipembedzo chinacho sakalandiridwa nacho kwa Mulungu, ndipo tsiku lotsiriza akakhala mu gulu la anthu oluza). [Surah Al-Imran:85] Mulungu akuyankhula kuti: (Palibe wina aliyense amene angasiye kutsatira chipembedzo cha Ibrahim(Abraham)-chomwe ndi chisilamu-kupatula amene ali osagwira mutu ndi mbuli, ndithudi ife tidamusankha Ibrahim pa dziko pano kukhala Mtumiki komanso Mneneri, ndipo moyo omwe ukubwera akakhala gulu la anthu olungama omwe akakhale ku malo apa mwamba ku mtendere). [Al-Baqarah:130] Mulungu akuyankhula kuti: (Ndithudi chipembedzo chovomerezeka pamaso pa Mulungu ndi Chisilamu). [Al-Imran:19] Chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ,ndi chivumbulutso chomwe chidavumbulutsidwa kuchokera kwa Mulungu kupita kwa akapolo ake, ndi chipembedzo cha Mulungu chomwe pa chifukwa chake Mulungu adalenga zolengedwa ndi cholinga chokwaniritsa cholingachi, ndi chifukwa chake mau tikamba tanthauzo la mau a Mulungu oti: (Tidatumiza Atumiki ku mibado yonse yomwe idalipo omwe amawalamulira kuti azipembedza Mulungu mmodzi yekha ndikumapewa kupemmbedza Satana,mafano ndi anthu omwalira omwe anthu amawatenga kukhala abwenzi a Mulungu). [An-Nahl:36] (Chawandikira chikonzere cha Mulungu chokubwereserani chilango chanu-inu anthu okanira-choncho musapemphe kuti chilangocho chifulumira kubwera nthawi yake isanakwane,wayeresedwa Mulungu ku zomwe amamuphatikiza nazo[1]. (Mulungu amatsitsa Angelo ndi uthenga wake kupititsa kwa Atumiki ake omwe wafuna kuchokera mwa akapolo ake kuti awachenje anthu zakuopsa komuphatikiza Mulungu ndikuti palibe wina oyenera kupembedzedwa mwa choonadi koma ine, choncho mudzindiopa)[2]. [Surah An-Nahl:1-2].

Pomwe zikhulupiliro zina zomwe si zokhuza umodzi wa Mulungu, ndi zochokera pa dziko pompano zochita kuyambisidwa ndi anthu, ndi chifukwa chake Atumiki a Mulungu akafuna kuwonesa kusokonekera kwa zikhulupiliro zomwe anthu ali nazo monga kumuphatikiza Mulungu ndi zina,kukanira za umodzi wa Mulungu, umthira kuwiri ndi zina zotero mu mitundu yakusokera amagwiritsa ntchito njira yowafotokozera kuti zomwe akusatirazo Mulungu sanabvumbulutse mau alionse pa zimenezo,talongosola kale mau omwe Yusuf adawauza anzake awiri omwe adalowa nawo limodzi mu ndende: (Kodi kupembedza milungu yolengedwa yosinasiyana ndi zabwino kapena kupembedza Mulungu mmodzi yekha amene ali wa mphamvu kuposa kalikonse?[39]. Simukupembedza zina posiya Mulungu oyenera kupembedzedwa posakhala maina opanda matanthauzo,zomwe inu ndi makolo anu mwazika kukhala milungu kamba ka umbuli ndikusokera komwe muli nako,Mulungu sadatumize umboni osonyeza kuyenera kopembedzedwa zimenezo) [Surah Yusuf:39-40]. Mulungu Wamphamvuzonse adati mu Surah An-Najm: (Tandiuzeni za mafano anu omwe inu mwapasa maina oti Allata ndi Al-Uzza omwe mukuti mwawatenga mu maina a Mulungu[19] Ndi fano lina lachitatu lotchedwa Manata[20]. Kodi mukuzikira ana achimuna ndikumamuikira Mulungu ana achikazi?[21] (Kagawidwe kameneko ndi kopanda chilungamo)[22]. Mafano amenewa angokhala maina omwe alibe mbiri zokwanira ,koma ndi maina chabe omwe munawatcha inu ndi azibambo anu potengera zilakolako zanu zosokonekera,Mulungu sanabvumbulutse mau oikira umboni zomwe mukuyankhulazo). [Surah Al-Najm:19-23]. Naye Mtumiki Hud-mtendere ukhale pa iye- adati kwa anthu ake: (Kodi mukukangana nane pa mafano omwe inu ndi makolo anu mwawatcha ndikuwachita kukhala milungu ,zomwe Mulungu sadazisisire umboni; chifukwa ndi zolengedwa zomwe sizipereka vuto kapena kuthandiza,amene ali oyenera kupembedzedwa mwa choonadi ndi Mlengi mmodzi yekha, Choncho, dikirani kutsika kwa chilango cha Mulungu painu,ine ndudikira nanu limodzi kutsika kwa chilangocho)[71]. [Al-Araf:71].

Tsinde ndi gwero la kukhulupirira Mulungu mmodzi ndi buku la Mulungu Wamphamvu zonse ndi zochita za Mneneri wake-madalitso ndi mtendere zikhale pa naye-,zotengedwa ku gwero lokoma limeneli ndi kasupe woyera; pomwe zikhulupiriro zomwe anthu ali nazo gwero lake ndi: mwina ndi zomwe malingaliro awo ovunda amawalamulira ndi malingaliro awo ovunda amafunikira, kapena ndi chivumbulutso chochokera ku ziwanda zawo zopanduka. “Ndipo chivumbulutso chili m’mitundu iwiri: chivumbulutso chochokera kwa wachifundo chambiri, ndi chivumbulutso chochokera kwa Satana.” Mulungu Wamphamvu zonse adati: (Ndithudi, asatana ochokera mu ziwanda amawauza abwenzi awo ochokera mwa anthu kuti abweretse chikaiko pa lamulo loletsa kudya nyama yofa yokha,ndipo amawalamula kuti awauze Asilamu potsutsana nawo mau oti: inu posadya kwanu nyama yofa yokha ndiye kuti mukusiya osadya chomwe wapha Mulungu, ndipo mmalo mwake mukumadya zomwe mwazinga inu nokha,choncho ngati mutawatsatira iwowo-inu Asilamu pozichita kukhala zololedwa nyama zafa zokha-ndiye kuti inu ndi iwowo mukhala ofanana pa mchitidwe umenewu). [Surah Al-An 'am:121]. Mulungu akuyankhula kuti: (Momwe takuyesera iwe mayeso-ee Mtumiki-kudzera mwa adani ako ochokera mwa anthu opembedza mafano, ndi momwenso tidawayesera Atumiki onse-mtendere ukhale pa iwo-kudzera mwa adani ochokera mwa anthu ndi a Satana, ndikumauzana mau oipa omwe amawakongoletsa ndi mau abwino; ndi cholinga chomunyenga amene akumva mauwo) [Al-An’am:112] Mulungu akuyankhula kuti: (Kodi ndikuzeni-ee inu anthu-za munthu amene Satana amatsika kwa iye)[221]. [Surah As-Shu'ara: 221]. Mwana wa Al-Mukhtar mwana wa Abi Ubaid ali gulu limeneli, zinanenedwa kwa mwana wa Umar ndi wa Abbas,zinanenedwa kwa mmodzi mwa ana awiriwa kuti: Al-Mukhtar akuyankhula kuti mau a Mulungu akumabvumbulutsidwa kwa iye; ndipo adati: (Ndithudi a Satana ochokera mu ziwanda amawauza abwenzi awo ochokera mwa anthu kuti azitsutsana nanu) Ndipo kudanenedwa kwa winayo:akumanena kuti mau a Mulungu akumatsitsidwa kwa iye; ndiye adati: (Kodi ndikuzeni-ee inu anthu-za munthu amene Satana amatsika kwa iye)([17]). ( ) "Majmu’ Al-Fatawa"- Lolembedwa ndi Ibn Taymiyyah (13/75).

Satana amawauza anthu omwe osokera za zikhulupiriro, malingaliro,amawanong oneza, ndi maganizo amene amawakhulupilira kuti ndi owona, ndipo kenako amawaitanira anthu kwa iwo kudzera mu chivumbulutso chimene Satana adawatsitsira, kapena zinthu zimene munthu amazifikira chifukwa cha kukoma kwake koipa. Kenako, kuchokera m’menemo mumatuluka zochita, kulambira, ndi miyambo, zimene iye akunena poperekera umboni mu zimenezo kuti: “Tidaziyesa,” kapena “ma shehe athu anaziyesa.” Chipembedzo sichichokera pa zochitika. Kapena zochita zomwe amatenga ku maloto; akunena kuti: “Ndinaona zakuti m’maloto anga,” ndipo amamangapo chipembedzo kapena chikhulupiriro, ndi zina zotero kuchokera ku magwero amene anthu ambiri amachokerako zikhulupiriro zimene Mulungu Wamphamvu zonse sanazivumbulutsirepo umboni uliwonse.

Choncho, chikhulupiriro chodalitsika ndi kukhulupilira Mulungu mmodzi, chomwe ndi chipembedzo cha Mulungu Wamphamvuzonse, chipembedzo chimene Mulungu savomereza chipembedzo chilichonse koma chokhacho. Ndi chikhulupiriro chochokera ku gwero lokoma ndi kasupe woyera. Aliyense amene amamwa kuchokera ku gwero loyamba ndi kasupe wotsekemera adzapeza magwero otsala a chipwirikiti ndi oipitsidwa. Komabe, munthu sadziwa kuipitsidwa kwa magwero amenewa pokhapokha atadziwa gwero loyera ndi lokoma, lomwe ndi chivumbulutso ndi kutsitsa kwa Mulungu Wamphamvuzonse. Ichi nchifukwa chake Amushirikina ambiri, pambuyo pa chiongoko chawo ndi kulowa mu Umulungu m'modzi, amazindikira kuti iwo adali anthu osalingalira, pomwe pa nthawi ya kusokera kwawo, kupembedza milungu yambirimbiri, ndi bodza lawo, ankaganiza kuti ichi ndi kulingalila kolondola ndi chipembedzo choongoka.

Ichi ndi chifukwa chake ena mwa ophunzira a Mtumiki amakhala nthawi zina ndi kutchula nkhani zawo zachilendo pamene iwo adali opembedza mafano ndikuyamika Mulungu yemwe adawatsogolera ku Chisilamu ndi kupembedza Mulungu m'modzi. Kuchokera kwa Abu Uthman Nahdi yemwe adalipo kale Chisilamu chisanadze ndipo adalowa m’Chisilamu m’nthawi ya Mtumiki-mtendere ndi madalitso zikhale pa iye-koma osamuona, adati: “Ife tidali kupembedza mwala m’nthawi ya Umbuli, ndipo tidamva oitana akuitana: “E, inu anthu apaulendo! Mbuye wanu waonongeka; kutanthauza kuti: mwala omwe adali kuupembedza wasowa, Adati: “tidatuluka panjira iliyonse yovuta ndi yophweka, ndipo tidamva woitana akuitana: “tampeza Mbuye wanu, kapena china chofanana ndi Iye, adati: “tidadza ndipo padali mwala, ndipo tidaphera ngamira pamwamba pake ngati mwala umenewo, kapena pafupi ndi iwo; nzeru za anthu awa zili pati?! ()Nkhani ikupezeka mu buku la Ibn Abi Shaybah mu buku lake la “Musannaf” (33914), ndi Ibn Sa’d mu buku la “Al-Tabaqat Al-Kubra” (7/97), ndi Abu Nu’aim mu buku la “Ma’rifat Al-Sahaba” (4707), ndipo anthu omwe adalandira nkhani imeneyi ndi yabwino.

Komabe, panthawi ya zochita ndi machitidwe amenewa, amawafotokoza Aneneri ndi Atumiki a Mulungu Wamphamvu zonse kuti ndi amisala ndipo amadziona iwo kuti ndi oganiza bwino. Komabe, ngati Mulungu Wamphamvu zonse adzaunika m’maganizo mwawo za chikhulupiriro cha umodzi wa Mulungu ndi kuongolera mitima ku Chisilamu chimenechi, zidzaonekera kwa munthu kuti zimene opembedza mafano ali nazo ndi zowonongeka ndi kuti magwero amene akuwadalira ndi oipitsidwa ndi bodza lililonse ndi kusokera, ndipo zidzaonekera poyera kuti aliyense wopembedza mafano ndi oipitsitsa maganizo.

Nkhani ya Chisanu ndi Chimodzi:

PHINDU NDI ZOTSATIRA ZA CHIKHULUPILIRO CHA UMODZI WA MULUNGU

Chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu chili ndi zotsatira ndi phindu losawerengeka,taonani umboni wa zimenezo mu mau a Mulungu: (Kodi sukudziwa-iwe Mtumiki-mmene Mulungu waperekera fanizo la mau a chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu a (Lailaha illa Allah),wafanizira liwu limeneli ndi mtengo waukulu,omwe ndi wa zipatso za tende,mitsitsi yake yoti yalowa pansi pa nthaka, ndipo nthambi zake zili mmwamba mbali ya mtambo)[24]. Mtengo omwe umatulutsa zipatso zake nthawi yomwe Mulungu anaika kukhala yotulutsira zipatso zake). [Surah Ibrahim:24-25]. Kutanthauza zipatso zake ndi ubwino wake.

Zotsatira ndi phindu la chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu pa moyo wa munthu pa dziko lapansi komanso moyo omwe ukubwera zilibe malire komanso si zowerengeka,koma tiyankhula mau ofotokoza za ubwino wake mopanda kupatula:

Chilichonse chabwino chimene kapolo wapeza pa dziko lapansi ndi tsiku lomaliza, ndi choipa chilichonse chimene kapolo wapulumutsidwa nacho padziko lapansi ndi tsiku lomaliza, chimachokera ku zipatso ndi zotsatira za kupembedza Mulungu m'modzi. Ngati tizama mu tsatanetsatane wa zipatso ndi zotsatira za kupembedza Mulungu m'modzi, ndiye kuti chimodzi mwa zipatso zazikulu ndi zotsatira za kupembedza Mulungu mmodzi ndiko kukonza ndi kuyeretsa ntchito. Pakuti zochita, zilizonse zomwe zingakhale, ndi zilizonse zomwe zili, sizovomerezeka kwa wochita, ndiponso sizilandiridwa kwa iye popanda Kukhulupirira Mulungu mmodzi. Kukhulupirira Mulungu m'modzi ndiko kuchita monga maziko a nyumba komanso ngati mizu ya mitengo. Pachifukwa ichi, Mulungu Wapamwamba mwamba adati: (Ndipo kwa munthu amene angafune malipiro a moyo osatha pogwira ntchito yake yabwino, ndikumagwira ntchito zomwe Mulungu walamulira pokonzekera za moyo umenewo, ndikukhalanso munthu okhulupilira mwa Mulungu ndi malipiro ochuluka omwe akapeze kwa Mulungu,anthu amenewo ntchito zawo zikalandiridwa ndipo Mulungu amasungira malipiro a ntchito zimenezo,ndipo akapasidwa malipiro ake tsiku lomariza)[19] [Surah Al-Isra:19]. Ndipo Mulungu Wamphamvu zonse adati: (Kwa munthu amene angamagwire ntchito yabwino,mamuna kapena mkazi,ndikukhala okhulupilira mwa Mulungu ndi Mtumiki wake,pa dziko pano timukhazika umoyo wa bwino ndi odekha,ngakhale atakhala kuti ali ndi chuma chochepa, ndipo tsiku lomariza tikawalipira malipiro awo a bwino mofanana ndi ntchito zabwino zomwe amagwira pa dziko la pansi)[97]. [Surat An-Nahl:97]. Chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndi chomwe chimaipanga ntchito kukhala yondolola ndikuiyeretsa, zitakhala kuti munthu ali ndi ntchito yochuluka ;ntchito imeneyo singalandiridwe kupatula ngati ali ndi chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu,Mulungu akuyankhula kuti: (Chifukwa chomwe chidapangitsa kuti zopereka zawo zisalandiridwe ndi chifukwa choti iwowo adabisa mmitima mwawo khalidwe lawo lokanira mwa Mulungu ndi Mtumiki wake-Muhammad-mtendere ndi madalitso a Mulungu zikhale pa iye). [At-Taubah:54] Mulungu Wapamwamba adati: (Munthu amene angakanire malamulo a chikhulupiliro nchito yake imaonongeka) [Al-Maidah:5] Iye adati: (Ndithu kwavumbulutsidwa kwa iwe-ee Mtumiki-komanso kwa Atumiki omwe adatumizidwa iwe usanatumizidwe uthenga oti: ngati utamuphatikiza Mulungu ndi zinthu zina,ntchito yake idzaonongeka). [Az-Zumar:65]. Kukhulupilira za umodzi wa Mulungu zimapangisa ntchito kukhala yolondola,ndipo ntchito sikhala yolondola popanda chikhulupiliro chimenechi.

Chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndi chifukwa chopambana ndi ulemelero pa dziko la pansi komanso moyo ukubwera. (Anthu omwe mbiri zawo ndi zomwe zalongosoledwazi, ali pa dangalira lochokera kwa Mbuye wawo ndipo ndi anthu omwe akakhale opambana tsiku lotsiriza). [Surah Al-Baqarah:5]. Anthu okhulupirira Mulungu m'modzi ndi anthu oongoka ndi kupambana, ndipo kupambana ndi liwu lalikulu lomwe likunenedwa pakupeza zabwino. Opambana ndi amene wapeza zabwino zapadziko la pansi ndi tsiku lomariza, ndipo ubwino siupezeka kapena kupezedwa pa dziko la pansi ndi tsiku lomariza kupatula kupembedza Mulungu m'modzi yekha ndi kudzipereka kwa chipembedzo kwa Iye, ulemelero ukhale kwa Iye wapamwamba mwamba.

Zina mwa zipatso zokhulupirira Mulungu m'modzi ndi chifukwa chopezera ulemelero wa Mulungu ndi kukalowa ku Paradiso ya Mulungu, komanso ndi chifukwa chopulumukira ku chilango ndi mkwiyo wa Mulungu. Kwa amene adzakumane ndi Mulungu ali okhulupirira Mulungu mmodzi yekha, adzalowa ku Paradiso, ndipo amene adzakumane ndi Mulungu - Mulungu atitalikitse- ali omuphatikiza Mulungu ndi zinthu zina, adzalowa ku moto ndipo adzaikidwa m'menemo mpaka muyaya,Mulungu akuyankhula kuti: (Ndithudi Mulungu sakakhululuka kwa munthu amene angamwalire akumuphatikiza Mulungu,koma iye akamukhululukira munthu amene wamfuna ngati adamwalira akuchita machimo ena osakhala omuphatikiza Mulungu ndi zinthu zina). [Al-Nisa:48] Zotsatira za chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu, ndi kupambana pokalowa ku mtendere ndikupulumuka ku ng anjo ya moto.

Ngati wakwaniritsadi kukhulupilira Mulungu mmodzi ndi kuzindikira kokakamizika kapena kovomerezeka, ndiye kuti chipulumutso chake ndi chipulumutso chakukalowa ku Moto. Komabe, ngati iye adali okhulupirira mwa Mulungu m'modzi koma amachita machimo ndi kuphwanya malamulo ang ono ang ono osakhala kupembedza milungu yambiri, ndiye kuti chipulumutso chake ndi chipulumutso chosakhala ku moto mpaka kale kale;chifukwa palibe amene adzakhale kumoto mpaka kalekale kupatula omuphatikiza Mulungu, monga momwe nkhani yochokera kwa Mtumiki ikufotokozera: "Pa tsiku lotsiriza Mulungu adzalamula Angelo kuti atulutse kuchokera ku moto munthu wina aliyense amene sadali kumuphatikiza Mulungu ndi zinthu zina mwa anthu omwe Mulungu adzafune kuwachitira chisoni mwa omwe adali akuyankhula mau oti: palibe Mulungu opembedzedwa mwa choonadi koma Mulungu mmodzi yekha"([19]). ()Nkhani ikupezeka mu buku la Bukhar,nambala yake ndi (7437),komanso mu buku la Muslim ndipo nambala yake ndi(182) kuchokera mu nkhani yomwe ikudzera kwa Abu Hurairah.

China mwa zotsatira ndi phindu la chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndi choti: ndi njira imodzi yopezera mtendere wa mu mtima, ndipo potengera kukwanira,mphamvu ndikuonjezereka kwa chikhulupiliro chimenechi, mtima wa munthu umapezanso mtendere ofanana ndi mmene alili pa chikhulupiliro.

Mulungu akuyankhula kuti: (Kodi munthu amene Mulungu wamuwongola ndi Chisilamu ndikumakhala moyo wake akutsatira dangalira lochokera kwa mbuye wake ndikumamudziwa Mulungu ndi malamulo ake) [Az-Zumar:22] Mulungu akuyankhula kuti: (Munthu amene Mulungu wamufuna kuti amupepusire kuti atsatire njira yowongoka,amafewesa mtima wake ndikukonzekeresa zovomera choona, ndipo akafuna kuti amunyozese ndikuti asamupepusire kuti atsatire njira yowongoka,amaupanga mtima wake kukhala omangika kwambiri kuti avomereze choona,pokanika kuvomereza zoti choona achilandire monga momwe amakanikira kukwera kwa mwamba). [Al-An'am: 125] Chiwongoko ndi kukhulupilira za umodzi wa Mulungu ndi chifukwa chachikulu mu zifukwa zopezera mtendere wa mu mtima,pomwe kumuphatikiza Mulungu ndi zinthu zina,kusokera ndi zina mu zifukwa zazikulu zopangisa kukhala munthu osowa mtendere wa mu mtima.

Zotsatira komanso phindu la chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndi choti: Mulungu walonjeza anthu okhulupilira za umodzi wake za ulemelero,chipambano pa dziko lapansi,kuthekera kolamulira pa dziko ndi kukonza za umoyo wawo,Mulungu akuyankhula kuti: (Mulungu walonjeza za chipambano powalonjeza anthu okhulupilira mwa inu komanso amagwira ntchito zabwino kuti awachita kukhala alowa mmalo a malo a anthu opembedza mafano,ndikuwachita kukhala adindo madera amenewo,monga momwe adachitira ndi azimbuyawo omwe adali okhulupilira mwa Mulungu ndi Atumiki, ndikuti achichita chipembedzo chawo-chomwe ndi Chisilamu-chomwe Mulunguyo adasangalala powasankhira kukhala chipembedzo chawo-kukhala chipembedzo champhamvu , ndikuwasinthanisira mantha awo ndikuwapasa mtendere,ngati atamapembedza Mulungu mmodzi yekha,ndikumakhala olungama potsatira malamulo a Mulungu,ndikumapewa zomusakaniza Mulungu ndi zinthu zina,tsono kwa munthu amene angakanire pambuyo pa mitendere yonseyi,anthu amenewo ndi anthu ogamukira malamulo a Mulungu)[55] [Surah Al-Nur:55].

Ubwino wina wa chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu ndi oti: chikhulupiliro cha umodzi wa Mulungu chimatsegula khomo la zabwino,chisangalalo ndikudekha kwa kapolo wa Mulungu,Mulungu akuyankhula kuti: (Mulungu amawaongola anthu omwe mitima yawo imakhala pansi pokhulupilira kwawo za umodzi wa Mulungu komanso akamamukumbukira Mulungu mitima yawo imapeza mtendere ndikumadekha,dziwani kuti kuzera mukumvera malamulo a Mulungu,kumukumbukira,komanso kukhulupilira za malipiro omwe ali nawo kwa ogwira ntchito zabwino,mitima imakhala pansi ndikumapeza mpumulo)[28]. [Surah Ar-Rad:28]. Mulungu akuyankhula kuti: (Ndithu kwa munthu amene chingamufikire chiongoko komanso kufotokozera kwa malamulo kuchokera kwa ine, ndikumatsatira chiongoko ndikufotokozera kwa malamulo anga ndikumagwiritsa ntchito ziwiri zimenezo,adzakhala owongoka pa dziko la pansi ndipo tsiku lomariza sadzakhala ndi tsoka lokalangidwa ndi zilango za Mulungu)[123]. (Kwa munthu amene angasiye kundikumbukira ine,ndithudi moyo wa dziko la pansi ukhala wa mavuto-ngakhale zitamaoneka kuti iye ndi mmodzi mwa omwe ali ndi zabwino-, adzaphinjidwa mmanda mwawo ndikulangidwa mmenemo, ndipo tsiku lomariza tidzamusonkhanisa ali osapenya kuti asakathe kupenya umboni)[124]. [Surah Taha:123-124].

Pa mbuyo pa zonse zakambidwazi; zomwe takamba mu bukuli ndi nsichi zochepa zokhuza nkhani yaikulu yomwe imakambidwa mu bukuli, ndipo ndikupempha Mulungu kuti atipange kukhala opindula ku zomwe watiphunzitsa, ndikuti azipange zomwe watiphunzitsazo kukhala umboni okatithandiza osati kutika mmavuto, ndikuti ationgole ku njira yowongoka.

Ndipo Mulungu ndiye akudziwa bwino, ndipo madalitso ndi mtendere a Mulungu zikhale pa kapolo komanso Mtumiki wake, Mtumiki wathu Muhammad, aku banja lake ndi ophunzira ake onse.